< Yobu 22 >

1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
Da svarede Elifas, Themaniten, og sagde:
2 “Kodi munthu nʼkukhala waphindu kwa Mulungu? Kodi munthu wanzeru angamupindulire Iye?
Mon en Mand kan gavne Gud? nej; men han gavner sig selv, naar han handler klogelig.
3 Kodi Wamphamvuzonse akanapeza chabwino chotani iweyo ukanakhala wolungama? Kodi iyeyo akanapeza phindu lanji makhalidwe ako akanakhala angwiro?
Mon det er den Almægtige en Fordel, at du er retfærdig? og mon det er ham en Vinding, at du holder dine Veje fuldkomne?
4 “Kodi nʼchifukwa choti umamuopa, kuti azikudzudzula, kuti azifuna kukukokera ku mlandu?
Mon han af Frygt for dig skal overbevise dig og gaa i Rette med dig?
5 Kodi osati nʼchifukwa chakuti kuyipa kwako nʼkwakukulu? Kodi machimo ako si opanda malire?
Er ikke din Ondskab megen og ingen Ende paa dine Misgerninger?
6 Iwe unkawumiriza abale ako kuti akupatse chikole popanda chifukwa; umalanda anthu zovala zawo ndi kuwasiya amaliseche.
Thi du tog Pant af dine Brødre uden Føje og trak Klæderne af de nøgne.
7 Sunawapatse madzi anthu otopa, ndipo unawamana chakudya anthu anjala,
Du gav ikke den trætte Vand at drikke og nægtede den hungrige Brød.
8 ngakhale unali munthu wamphamvu, wokhala ndi malo akeake, munthu waulemu wake, wokhala mʼdzikomo.
Men den Mand, hvis Arm var stærk, han havde Landet, og den, hvis Person var anset, boede deri.
9 Ndipo akazi amasiye unawachotsa wopanda kanthu, ndipo unapondereza ana amasiye.
Du lod Enker fare tomhændede, og de faderløses Arme knustes.
10 Nʼchifukwa chake misampha yakuzungulira, nʼchifukwa chake tsoka ladzidzidzi lakuchititsa mantha,
Derfor er der Snarer trindt omkring dig, og Rædsel har hastelig forfærdet dig.
11 nʼchifukwa chake kuli mdima kuti sungathe kuona kanthu, nʼchifukwa chakenso madzi achigumula akumiza.
Eller ser du ikke Mørket og Vandfloden, som bedækker dig?
12 “Kodi Mulungu sali kutalitali kumwamba? Ndipo ona nyenyezi zili mmwamba kwambirizo, ona kutalika kwake pamene zililipo!
Er ikke Gud i den høje Himmel? og se de øverste Stjerner, hvor de ere høje!
13 Komabe iweyo ukunena kuti, ‘Kodi Mulungu amadziwa chiyani? Kodi Iye amaweruza mu mdima woterewu?
Derfor siger du: Hvad ved Gud? skulde han kunne dømme igennem Mørket?
14 Mitambo yakuda yamuphimba, kotero kuti Iye sakutiona pamene akuyendayenda pamwamba pa thambopo.’
Skyerne ere et Skjul for ham, at han ikke ser, og han vandrer omkring Himlenes Kreds.
15 Kodi iwe udzayendabe mʼnjira yakale imene anthu oyipa ankayendamo?
Vil du tage Vare paa Fortidens Vej, som de uretfærdige Folk have vandret paa,
16 Iwo anachotsedwa nthawi yawo isanakwane, maziko awo anakokoloka ndi madzi achigumula.
de, som reves bort, førend det var deres Tid, hvis Grundvold opløstes i en Strøm;
17 Anthuwo anati kwa Mulungu, ‘Tichokereni! Kodi Wamphamvuzonse angatichitire chiyani?’
de, som sagde til Gud: Vig fra os; og: Hvad den Almægtige vel skulde kunne gøre for dem.
18 Chonsecho ndi Iye amene anadzaza nyumba zawo ndi zinthu zabwino, choncho ine sindigwirizana ndi uphungu wa anthu oyipa.
Han havde dog fyldt deres Huse med godt; men de ugudeliges Raad er langt fra mig.
19 “Anthu olungama amaona kuwonongeka kwawo ndipo amakondwera; anthu osalakwa amangoseka, akamuona woyipa akulangidwa.
De retfærdige se det og glæde sig, og den uskyldige spotter dem:
20 Amanena kuti, ‘Ndithudi adani athu awonongeka ndipo moto wawononga chuma chawo!’
„Sandelig, vor Modstander er tilintetgjort, og Ild har fortæret deres Herlighed‟.
21 “Gonjera Mulungu kuti ukhale naye pamtendere; ukatero udzaona zabwino.
Kære, hold dig til ham, og hav saa Fred! deraf skal komme godt til dig.
22 Landira malangizo a pakamwa pake ndipo usunge mawu ake mu mtima mwako.
Kære, tag Lærdom af hans Mund, og læg hans Ord i dit Hjerte!
23 Ukabwerera kwa Wamphamvuzonse udzabwezeretsedwa; ukachotsa zoyipa zonse zimene zimachitika mʼnyumba mwako,
Dersom du vender om til den Almægtige, da bliver du bygget op igen, ja, naar du holder Uret langt fra dine Telte.
24 ndipo chuma chamtengowapatali nuchiona ngati fumbi, golide wa ku Ofiri numutaya ku miyala ya ku zigwa.
Og kast Guldet i Støvet og Ofirs Guld blandt Bækkens Stene:
25 Pamenepo Wamphamvuzonseyo adzakhala golide wako, siliva wako wamtengowapatali.
Saa skal den Almægtige være dit Guld, og han skal være dit kostbare Sølv.
26 Pamenepo udzakondwera naye Wamphamvuzonse ndipo udzakweza nkhope yako kwa Mulungu.
Thi da skal du forlystes ved den Almægtige og opløfte dit Ansigt til Gud.
27 Udzamupempha ndipo adzakumvera, ndipo udzapereka zimene unalonjeza.
Du skal bede til ham, og han skal høre dig, og du skal betale dine Løfter.
28 Chimene watsimikiza kuti uchite, chidzachitikadi, kuwala kudzakuwunikira pa njira yako.
Naar du beslutter en Ting, da skal den lykkes for dig, og Lyset skal skinne over dine Veje.
29 Pamene anthu agwetsedwa pansi, iwe nʼkunena kuti, ‘Akwezeni!’ Pamenepo Iye adzapulumutsa anthu oponderezedwa.
Naar man trykker dig ned, da siger du: Opad! og han skal frelse den, som slaar Øjnene ned.
30 Iye adzapulumutsa ngakhale munthu amene ndi wolakwa, ameneyo adzapulumutsidwa kudzera mʼkulungama kwako.”
Han skal fri endogsaa den, der ikke er uskyldig, og denne skal udfries ved dine Hænders Renhed.

< Yobu 22 >