< Yobu 22 >

1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
A odpovídaje Elifaz Temanský, řekl:
2 “Kodi munthu nʼkukhala waphindu kwa Mulungu? Kodi munthu wanzeru angamupindulire Iye?
Zdaliž Bohu silnému co prospěšný býti může člověk, když sobě nejmoudřeji počíná?
3 Kodi Wamphamvuzonse akanapeza chabwino chotani iweyo ukanakhala wolungama? Kodi iyeyo akanapeza phindu lanji makhalidwe ako akanakhala angwiro?
Zdaliž se kochá Všemohoucí v tom, že ty se ospravedlňuješ? Aneb má-liž zisk, když bys dokonalé ukázal býti cesty své?
4 “Kodi nʼchifukwa choti umamuopa, kuti azikudzudzula, kuti azifuna kukukokera ku mlandu?
Zdali, že by se tebe bál, tresce tě, mstě nad tebou?
5 Kodi osati nʼchifukwa chakuti kuyipa kwako nʼkwakukulu? Kodi machimo ako si opanda malire?
Zdali zlost tvá není mnohá? Anobrž není konce nepravostem tvým.
6 Iwe unkawumiriza abale ako kuti akupatse chikole popanda chifukwa; umalanda anthu zovala zawo ndi kuwasiya amaliseche.
Nebo jsi brával základ od bratří svých bez příčiny, a roucha z nahých jsi svláčel.
7 Sunawapatse madzi anthu otopa, ndipo unawamana chakudya anthu anjala,
Vody ustalému jsi nepodal, a hladovitému zbraňovals chleba.
8 ngakhale unali munthu wamphamvu, wokhala ndi malo akeake, munthu waulemu wake, wokhala mʼdzikomo.
Ale muži boháči přál jsi země, tak aby ten, jehož osoba vzácná, v ní seděl.
9 Ndipo akazi amasiye unawachotsa wopanda kanthu, ndipo unapondereza ana amasiye.
Vdovy pak pouštěl jsi prázdné, ačkoli ramena sirotků potřína byla.
10 Nʼchifukwa chake misampha yakuzungulira, nʼchifukwa chake tsoka ladzidzidzi lakuchititsa mantha,
A protož obkličuji tě osídla, a děsí tě strach nenadálý,
11 nʼchifukwa chake kuli mdima kuti sungathe kuona kanthu, nʼchifukwa chakenso madzi achigumula akumiza.
Aneb tma, abys neviděl, anobrž rozvodnění přikrývá tě.
12 “Kodi Mulungu sali kutalitali kumwamba? Ndipo ona nyenyezi zili mmwamba kwambirizo, ona kutalika kwake pamene zililipo!
Říkáš: Zdaž Bůh není na výsosti nebeské? Ano shlédni vrch hvězd, jak jsou vysoké.
13 Komabe iweyo ukunena kuti, ‘Kodi Mulungu amadziwa chiyani? Kodi Iye amaweruza mu mdima woterewu?
Protož pravíš: Jak by věděl Bůh silný? Skrze mrákotu-liž by soudil?
14 Mitambo yakuda yamuphimba, kotero kuti Iye sakutiona pamene akuyendayenda pamwamba pa thambopo.’
Oblakové jsou skrýše jeho, tak že nevidí; nebo okršlek nebeský obchází.
15 Kodi iwe udzayendabe mʼnjira yakale imene anthu oyipa ankayendamo?
Šetříš-liž stezky věku předešlého, kterouž kráčeli lidé marní?
16 Iwo anachotsedwa nthawi yawo isanakwane, maziko awo anakokoloka ndi madzi achigumula.
Kteříž vypléněni jsou před časem, potok vylit jest na základ jejich.
17 Anthuwo anati kwa Mulungu, ‘Tichokereni! Kodi Wamphamvuzonse angatichitire chiyani?’
Kteříž říkali Bohu silnému: Odejdi od nás. Což by tedy jim učiniti měl Všemohoucí?
18 Chonsecho ndi Iye amene anadzaza nyumba zawo ndi zinthu zabwino, choncho ine sindigwirizana ndi uphungu wa anthu oyipa.
On zajisté domy jejich naplnil dobrými věcmi, (ale rada bezbožných vzdálena jest ode mne).
19 “Anthu olungama amaona kuwonongeka kwawo ndipo amakondwera; anthu osalakwa amangoseka, akamuona woyipa akulangidwa.
Což vidouce spravedliví, veselí se, a nevinný posmívá se jim,
20 Amanena kuti, ‘Ndithudi adani athu awonongeka ndipo moto wawononga chuma chawo!’
Zvlášť když není vypléněno jmění naše, ostatky pak jejich sežral oheň.
21 “Gonjera Mulungu kuti ukhale naye pamtendere; ukatero udzaona zabwino.
Přivykejž medle s ním choditi, a pokojněji se míti, skrze to přijde tobě všecko dobré.
22 Landira malangizo a pakamwa pake ndipo usunge mawu ake mu mtima mwako.
Přijmi, prosím, z úst jeho zákon, a slož řeči jeho v srdci svém.
23 Ukabwerera kwa Wamphamvuzonse udzabwezeretsedwa; ukachotsa zoyipa zonse zimene zimachitika mʼnyumba mwako,
Navrátíš-li se k Všemohoucímu, vzdělán budeš, a vzdálíš-li nepravost od stanů svých,
24 ndipo chuma chamtengowapatali nuchiona ngati fumbi, golide wa ku Ofiri numutaya ku miyala ya ku zigwa.
Tedy nakladeš na zemi zlata, a místo kamení potočního zlata z Ofir.
25 Pamenepo Wamphamvuzonseyo adzakhala golide wako, siliva wako wamtengowapatali.
Nebo bude Všemohoucí nejčistším zlatem tvým, a stříbrem i silou tvou.
26 Pamenepo udzakondwera naye Wamphamvuzonse ndipo udzakweza nkhope yako kwa Mulungu.
A tehdáž v Všemohoucím kochati se budeš, a pozdvihna k Bohu tváři své,
27 Udzamupempha ndipo adzakumvera, ndipo udzapereka zimene unalonjeza.
Pokorně modliti se budeš jemu, a vyslyší tě; pročež sliby své plniti budeš.
28 Chimene watsimikiza kuti uchite, chidzachitikadi, kuwala kudzakuwunikira pa njira yako.
Nebo cožkoli začneš, budeť se dařiti, anobrž na cestách tvých svítiti bude světlo.
29 Pamene anthu agwetsedwa pansi, iwe nʼkunena kuti, ‘Akwezeni!’ Pamenepo Iye adzapulumutsa anthu oponderezedwa.
Když jiní sníženi budou, tedy díš: Jáť jsem povýšen. Nebo toho, kdož jest očí ponížených, Bůh spasena učiní.
30 Iye adzapulumutsa ngakhale munthu amene ndi wolakwa, ameneyo adzapulumutsidwa kudzera mʼkulungama kwako.”
Vysvobodí i toho, kterýž není bez viny, vysvobodí, pravím, čistotou rukou tvých.

< Yobu 22 >