< Yobu 21 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
А Йов відповів та й сказав:
2 “Mvetserani bwino mawu anga; ichi chikhale chitonthozo changa chochokera kwa inu.
„Уважно послухайте сло́во моє, і нехай бу́де мені це розра́дою вашою!
3 Ndiloleni ndiyankhule ndipo ndikatha kuyankhula munditonzetonze.
Перете́рпіть мені, а я промовля́тиму, — по промові ж моїй насміха́тися будеш.
4 “Kodi ine ndikudandaulira munthu? Tsono ndilekerenji kupsa mtima?
Хіба до люди́ни моє нарі́кання? Чи не мав би чого стати нетерпели́вим мій дух?
5 Ndipenyeni ndipo mudabwe; mugwire dzanja pakamwa.
Оберні́ться до мене — й жахні́ться, та руку на уста свої покладіть.
6 Ndikamaganiza zimenezi ndimachita mantha kwambiri; thupi langa limanjenjemera.
І якщо я згадаю про це, то жаха́юсь, і морозом пройма́ється тіло моє.
7 Chifukwa chiyani anthu oyipa amakhalabe ndi moyo, amakalamba ndi kusanduka amphamvu?
Чого несправедливі живуть, доживають до ві́ку, й багатством зміцня́ються?
8 Amaona ana awo akukhazikika pamodzi nawo, zidzukulu zawo zikukula bwino iwo akuona.
Насіння їх міцно стоїть перед ними, при них, а їхні наща́дки — на їхніх оча́х.
9 Mabanja awo amakhala pa mtendere ndipo sakhala ndi mantha; mkwapulo wa Mulungu suwakhudza nʼkomwe.
Доми їхні — то спо́кій від страху, і над ними нема бича Божого.
10 Ngʼombe zawo zazimuna sizilephera kubereketsa; ngʼombe zawo zazikazi sizipoloza.
Спинається бик його, і не даре́мно, — зачинає корова його, й не скидає.
11 Amatulutsa ana awo ngati gulu la nkhosa; makanda awo amavinavina pabwalo.
Вони випускають своїх молодя́т, як отару, а їх діти вибри́кують.
12 Amayimba nyimbo pogwiritsa ntchito matambolini ndi azeze; amakondwa pakumva kulira kwa chitoliro.
Вони голос здіймають при бубні та цитрі, і веселяться при звуку сопілки.
13 Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero ndipo amatsikira ku manda mwamtendere. (Sheol h7585)
Провадять в добрі свої дні, і сходять в споко́ї в шео́л. (Sheol h7585)
14 Koma anthuwo amawuza Mulungu kuti, ‘Tichokereni!’ Ife tilibe chikhumbokhumbo chofuna kudziwa njira zanu.
А до Бога говорять вони: „Уступи́ся від нас, — ми ж дорі́г Твоїх знати не хочем!
15 Kodi Wamphamvuzonseyo ndani kuti timutumikire? Ife tipindula chiyani tikamapemphera kwa Iyeyo?
Що таке Всемогу́тній, що бу́дем служити Йому? І що́ скориста́єм, як будем благати Його?“
16 Komatu ulemerero wawo suli mʼmanja mwawo, koma ine ndimakhala patali ndi uphungu wa anthu oyipa.
Та не в їхній руці добро їхнє, — дале́ка від мене порада безбожних...
17 “Koma nʼkangati kamene nyale ya anthu oyipa imazimitsidwa? Nʼkangati kamene tsoka limawagwera? Nʼkangati kamene Mulungu amawakwiyira ndi kuwalanga?
Як часто світи́льник безбожним згасає, і прихо́дить на них їх нещастя? — Він приділює в гніві Своїм на них па́стки!
18 Nʼkangati kamene iwo amakhala ngati phesi lowuluka ndi mphepo, ngati mungu wowuluzika ndi kamvuluvulu?
Вони будуть, немов та солома на вітрі, і немов та полова, що буря схопи́ла її!
19 Paja amati, ‘Mulungu amalanga ana chifukwa cha machimo abambo awo.’ Koma Mulungu amabwezera chilango munthuyo, kuti adziwe kuti Mulungu amalangadi.
„Бог ховає синам його кривду Свою“— та нехай надолу́жить самому йому, і він зна́тиме!
20 Mulole kuti adzionere yekha chilango chake, kuti alawe ukali wa Wamphamvuzonse.
Нехай його очі побачать нещастя його́, й бодай сам він пив гнів Всемогу́тнього!
21 Nanga kodi amalabadira chiyani zabanja lake limene walisiya mʼmbuyo, pamene chiwerengero cha masiku ake chatha?
Яке бо стара́ння його про роди́ну по ньому, як для нього число його місяців вже перелічене?
22 “Kodi alipo wina amene angaphunzitse Mulungu nzeru, poti Iye amaweruza ngakhale anthu apamwamba?
Чи буде хто Бога навчати знання́, Його, що й небесних суди́тиме?
23 Munthu wina amamwalira ali ndi mphamvu zonse, ali pa mtendere ndi pa mpumulo,
Оцей в повній силі своїй помирає, — увесь він спокі́йний та ми́рний,
24 thupi lake lili lonenepa, mafupa ake ali odzaza ndi mafuta.
діжки́ його повні були молока, а мі́зок косте́й його свіжий.
25 Munthu wina amamwalira ali wowawidwa mtima, wosalawapo chinthu chabwino chilichonse.
А цей помирає з душею огі́рченою, і доброго не спожива́в він,
26 Olemera ndi osauka omwe amamwalira ndi kuyikidwa mʼmanda ndipo onse amatuluka mphutsi.
та по́рохом будуть лежати обо́є вони, і черва́ їх покриє.
27 “Ndikudziwa bwino zimene mukuganiza, ziwembu zanu zomwe mukuti mundichitire.
Тож я знаю думки́ ваші й за́думи, що хочете кри́вдити ними мене.
28 Inu mukuti, ‘Kodi nyumba ya mkulu uja ili kuti, matenti amene munkakhala anthu oyipa aja ali kuti?’
Бож питаєте ви: Де́ князів дім, і де наме́т пробува́ння безбожних?
29 Kodi munawafunsapo anthu amene ali pa ulendo? Kodi munaganizirapo zimene iwo amanena?
Тож спитайтеся тих, що дорогою йдуть, а їхніх озна́к не зата́юйте:
30 Zakuti munthu woyipa amasungidwa chifukwa cha tsiku la tsoka, kuti amapulumutsidwa chifukwa cha tsiku la ukali wa Mulungu?
що буває врято́ваний злий в день загибелі, на день гніву відво́диться в за́хист!
31 Kodi ndani amadzudzula munthu wochimwayo? Ndani amamubwezera zoyipa zimene anachita?
Хто йому́ розповість у лице про дорогу його́? А коли наробив, хто йому́ надолу́жить?
32 Iye amanyamulidwa kupita ku manda ndipo anthu amachezera pa manda ake.
І на кладо́вище буде прова́джений він, і про могилу подбають.
33 Dothi la ku chigwa limamukomera; anthu onse amatsatira mtembo wake, ndipo anthu osawerengeka amakhala patsogolo pa chitanda chakecho.
Ски́би долини солодкі йому́, і тя́гнеться кожна люди́на за ним, а тим, хто попе́реду нього, — немає числа.
34 “Nanga inu mudzanditonthoza bwanji ine ndi mawu anu opandapakewo palibe chimene chatsala kuti muyankhe koma mabodza basi!”
І я́к ви мене потішаєте ма́рністю, коли з ваших ві́дповідей зостається сама тільки фальш?“

< Yobu 21 >