< Yobu 21 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Job svarade och sade:
2 “Mvetserani bwino mawu anga; ichi chikhale chitonthozo changa chochokera kwa inu.
Hörer dock till min ord, och låter säga eder;
3 Ndiloleni ndiyankhule ndipo ndikatha kuyankhula munditonzetonze.
Hafver tålamod med mig, att jag ock må tala; och görer sedan spott af mig.
4 “Kodi ine ndikudandaulira munthu? Tsono ndilekerenji kupsa mtima?
Månn jag handla med en mennisko, att min ande icke skulle härutinnan ångse varda?
5 Ndipenyeni ndipo mudabwe; mugwire dzanja pakamwa.
Vänder eder hit till mig; I skolen förundra eder, och måsten lägga handena på munnen.
6 Ndikamaganiza zimenezi ndimachita mantha kwambiri; thupi langa limanjenjemera.
När jag tänker deruppå, så förskräckes jag; och ett bäfvande kommer uppå mitt kött.
7 Chifukwa chiyani anthu oyipa amakhalabe ndi moyo, amakalamba ndi kusanduka amphamvu?
Hvi lefva då de ogudaktige, varda gamle, och växa till i ägodelar?
8 Amaona ana awo akukhazikika pamodzi nawo, zidzukulu zawo zikukula bwino iwo akuona.
Deras säd är säker omkring dem, och deras afföda är när dem.
9 Mabanja awo amakhala pa mtendere ndipo sakhala ndi mantha; mkwapulo wa Mulungu suwakhudza nʼkomwe.
Deras hus hafver frid för räddhåga, och Guds ris är icke öfver dem.
10 Ngʼombe zawo zazimuna sizilephera kubereketsa; ngʼombe zawo zazikazi sizipoloza.
Deras oxa släpper man till, ock missgår icke; deras ko kalfvar, och är icke ofruktsam.
11 Amatulutsa ana awo ngati gulu la nkhosa; makanda awo amavinavina pabwalo.
Deras unga barn gå ut såsom en hjord, och deras barn springa.
12 Amayimba nyimbo pogwiritsa ntchito matambolini ndi azeze; amakondwa pakumva kulira kwa chitoliro.
De fröjda sig med trummor och harpor, och äro glade med pipande;
13 Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero ndipo amatsikira ku manda mwamtendere. (Sheol h7585)
De varda gamle med göda dagar, och förskräckas som nogast ett ögnablick för helvetet; (Sheol h7585)
14 Koma anthuwo amawuza Mulungu kuti, ‘Tichokereni!’ Ife tilibe chikhumbokhumbo chofuna kudziwa njira zanu.
De dock säga till Gud: Gack bort ifrån oss; vi vilje intet veta af dina vägar;
15 Kodi Wamphamvuzonseyo ndani kuti timutumikire? Ife tipindula chiyani tikamapemphera kwa Iyeyo?
Ho är den Allsmägtige, att vi honom tjena skole? Eller hvad kan det båta oss, om vi löpe emot honom?
16 Komatu ulemerero wawo suli mʼmanja mwawo, koma ine ndimakhala patali ndi uphungu wa anthu oyipa.
Men si, deras ägodelar stå icke uti deras händer; derföre skall de ogudaktigas sinne vara långt ifrå mig.
17 “Koma nʼkangati kamene nyale ya anthu oyipa imazimitsidwa? Nʼkangati kamene tsoka limawagwera? Nʼkangati kamene Mulungu amawakwiyira ndi kuwalanga?
Huru varder de ogudaktigas lykta utsläckt; och deras förderf kommer öfver dem? Han skall utskifta jämmer i sine vrede.
18 Nʼkangati kamene iwo amakhala ngati phesi lowuluka ndi mphepo, ngati mungu wowuluzika ndi kamvuluvulu?
De skola varda såsom strå för vädret, och såsom agnar, hvilka stormen bortförer.
19 Paja amati, ‘Mulungu amalanga ana chifukwa cha machimo abambo awo.’ Koma Mulungu amabwezera chilango munthuyo, kuti adziwe kuti Mulungu amalangadi.
Gud förvarar hans barnom bedröfvelse; när han skall löna honom, då skall man förnimmat,
20 Mulole kuti adzionere yekha chilango chake, kuti alawe ukali wa Wamphamvuzonse.
Hans ögon skola se hans förderf, och af dens Allsmägtigas vrede skall han dricka.
21 Nanga kodi amalabadira chiyani zabanja lake limene walisiya mʼmbuyo, pamene chiwerengero cha masiku ake chatha?
Ty ho skall hafva behag till hans hus efter honom? Och hans månaders tal skall näppliga halft blifva.
22 “Kodi alipo wina amene angaphunzitse Mulungu nzeru, poti Iye amaweruza ngakhale anthu apamwamba?
Ho vill lära Gud, den ock dömer de höga?
23 Munthu wina amamwalira ali ndi mphamvu zonse, ali pa mtendere ndi pa mpumulo,
Denne dör frisk och helbregda, rik och säll.
24 thupi lake lili lonenepa, mafupa ake ali odzaza ndi mafuta.
Hans mjölkekar äro full med mjölk, och hans ben varda full med märg.
25 Munthu wina amamwalira ali wowawidwa mtima, wosalawapo chinthu chabwino chilichonse.
Men en annan dör med bedröfvada själ, och hafver aldrig ätit i glädje.
26 Olemera ndi osauka omwe amamwalira ndi kuyikidwa mʼmanda ndipo onse amatuluka mphutsi.
Och de ligga tillhopa med hvarannan i jordene, och matkar öfvertäcka dem.
27 “Ndikudziwa bwino zimene mukuganiza, ziwembu zanu zomwe mukuti mundichitire.
Si, jag känner väl edra tankar, och edor vrånga anslag emot mig.
28 Inu mukuti, ‘Kodi nyumba ya mkulu uja ili kuti, matenti amene munkakhala anthu oyipa aja ali kuti?’
Ty I sägen: Hvar är Förstans hus? Och hvar äro hyddorna, der de ogudaktige bodde?
29 Kodi munawafunsapo anthu amene ali pa ulendo? Kodi munaganizirapo zimene iwo amanena?
Talen I dock derom såsom meniga folket; och veten icke hvad de andras väsende betyder?
30 Zakuti munthu woyipa amasungidwa chifukwa cha tsiku la tsoka, kuti amapulumutsidwa chifukwa cha tsiku la ukali wa Mulungu?
Ty den onde varder behållen intill förderfvelsens dag, och intill vredenes dag blifver han.
31 Kodi ndani amadzudzula munthu wochimwayo? Ndani amamubwezera zoyipa zimene anachita?
Ho vill säga hvad han förtjenar, när man det utvärtes anser? Ho vill vedergälla honom hvad han gör?
32 Iye amanyamulidwa kupita ku manda ndipo anthu amachezera pa manda ake.
Men han varder bortdragen till grafvena, och man vaktar efter honom i högomen.
33 Dothi la ku chigwa limamukomera; anthu onse amatsatira mtembo wake, ndipo anthu osawerengeka amakhala patsogolo pa chitanda chakecho.
Bäckaslem behagar honom väl, och alla menniskor varda dragna efter honom; och uppå dem, som för honom varit hafva, är intet tal.
34 “Nanga inu mudzanditonthoza bwanji ine ndi mawu anu opandapakewo palibe chimene chatsala kuti muyankhe koma mabodza basi!”
Huru trösten I mig så fåfängt, och edor svar finnas dock orätt?

< Yobu 21 >