< Yobu 21 >
1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Отвещав же Иов, рече:
2 “Mvetserani bwino mawu anga; ichi chikhale chitonthozo changa chochokera kwa inu.
послушайте, послушайте словес моих, да не будет ми от вас сие утешение:
3 Ndiloleni ndiyankhule ndipo ndikatha kuyankhula munditonzetonze.
потерпите ми, аз же возглаголю, таже не посмеетемися.
4 “Kodi ine ndikudandaulira munthu? Tsono ndilekerenji kupsa mtima?
Что бо? Еда человеческо ми обличение? Или почто не возярюся?
5 Ndipenyeni ndipo mudabwe; mugwire dzanja pakamwa.
Воззревшии на мя удивитеся, руку положше на ланите.
6 Ndikamaganiza zimenezi ndimachita mantha kwambiri; thupi langa limanjenjemera.
Аще бо воспомяну, ужаснуся: обдержат бо плоть мою болезни.
7 Chifukwa chiyani anthu oyipa amakhalabe ndi moyo, amakalamba ndi kusanduka amphamvu?
Почто нечестивии живут, обетшаша же в богатстве?
8 Amaona ana awo akukhazikika pamodzi nawo, zidzukulu zawo zikukula bwino iwo akuona.
Семя их по души, чада же их пред очима.
9 Mabanja awo amakhala pa mtendere ndipo sakhala ndi mantha; mkwapulo wa Mulungu suwakhudza nʼkomwe.
Домове их обилнии суть, страх же нигде, раны же от Господа несть на них.
10 Ngʼombe zawo zazimuna sizilephera kubereketsa; ngʼombe zawo zazikazi sizipoloza.
Говядо их не изверже: спасена же бысть их имущая во чреве и не лишися.
11 Amatulutsa ana awo ngati gulu la nkhosa; makanda awo amavinavina pabwalo.
Пребывают же яко овцы вечныя, дети же их предиграют,
12 Amayimba nyimbo pogwiritsa ntchito matambolini ndi azeze; amakondwa pakumva kulira kwa chitoliro.
вземше псалтирь и гусли, и веселятся гласом песни.
13 Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero ndipo amatsikira ku manda mwamtendere. (Sheol )
Скончаша во благих житие свое, в покои же адове успоша. (Sheol )
14 Koma anthuwo amawuza Mulungu kuti, ‘Tichokereni!’ Ife tilibe chikhumbokhumbo chofuna kudziwa njira zanu.
Глаголют же Господеви: отступи от нас, путий Твоих ведети не хощем:
15 Kodi Wamphamvuzonseyo ndani kuti timutumikire? Ife tipindula chiyani tikamapemphera kwa Iyeyo?
что достоин, яко да поработаем Ему? И кая польза, яко да взыщем Его?
16 Komatu ulemerero wawo suli mʼmanja mwawo, koma ine ndimakhala patali ndi uphungu wa anthu oyipa.
В руках бо их бяху благая, дел же нечестивых не надзирает.
17 “Koma nʼkangati kamene nyale ya anthu oyipa imazimitsidwa? Nʼkangati kamene tsoka limawagwera? Nʼkangati kamene Mulungu amawakwiyira ndi kuwalanga?
Обаче же и нечестивых светилник угаснет, найдет же им развращение, болезни же их оымут от гнева:
18 Nʼkangati kamene iwo amakhala ngati phesi lowuluka ndi mphepo, ngati mungu wowuluzika ndi kamvuluvulu?
будут же аки плевы пред ветром, или якоже прах, егоже взя вихр.
19 Paja amati, ‘Mulungu amalanga ana chifukwa cha machimo abambo awo.’ Koma Mulungu amabwezera chilango munthuyo, kuti adziwe kuti Mulungu amalangadi.
Да оскудеют сыном имения его: воздаст противу ему, и уразумеет.
20 Mulole kuti adzionere yekha chilango chake, kuti alawe ukali wa Wamphamvuzonse.
Да узрят очи его свое убиение, от Господа же да не спасется.
21 Nanga kodi amalabadira chiyani zabanja lake limene walisiya mʼmbuyo, pamene chiwerengero cha masiku ake chatha?
Яко воля его с ним в дому его, и числа месяцей его разделишася.
22 “Kodi alipo wina amene angaphunzitse Mulungu nzeru, poti Iye amaweruza ngakhale anthu apamwamba?
Не Господь ли есть научаяй разуму и хитрости? Тойже мудрых разсуждает.
23 Munthu wina amamwalira ali ndi mphamvu zonse, ali pa mtendere ndi pa mpumulo,
Той умрет в силе простоты своея, всецел же благодушествуяй и благоуспеваяй,
24 thupi lake lili lonenepa, mafupa ake ali odzaza ndi mafuta.
утроба же его исполнена тука, мозг же его разливается.
25 Munthu wina amamwalira ali wowawidwa mtima, wosalawapo chinthu chabwino chilichonse.
Ов же умирает в горести души, не ядый ничтоже блага.
26 Olemera ndi osauka omwe amamwalira ndi kuyikidwa mʼmanda ndipo onse amatuluka mphutsi.
Вкупе же на земли спят, гнилость же их покры.
27 “Ndikudziwa bwino zimene mukuganiza, ziwembu zanu zomwe mukuti mundichitire.
Темже вем вас, яко дерзостию належите ми,
28 Inu mukuti, ‘Kodi nyumba ya mkulu uja ili kuti, matenti amene munkakhala anthu oyipa aja ali kuti?’
яко речете: где есть дом княжь? И где есть покров селений нечестивых?
29 Kodi munawafunsapo anthu amene ali pa ulendo? Kodi munaganizirapo zimene iwo amanena?
Вопросите мимоходящих путем, и знамения их не чужда сотворите.
30 Zakuti munthu woyipa amasungidwa chifukwa cha tsiku la tsoka, kuti amapulumutsidwa chifukwa cha tsiku la ukali wa Mulungu?
Яко на день пагубы соблюдается нечестивый, и в день гнева Его отведен будет.
31 Kodi ndani amadzudzula munthu wochimwayo? Ndani amamubwezera zoyipa zimene anachita?
Кто возвестит пред лицем его путь его, и еже той сотвори, кто воздаст ему?
32 Iye amanyamulidwa kupita ku manda ndipo anthu amachezera pa manda ake.
И той во гроб отнесен бысть, и на гробищих побде.
33 Dothi la ku chigwa limamukomera; anthu onse amatsatira mtembo wake, ndipo anthu osawerengeka amakhala patsogolo pa chitanda chakecho.
Усладися ему дробное камение потока, и вслед его всяк человек отидет, и пред ним безчисленнии.
34 “Nanga inu mudzanditonthoza bwanji ine ndi mawu anu opandapakewo palibe chimene chatsala kuti muyankhe koma mabodza basi!”
Како же мя утешаете суетными? А еже бы мне почити от вас, ничтоже.