< Yobu 21 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Respondens autem Iob, dixit:
2 “Mvetserani bwino mawu anga; ichi chikhale chitonthozo changa chochokera kwa inu.
Audite quaeso sermones meos, et agite poenitentiam.
3 Ndiloleni ndiyankhule ndipo ndikatha kuyankhula munditonzetonze.
Sustinete me, et ego loquar, et post mea, si videbitur, verba ridete.
4 “Kodi ine ndikudandaulira munthu? Tsono ndilekerenji kupsa mtima?
Numquid contra hominem disputatio mea est, ut merito non debeam contristari?
5 Ndipenyeni ndipo mudabwe; mugwire dzanja pakamwa.
Attendite me, et obstupescite, et superponite digitum ori vestro:
6 Ndikamaganiza zimenezi ndimachita mantha kwambiri; thupi langa limanjenjemera.
Et ego quando recordatus fuero, pertimesco, et concutit carnem meam tremor.
7 Chifukwa chiyani anthu oyipa amakhalabe ndi moyo, amakalamba ndi kusanduka amphamvu?
Quare ergo impii vivunt, sublevati sunt, confortatique divitiis?
8 Amaona ana awo akukhazikika pamodzi nawo, zidzukulu zawo zikukula bwino iwo akuona.
Semen eorum permanet coram eis, propinquorum turba, et nepotum in conspectu eorum.
9 Mabanja awo amakhala pa mtendere ndipo sakhala ndi mantha; mkwapulo wa Mulungu suwakhudza nʼkomwe.
Domus eorum securae sunt et pacatae, et non est virga Dei super illos.
10 Ngʼombe zawo zazimuna sizilephera kubereketsa; ngʼombe zawo zazikazi sizipoloza.
Bos eorum concepit, et non abortivit: vacca peperit, et non est privata foetu suo.
11 Amatulutsa ana awo ngati gulu la nkhosa; makanda awo amavinavina pabwalo.
Egrediuntur quasi greges parvuli eorum, et infantes eorum exultant lusibus.
12 Amayimba nyimbo pogwiritsa ntchito matambolini ndi azeze; amakondwa pakumva kulira kwa chitoliro.
Tenent tympanum, et citharam, et gaudent ad sonitum organi.
13 Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero ndipo amatsikira ku manda mwamtendere. (Sheol h7585)
Ducunt in bonis dies suos, et in puncto ad inferna descendunt. (Sheol h7585)
14 Koma anthuwo amawuza Mulungu kuti, ‘Tichokereni!’ Ife tilibe chikhumbokhumbo chofuna kudziwa njira zanu.
Qui dixerunt Deo: Recede a nobis, et scientiam viarum tuarum nolumus.
15 Kodi Wamphamvuzonseyo ndani kuti timutumikire? Ife tipindula chiyani tikamapemphera kwa Iyeyo?
Quis est Omnipotens, ut serviamus ei? et quid nobis prodest si oraverimus illum?
16 Komatu ulemerero wawo suli mʼmanja mwawo, koma ine ndimakhala patali ndi uphungu wa anthu oyipa.
Verumtamen quia non sunt in manu eorum bona sua, consilium impiorum longe sit a me.
17 “Koma nʼkangati kamene nyale ya anthu oyipa imazimitsidwa? Nʼkangati kamene tsoka limawagwera? Nʼkangati kamene Mulungu amawakwiyira ndi kuwalanga?
Quoties lucerna impiorum extinguetur, et superveniet eis inundatio, et dolores dividet furoris sui?
18 Nʼkangati kamene iwo amakhala ngati phesi lowuluka ndi mphepo, ngati mungu wowuluzika ndi kamvuluvulu?
Erunt sicut paleae ante faciem venti, et sicut favilla quam turbo dispergit.
19 Paja amati, ‘Mulungu amalanga ana chifukwa cha machimo abambo awo.’ Koma Mulungu amabwezera chilango munthuyo, kuti adziwe kuti Mulungu amalangadi.
Deus servabit filiis illius dolorem patris: et cum reddiderit, tunc sciet.
20 Mulole kuti adzionere yekha chilango chake, kuti alawe ukali wa Wamphamvuzonse.
Videbunt oculi eius interfectionem suam, et de furore Omnipotentis bibet.
21 Nanga kodi amalabadira chiyani zabanja lake limene walisiya mʼmbuyo, pamene chiwerengero cha masiku ake chatha?
Quid enim ad eum pertinet de domo sua post se? et si numerus mensium eius dimidietur?
22 “Kodi alipo wina amene angaphunzitse Mulungu nzeru, poti Iye amaweruza ngakhale anthu apamwamba?
Numquid Deus docebit quispiam scientiam, qui excelsos iudicat?
23 Munthu wina amamwalira ali ndi mphamvu zonse, ali pa mtendere ndi pa mpumulo,
Iste moritur robustus et sanus, dives et felix.
24 thupi lake lili lonenepa, mafupa ake ali odzaza ndi mafuta.
Viscera eius plena sunt adipe, et medullis ossa illius irrigantur:
25 Munthu wina amamwalira ali wowawidwa mtima, wosalawapo chinthu chabwino chilichonse.
Alius vero moritur in amaritudine animae absque ullis opibus:
26 Olemera ndi osauka omwe amamwalira ndi kuyikidwa mʼmanda ndipo onse amatuluka mphutsi.
Et tamen simul in pulvere dormient, et vermes operient eos.
27 “Ndikudziwa bwino zimene mukuganiza, ziwembu zanu zomwe mukuti mundichitire.
Certe novi cogitationes vestras, et sententias contra me iniquas.
28 Inu mukuti, ‘Kodi nyumba ya mkulu uja ili kuti, matenti amene munkakhala anthu oyipa aja ali kuti?’
Dicitis enim: Ubi est domus principis? et ubi tabernacula impiorum?
29 Kodi munawafunsapo anthu amene ali pa ulendo? Kodi munaganizirapo zimene iwo amanena?
Interrogate quemlibet de viatoribus, et haec eadem illum intelligere cognoscetis:
30 Zakuti munthu woyipa amasungidwa chifukwa cha tsiku la tsoka, kuti amapulumutsidwa chifukwa cha tsiku la ukali wa Mulungu?
Quia in diem perditionis servatur malus, et ad diem furoris ducetur.
31 Kodi ndani amadzudzula munthu wochimwayo? Ndani amamubwezera zoyipa zimene anachita?
Quis arguet coram eo viam eius? et quae fecit, quis reddet illi?
32 Iye amanyamulidwa kupita ku manda ndipo anthu amachezera pa manda ake.
Ipse ad sepulchra ducetur, et in congerie mortuorum vigilabit.
33 Dothi la ku chigwa limamukomera; anthu onse amatsatira mtembo wake, ndipo anthu osawerengeka amakhala patsogolo pa chitanda chakecho.
Dulcis fuit glareis Cocyti, et post se omnem hominem trahet, et ante se innumerabiles.
34 “Nanga inu mudzanditonthoza bwanji ine ndi mawu anu opandapakewo palibe chimene chatsala kuti muyankhe koma mabodza basi!”
Quomodo igitur consolamini me frustra, cum responsio vestra repugnare ostensa sit veritati?

< Yobu 21 >