< Yobu 21 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
ヨブこたへて曰く
2 “Mvetserani bwino mawu anga; ichi chikhale chitonthozo changa chochokera kwa inu.
請ふ汝等わが言を謹んで聽き 之をもて汝らの慰藉に代よ
3 Ndiloleni ndiyankhule ndipo ndikatha kuyankhula munditonzetonze.
先われに容して言しめよ 我が言る後なんぢ嘲るも可し
4 “Kodi ine ndikudandaulira munthu? Tsono ndilekerenji kupsa mtima?
わが怨言は世の人の上につきて起れる者ならんや 我なんぞ氣をいらだつ可らざらんや
5 Ndipenyeni ndipo mudabwe; mugwire dzanja pakamwa.
なんぢら我を視て驚き手を口にあてよ
6 Ndikamaganiza zimenezi ndimachita mantha kwambiri; thupi langa limanjenjemera.
われ思ひまはせば畏しくなりて身體しきりに戰慄く
7 Chifukwa chiyani anthu oyipa amakhalabe ndi moyo, amakalamba ndi kusanduka amphamvu?
惡き人何とて生ながらへ 老かつ勢力強くなるや
8 Amaona ana awo akukhazikika pamodzi nawo, zidzukulu zawo zikukula bwino iwo akuona.
その子等はその周圍にありてその前に堅く立ち その子孫もその目の前に堅く立べし
9 Mabanja awo amakhala pa mtendere ndipo sakhala ndi mantha; mkwapulo wa Mulungu suwakhudza nʼkomwe.
またその家は平安にして畏懼なく 神の杖その上に臨まじ
10 Ngʼombe zawo zazimuna sizilephera kubereketsa; ngʼombe zawo zazikazi sizipoloza.
その牡牛は種を與へて過らず その牝牛は子を產てそこなふ事なし
11 Amatulutsa ana awo ngati gulu la nkhosa; makanda awo amavinavina pabwalo.
彼等はその少き者等を外に出すこと群のごとし その子等は舞をどる
12 Amayimba nyimbo pogwiritsa ntchito matambolini ndi azeze; amakondwa pakumva kulira kwa chitoliro.
彼等は鼓と琴とをもて歌ひ 笛の音に由て樂み
13 Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero ndipo amatsikira ku manda mwamtendere. (Sheol h7585)
その日を幸福に暮し まばたくまに陰府にくだる (Sheol h7585)
14 Koma anthuwo amawuza Mulungu kuti, ‘Tichokereni!’ Ife tilibe chikhumbokhumbo chofuna kudziwa njira zanu.
然はあれども彼等は神に言らく我らを離れ賜へ 我らは汝の道をしることを好まず
15 Kodi Wamphamvuzonseyo ndani kuti timutumikire? Ife tipindula chiyani tikamapemphera kwa Iyeyo?
全能者は何者なれば我らこれに事ふべき 我儕これに祈るとも何の益を得んやと
16 Komatu ulemerero wawo suli mʼmanja mwawo, koma ine ndimakhala patali ndi uphungu wa anthu oyipa.
視よ彼らの福祿は彼らの力に由にあらざるなり 惡人の希圖は我の與する所にあらず
17 “Koma nʼkangati kamene nyale ya anthu oyipa imazimitsidwa? Nʼkangati kamene tsoka limawagwera? Nʼkangati kamene Mulungu amawakwiyira ndi kuwalanga?
惡人のその燈火を滅るる事幾度ありしか その滅亡のこれに臨む事 神の怒りて之に艱苦を蒙らせたまふ事幾度有しか
18 Nʼkangati kamene iwo amakhala ngati phesi lowuluka ndi mphepo, ngati mungu wowuluzika ndi kamvuluvulu?
かれら風の前の藁の如く 暴風に吹さらるる籾殼の如くなること幾度有しか
19 Paja amati, ‘Mulungu amalanga ana chifukwa cha machimo abambo awo.’ Koma Mulungu amabwezera chilango munthuyo, kuti adziwe kuti Mulungu amalangadi.
神かれの愆を積たくはへてその子孫に報いたまふか 之を彼自己の身に報い知しむるに如ず
20 Mulole kuti adzionere yekha chilango chake, kuti alawe ukali wa Wamphamvuzonse.
かれをして自らその滅亡を目に視させ かつ全能者の震怒を飮しめよ
21 Nanga kodi amalabadira chiyani zabanja lake limene walisiya mʼmbuyo, pamene chiwerengero cha masiku ake chatha?
その月の數すでに盡るに於ては何ぞその後の家に關はる所あらん
22 “Kodi alipo wina amene angaphunzitse Mulungu nzeru, poti Iye amaweruza ngakhale anthu apamwamba?
神は天にある者等をさへ審判たまふなれば誰か能これに知識を敎へんや
23 Munthu wina amamwalira ali ndi mphamvu zonse, ali pa mtendere ndi pa mpumulo,
或人は繁榮を極め全く平穩にかつ安康にして死に
24 thupi lake lili lonenepa, mafupa ake ali odzaza ndi mafuta.
その器に乳充ち その骨の髓は潤ほへり
25 Munthu wina amamwalira ali wowawidwa mtima, wosalawapo chinthu chabwino chilichonse.
また或人は心を苦しめて死し 終に福祉をあぢはふる事なし
26 Olemera ndi osauka omwe amamwalira ndi kuyikidwa mʼmanda ndipo onse amatuluka mphutsi.
是等は倶に齊しく塵に臥して蛆におほはる
27 “Ndikudziwa bwino zimene mukuganiza, ziwembu zanu zomwe mukuti mundichitire.
我まことに汝らの思念を知り 汝らが我を攻撃んとするの計略を知る
28 Inu mukuti, ‘Kodi nyumba ya mkulu uja ili kuti, matenti amene munkakhala anthu oyipa aja ali kuti?’
なんぢらは言ふ王侯の家は何に在る 惡人の住所は何にあると
29 Kodi munawafunsapo anthu amene ali pa ulendo? Kodi munaganizirapo zimene iwo amanena?
汝らは路往く人々に詢ざりしや 彼等の證據を曉らざるや
30 Zakuti munthu woyipa amasungidwa chifukwa cha tsiku la tsoka, kuti amapulumutsidwa chifukwa cha tsiku la ukali wa Mulungu?
すなはち滅亡の日に惡人遺され 烈しき怒の日に惡人たづさへ出さる
31 Kodi ndani amadzudzula munthu wochimwayo? Ndani amamubwezera zoyipa zimene anachita?
誰か能かれに打向ひて彼の行爲を指示さんや 誰か能彼の爲たる所を彼に報ゆることを爲ん
32 Iye amanyamulidwa kupita ku manda ndipo anthu amachezera pa manda ake.
彼は舁れて墓に到り 塚の上にて守護ることを爲す
33 Dothi la ku chigwa limamukomera; anthu onse amatsatira mtembo wake, ndipo anthu osawerengeka amakhala patsogolo pa chitanda chakecho.
谷の土塊も彼には快し 一切の人その後に從ふ 其前に行る者も數へがたし
34 “Nanga inu mudzanditonthoza bwanji ine ndi mawu anu opandapakewo palibe chimene chatsala kuti muyankhe koma mabodza basi!”
旣に是の如くなるに汝等なんぞ徒に我を慰さめんとするや 汝らの答ふる所はただ虚僞のみ

< Yobu 21 >