< Yobu 21 >
1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Giobbe rispose:
2 “Mvetserani bwino mawu anga; ichi chikhale chitonthozo changa chochokera kwa inu.
Ascoltate bene la mia parola e sia questo almeno il conforto che mi date.
3 Ndiloleni ndiyankhule ndipo ndikatha kuyankhula munditonzetonze.
Tollerate che io parli e, dopo il mio parlare, deridetemi pure.
4 “Kodi ine ndikudandaulira munthu? Tsono ndilekerenji kupsa mtima?
Forse io mi lamento di un uomo? E perché non dovrei perder la pazienza?
5 Ndipenyeni ndipo mudabwe; mugwire dzanja pakamwa.
Statemi attenti e resterete stupiti, mettetevi la mano sulla bocca.
6 Ndikamaganiza zimenezi ndimachita mantha kwambiri; thupi langa limanjenjemera.
Se io ci penso, ne sono turbato e la mia carne è presa da un brivido.
7 Chifukwa chiyani anthu oyipa amakhalabe ndi moyo, amakalamba ndi kusanduka amphamvu?
Perché vivono i malvagi, invecchiano, anzi sono potenti e gagliardi?
8 Amaona ana awo akukhazikika pamodzi nawo, zidzukulu zawo zikukula bwino iwo akuona.
La loro prole prospera insieme con essi, i loro rampolli crescono sotto i loro occhi.
9 Mabanja awo amakhala pa mtendere ndipo sakhala ndi mantha; mkwapulo wa Mulungu suwakhudza nʼkomwe.
Le loro case sono tranquille e senza timori; il bastone di Dio non pesa su di loro.
10 Ngʼombe zawo zazimuna sizilephera kubereketsa; ngʼombe zawo zazikazi sizipoloza.
Il loro toro feconda e non falla, la vacca partorisce e non abortisce.
11 Amatulutsa ana awo ngati gulu la nkhosa; makanda awo amavinavina pabwalo.
Mandano fuori, come un gregge, i loro ragazzi e i loro figli saltano in festa.
12 Amayimba nyimbo pogwiritsa ntchito matambolini ndi azeze; amakondwa pakumva kulira kwa chitoliro.
Cantano al suono di timpani e di cetre, si divertono al suono delle zampogne.
13 Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero ndipo amatsikira ku manda mwamtendere. (Sheol )
Finiscono nel benessere i loro giorni e scendono tranquilli negli inferi. (Sheol )
14 Koma anthuwo amawuza Mulungu kuti, ‘Tichokereni!’ Ife tilibe chikhumbokhumbo chofuna kudziwa njira zanu.
Eppure dicevano a Dio: «Allontanati da noi, non vogliamo conoscer le tue vie.
15 Kodi Wamphamvuzonseyo ndani kuti timutumikire? Ife tipindula chiyani tikamapemphera kwa Iyeyo?
Chi è l'Onnipotente, perché dobbiamo servirlo? E che ci giova pregarlo?».
16 Komatu ulemerero wawo suli mʼmanja mwawo, koma ine ndimakhala patali ndi uphungu wa anthu oyipa.
Non hanno forse in mano il loro benessere? Il consiglio degli empi non è lungi da lui?
17 “Koma nʼkangati kamene nyale ya anthu oyipa imazimitsidwa? Nʼkangati kamene tsoka limawagwera? Nʼkangati kamene Mulungu amawakwiyira ndi kuwalanga?
Quante volte si spegne la lucerna degli empi, o la sventura piomba su di loro, e infliggerà loro castighi con ira?
18 Nʼkangati kamene iwo amakhala ngati phesi lowuluka ndi mphepo, ngati mungu wowuluzika ndi kamvuluvulu?
Diventano essi come paglia di fronte al vento o come pula in preda all'uragano?
19 Paja amati, ‘Mulungu amalanga ana chifukwa cha machimo abambo awo.’ Koma Mulungu amabwezera chilango munthuyo, kuti adziwe kuti Mulungu amalangadi.
«Dio serba per i loro figli il suo castigo...». Ma lo faccia pagare piuttosto a lui stesso e lo senta!
20 Mulole kuti adzionere yekha chilango chake, kuti alawe ukali wa Wamphamvuzonse.
Veda con i suoi occhi la sua rovina e beva dell'ira dell'Onnipotente!
21 Nanga kodi amalabadira chiyani zabanja lake limene walisiya mʼmbuyo, pamene chiwerengero cha masiku ake chatha?
Che cosa gli importa infatti della sua casa dopo di sé, quando il numero dei suoi mesi è finito?
22 “Kodi alipo wina amene angaphunzitse Mulungu nzeru, poti Iye amaweruza ngakhale anthu apamwamba?
S'insegna forse la scienza a Dio, a lui che giudica gli esseri di lassù?
23 Munthu wina amamwalira ali ndi mphamvu zonse, ali pa mtendere ndi pa mpumulo,
Uno muore in piena salute, tutto tranquillo e prospero;
24 thupi lake lili lonenepa, mafupa ake ali odzaza ndi mafuta.
i suoi fianchi sono coperti di grasso e il midollo delle sue ossa è ben nutrito.
25 Munthu wina amamwalira ali wowawidwa mtima, wosalawapo chinthu chabwino chilichonse.
Un altro muore con l'amarezza in cuore senza aver mai gustato il bene.
26 Olemera ndi osauka omwe amamwalira ndi kuyikidwa mʼmanda ndipo onse amatuluka mphutsi.
Nella polvere giacciono insieme e i vermi li ricoprono.
27 “Ndikudziwa bwino zimene mukuganiza, ziwembu zanu zomwe mukuti mundichitire.
Ecco, io conosco i vostri pensieri e gli iniqui giudizi che fate contro di me!
28 Inu mukuti, ‘Kodi nyumba ya mkulu uja ili kuti, matenti amene munkakhala anthu oyipa aja ali kuti?’
Infatti, voi dite: «Dov'è la casa del prepotente, dove sono le tende degli empi?».
29 Kodi munawafunsapo anthu amene ali pa ulendo? Kodi munaganizirapo zimene iwo amanena?
Non avete interrogato quelli che viaggiano? Non potete negare le loro prove,
30 Zakuti munthu woyipa amasungidwa chifukwa cha tsiku la tsoka, kuti amapulumutsidwa chifukwa cha tsiku la ukali wa Mulungu?
che nel giorno della sciagura è risparmiato il malvagio e nel giorno dell'ira egli la scampa.
31 Kodi ndani amadzudzula munthu wochimwayo? Ndani amamubwezera zoyipa zimene anachita?
Chi gli rimprovera in faccia la sua condotta e di quel che ha fatto chi lo ripaga?
32 Iye amanyamulidwa kupita ku manda ndipo anthu amachezera pa manda ake.
Egli sarà portato al sepolcro, sul suo tumulo si veglia
33 Dothi la ku chigwa limamukomera; anthu onse amatsatira mtembo wake, ndipo anthu osawerengeka amakhala patsogolo pa chitanda chakecho.
e gli sono lievi le zolle della tomba. Trae dietro di sé tutti gli uomini e innanzi a sé una folla senza numero.
34 “Nanga inu mudzanditonthoza bwanji ine ndi mawu anu opandapakewo palibe chimene chatsala kuti muyankhe koma mabodza basi!”
Perché dunque mi consolate invano, mentre delle vostre risposte non resta che inganno?