< Yobu 21 >
1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Then Job replied,
2 “Mvetserani bwino mawu anga; ichi chikhale chitonthozo changa chochokera kwa inu.
“Listen to what I say, all [three] of you; that is the only thing that you can do that will comfort me.
3 Ndiloleni ndiyankhule ndipo ndikatha kuyankhula munditonzetonze.
Be patient with me, and allow me to speak. Then, after I am finished speaking, you can continue to make fun of me.
4 “Kodi ine ndikudandaulira munthu? Tsono ndilekerenji kupsa mtima?
“It is certainly not [RHQ] people against whom I am complaining, [but God] And it is certainly [RHQ] right for me to be impatient!
5 Ndipenyeni ndipo mudabwe; mugwire dzanja pakamwa.
Look at me! Does what you see not cause you to be appalled and to put your hands over your mouths [and say no more]?
6 Ndikamaganiza zimenezi ndimachita mantha kwambiri; thupi langa limanjenjemera.
When I think about [what has happened to me], I am frightened and my entire body shakes.
7 Chifukwa chiyani anthu oyipa amakhalabe ndi moyo, amakalamba ndi kusanduka amphamvu?
“[But let me ask this: ] ‘Why do wicked people continue to live, and become prosperous, and not die until they are very old?’
8 Amaona ana awo akukhazikika pamodzi nawo, zidzukulu zawo zikukula bwino iwo akuona.
They have their children around them, and they watch them while they [grow up and] start to live in their own houses, and they enjoy their grandchildren.
9 Mabanja awo amakhala pa mtendere ndipo sakhala ndi mantha; mkwapulo wa Mulungu suwakhudza nʼkomwe.
Wicked people live in their own houses without being afraid, and God does not punish [MTY] them.
10 Ngʼombe zawo zazimuna sizilephera kubereketsa; ngʼombe zawo zazikazi sizipoloza.
Their bulls always mate with the cows successfully, and the cows give birth to calves and never miscarry.
11 Amatulutsa ana awo ngati gulu la nkhosa; makanda awo amavinavina pabwalo.
Wicked people send their young children outside [to play], and the children play [happily] like [SIM] lambs [in a pasture].
12 Amayimba nyimbo pogwiritsa ntchito matambolini ndi azeze; amakondwa pakumva kulira kwa chitoliro.
Some children dance and sing, while others shake tambourines and play lyres, and they are happy when they hear people playing flutes.
13 Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero ndipo amatsikira ku manda mwamtendere. (Sheol )
Wicked people enjoy having good things all the time that they are alive, and they die quietly/peacefully and go down to the place of the dead. (Sheol )
14 Koma anthuwo amawuza Mulungu kuti, ‘Tichokereni!’ Ife tilibe chikhumbokhumbo chofuna kudziwa njira zanu.
While they are alive, they say to God, ‘Do not bother us; we do not want to know how you want us to conduct our lives!
15 Kodi Wamphamvuzonseyo ndani kuti timutumikire? Ife tipindula chiyani tikamapemphera kwa Iyeyo?
Why do you, Almighty God, think that we should serve you? (What advantage do we get if we pray to you?/It is useless for us to pray to you.) [RHQ]’
16 Komatu ulemerero wawo suli mʼmanja mwawo, koma ine ndimakhala patali ndi uphungu wa anthu oyipa.
Think about it: Wicked people think that it is because of what they have done that they have become prosperous, but I do not understand why they think like that.
17 “Koma nʼkangati kamene nyale ya anthu oyipa imazimitsidwa? Nʼkangati kamene tsoka limawagwera? Nʼkangati kamene Mulungu amawakwiyira ndi kuwalanga?
(“How often does it happen that wicked people die [MET] before they are old?/Very seldom do wicked people die [MET] before they are old.) [RHQ] (Do they ever experience disasters?/They seldom experience disasters.) [RHQ] (Does God ever punish them because of being very angry with them?/God never punishes them because of being very angry with them.) [RHQ]
18 Nʼkangati kamene iwo amakhala ngati phesi lowuluka ndi mphepo, ngati mungu wowuluzika ndi kamvuluvulu?
[He does not blow] them away like wind blows away straw; they are never carried off by a whirlwind.
19 Paja amati, ‘Mulungu amalanga ana chifukwa cha machimo abambo awo.’ Koma Mulungu amabwezera chilango munthuyo, kuti adziwe kuti Mulungu amalangadi.
You say, ‘When people have committed sins, God waits and punishes their children because of those sins;’ but [I say that] God should punish those who sin, [not their children, ] in order that the sinners will know [that it is because of their own sins that they are being punished].
20 Mulole kuti adzionere yekha chilango chake, kuti alawe ukali wa Wamphamvuzonse.
I hope/wish that wicked people will experience themselves being destroyed, that they will experience being punished by an angry Almighty God.
21 Nanga kodi amalabadira chiyani zabanja lake limene walisiya mʼmbuyo, pamene chiwerengero cha masiku ake chatha?
After wicked people are dead, they are not at all concerned [RHQ] about what happens to their families [MTY].
22 “Kodi alipo wina amene angaphunzitse Mulungu nzeru, poti Iye amaweruza ngakhale anthu apamwamba?
“Since God judges [everyone, ] even those that are in heaven, (who can teach God anything?/certainly no one can teach God anything.) [RHQ]
23 Munthu wina amamwalira ali ndi mphamvu zonse, ali pa mtendere ndi pa mpumulo,
Some people die while they are very healthy, while they are peaceful, when they are not afraid of anything.
24 thupi lake lili lonenepa, mafupa ake ali odzaza ndi mafuta.
Their bodies are fat; their bones are strong.
25 Munthu wina amamwalira ali wowawidwa mtima, wosalawapo chinthu chabwino chilichonse.
Other people die being very miserable; they have never experienced good things happening to them.
26 Olemera ndi osauka omwe amamwalira ndi kuyikidwa mʼmanda ndipo onse amatuluka mphutsi.
But both rich and poor people die and are buried, and maggots eat their bodies. [Everyone dies, so it is clear that dying is not always the punishment for being wicked].
27 “Ndikudziwa bwino zimene mukuganiza, ziwembu zanu zomwe mukuti mundichitire.
“Listen, I know what you [three] are thinking. I know the evil things that you plan to do to me.
28 Inu mukuti, ‘Kodi nyumba ya mkulu uja ili kuti, matenti amene munkakhala anthu oyipa aja ali kuti?’
You say, ‘What happened to the tents in which wicked people were living? The houses of evil rulers have been destroyed!’
29 Kodi munawafunsapo anthu amene ali pa ulendo? Kodi munaganizirapo zimene iwo amanena?
But have you never inquired of people who travel much? Do you not believe their reports about what they have seen,
30 Zakuti munthu woyipa amasungidwa chifukwa cha tsiku la tsoka, kuti amapulumutsidwa chifukwa cha tsiku la ukali wa Mulungu?
that wicked people usually do not suffer at the time when there are great disasters; that wicked people are the ones who are rescued when God is angry [and punishes people] [MTY]?
31 Kodi ndani amadzudzula munthu wochimwayo? Ndani amamubwezera zoyipa zimene anachita?
There is no one [RHQ] who accuses wicked people, and there is no one who (pays them back/gives them the punishment that they deserve) for all the evil things that they have done.
32 Iye amanyamulidwa kupita ku manda ndipo anthu amachezera pa manda ake.
The corpses of wicked people are carried to their graves, and people are put there to guard those graves.
33 Dothi la ku chigwa limamukomera; anthu onse amatsatira mtembo wake, ndipo anthu osawerengeka amakhala patsogolo pa chitanda chakecho.
A huge number [HYP] of people go to the grave site. Some go in front of the procession and some come behind. And the clods of dirt thrown on the graves of those wicked people who have died are like a nice blanket.
34 “Nanga inu mudzanditonthoza bwanji ine ndi mawu anu opandapakewo palibe chimene chatsala kuti muyankhe koma mabodza basi!”
“So how can you console me by talking nonsense? Every reply that you make is full of lies!”