< Yobu 21 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
But Job answered and said:
2 “Mvetserani bwino mawu anga; ichi chikhale chitonthozo changa chochokera kwa inu.
Hear attentively my words, And let this be your consolation.
3 Ndiloleni ndiyankhule ndipo ndikatha kuyankhula munditonzetonze.
Bear with me, that I may speak; And after I have spoken, mock on!
4 “Kodi ine ndikudandaulira munthu? Tsono ndilekerenji kupsa mtima?
Is my complaint concerning man? Why then should I not be angry?
5 Ndipenyeni ndipo mudabwe; mugwire dzanja pakamwa.
Look upon me, and be astonished, And lay your hand upon your mouth!
6 Ndikamaganiza zimenezi ndimachita mantha kwambiri; thupi langa limanjenjemera.
When I think of it, I am confounded; Trembling taketh hold of my flesh.
7 Chifukwa chiyani anthu oyipa amakhalabe ndi moyo, amakalamba ndi kusanduka amphamvu?
Why is it that the wicked live, Grow old, yea, become mighty in substance?
8 Amaona ana awo akukhazikika pamodzi nawo, zidzukulu zawo zikukula bwino iwo akuona.
Their children are established in their sight with them, And their offspring before their eyes.
9 Mabanja awo amakhala pa mtendere ndipo sakhala ndi mantha; mkwapulo wa Mulungu suwakhudza nʼkomwe.
Their houses are in peace, without fear, And the rod of God cometh not upon them.
10 Ngʼombe zawo zazimuna sizilephera kubereketsa; ngʼombe zawo zazikazi sizipoloza.
Their bull gendereth, and faileth not; Their cow calveth, and casteth not her calf.
11 Amatulutsa ana awo ngati gulu la nkhosa; makanda awo amavinavina pabwalo.
They send forth their little ones like a flock, And their children dance.
12 Amayimba nyimbo pogwiritsa ntchito matambolini ndi azeze; amakondwa pakumva kulira kwa chitoliro.
They sing to the timbrel and harp, And rejoice at the sound of the pipe.
13 Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero ndipo amatsikira ku manda mwamtendere. (Sheol h7585)
They spend their days in prosperity, And in a moment go down to the under-world. (Sheol h7585)
14 Koma anthuwo amawuza Mulungu kuti, ‘Tichokereni!’ Ife tilibe chikhumbokhumbo chofuna kudziwa njira zanu.
And yet they say unto God, “Depart from us! We desire not the knowledge of thy ways!
15 Kodi Wamphamvuzonseyo ndani kuti timutumikire? Ife tipindula chiyani tikamapemphera kwa Iyeyo?
Who is the Almighty, that we should serve him? And what will it profit us, if we pray to him?”
16 Komatu ulemerero wawo suli mʼmanja mwawo, koma ine ndimakhala patali ndi uphungu wa anthu oyipa.
[[Ye say, ]] “Lo! their prosperity is not secure in their hands! Far from me be the conduct of the wicked!”
17 “Koma nʼkangati kamene nyale ya anthu oyipa imazimitsidwa? Nʼkangati kamene tsoka limawagwera? Nʼkangati kamene Mulungu amawakwiyira ndi kuwalanga?
How often is it, that the lamp of the wicked is put out? And that destruction cometh upon them, And that He dispenseth to them tribulations in his anger?
18 Nʼkangati kamene iwo amakhala ngati phesi lowuluka ndi mphepo, ngati mungu wowuluzika ndi kamvuluvulu?
How often are they as stubble before the wind, Or as chaff, which the whirlwind carrieth away?
19 Paja amati, ‘Mulungu amalanga ana chifukwa cha machimo abambo awo.’ Koma Mulungu amabwezera chilango munthuyo, kuti adziwe kuti Mulungu amalangadi.
“But” [[say ye]] “God layeth up his iniquity for his children.” Let him requite the offender, and let him feel it!
20 Mulole kuti adzionere yekha chilango chake, kuti alawe ukali wa Wamphamvuzonse.
Let his own eyes see his destruction, And let him drink of the wrath of the Almighty!
21 Nanga kodi amalabadira chiyani zabanja lake limene walisiya mʼmbuyo, pamene chiwerengero cha masiku ake chatha?
For what concern hath he for his household after him, When the number of his own months is completed?
22 “Kodi alipo wina amene angaphunzitse Mulungu nzeru, poti Iye amaweruza ngakhale anthu apamwamba?
Who then shall impart knowledge to God, —To him that judgeth the highest?
23 Munthu wina amamwalira ali ndi mphamvu zonse, ali pa mtendere ndi pa mpumulo,
One dieth in the fulness of his prosperity, Being wholly at ease and quiet;
24 thupi lake lili lonenepa, mafupa ake ali odzaza ndi mafuta.
His sides are full of fat, And his bones moist with marrow.
25 Munthu wina amamwalira ali wowawidwa mtima, wosalawapo chinthu chabwino chilichonse.
Another dieth in bitterness of soul, And hath not tasted pleasure.
26 Olemera ndi osauka omwe amamwalira ndi kuyikidwa mʼmanda ndipo onse amatuluka mphutsi.
Alike they lie down in the dust, And the worms cover them.
27 “Ndikudziwa bwino zimene mukuganiza, ziwembu zanu zomwe mukuti mundichitire.
Behold, I know your thoughts, And the devices by which ye wrong me.
28 Inu mukuti, ‘Kodi nyumba ya mkulu uja ili kuti, matenti amene munkakhala anthu oyipa aja ali kuti?’
For ye say, “Where is the house of the oppressor, And where the dwelling-places of the wicked?”
29 Kodi munawafunsapo anthu amene ali pa ulendo? Kodi munaganizirapo zimene iwo amanena?
Have ye never inquired of travellers, And do ye not know their tokens,
30 Zakuti munthu woyipa amasungidwa chifukwa cha tsiku la tsoka, kuti amapulumutsidwa chifukwa cha tsiku la ukali wa Mulungu?
That the wicked is spared in the day of destruction, And that he is borne to his grave in the day of wrath?
31 Kodi ndani amadzudzula munthu wochimwayo? Ndani amamubwezera zoyipa zimene anachita?
Who will charge him with his conduct to his face, And who will requite him for the evil he hath done?
32 Iye amanyamulidwa kupita ku manda ndipo anthu amachezera pa manda ake.
Even this man is borne with honor to the grave; Yea, he watcheth over his tomb.
33 Dothi la ku chigwa limamukomera; anthu onse amatsatira mtembo wake, ndipo anthu osawerengeka amakhala patsogolo pa chitanda chakecho.
Sweet to him are the sods of the valley: And all men move after him, As multitudes without number before him.
34 “Nanga inu mudzanditonthoza bwanji ine ndi mawu anu opandapakewo palibe chimene chatsala kuti muyankhe koma mabodza basi!”
Why then do ye offer your vain consolations? Your answers continue false.

< Yobu 21 >