< Yobu 21 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Then Job answered,
2 “Mvetserani bwino mawu anga; ichi chikhale chitonthozo changa chochokera kwa inu.
"Listen diligently to my speech. Let this be your consolation.
3 Ndiloleni ndiyankhule ndipo ndikatha kuyankhula munditonzetonze.
Allow me, and I also will speak; After I have spoken, mock on.
4 “Kodi ine ndikudandaulira munthu? Tsono ndilekerenji kupsa mtima?
As for me, is my complaint to man? Why shouldn't I be impatient?
5 Ndipenyeni ndipo mudabwe; mugwire dzanja pakamwa.
Look at me, and be astonished. Lay your hand on your mouth.
6 Ndikamaganiza zimenezi ndimachita mantha kwambiri; thupi langa limanjenjemera.
When I remember, I am troubled. Horror takes hold of my flesh.
7 Chifukwa chiyani anthu oyipa amakhalabe ndi moyo, amakalamba ndi kusanduka amphamvu?
"Why do the wicked live, become old, yes, and grow mighty in power?
8 Amaona ana awo akukhazikika pamodzi nawo, zidzukulu zawo zikukula bwino iwo akuona.
Their child is established with them in their sight, their offspring before their eyes.
9 Mabanja awo amakhala pa mtendere ndipo sakhala ndi mantha; mkwapulo wa Mulungu suwakhudza nʼkomwe.
Their houses are safe from fear, neither is the rod of God upon them.
10 Ngʼombe zawo zazimuna sizilephera kubereketsa; ngʼombe zawo zazikazi sizipoloza.
Their bulls breed without fail. Their cows calve, and do not miscarry.
11 Amatulutsa ana awo ngati gulu la nkhosa; makanda awo amavinavina pabwalo.
They send forth their little ones like a flock. Their children dance.
12 Amayimba nyimbo pogwiritsa ntchito matambolini ndi azeze; amakondwa pakumva kulira kwa chitoliro.
They sing to the tambourine and harp, and rejoice at the sound of the pipe.
13 Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero ndipo amatsikira ku manda mwamtendere. (Sheol h7585)
They spend their days in prosperity. In an instant they go down to Sheol. (Sheol h7585)
14 Koma anthuwo amawuza Mulungu kuti, ‘Tichokereni!’ Ife tilibe chikhumbokhumbo chofuna kudziwa njira zanu.
They tell God, 'Depart from us, for we do not want to know about your ways.
15 Kodi Wamphamvuzonseyo ndani kuti timutumikire? Ife tipindula chiyani tikamapemphera kwa Iyeyo?
What is Shaddai, that we should serve him? What profit should we have, if we pray to him?'
16 Komatu ulemerero wawo suli mʼmanja mwawo, koma ine ndimakhala patali ndi uphungu wa anthu oyipa.
Look, their prosperity is not in their hand. The counsel of the wicked is far from me.
17 “Koma nʼkangati kamene nyale ya anthu oyipa imazimitsidwa? Nʼkangati kamene tsoka limawagwera? Nʼkangati kamene Mulungu amawakwiyira ndi kuwalanga?
"How often is it that the lamp of the wicked is put out, that their calamity comes on them, that he distributes sorrows in his anger?
18 Nʼkangati kamene iwo amakhala ngati phesi lowuluka ndi mphepo, ngati mungu wowuluzika ndi kamvuluvulu?
How often is it that they are as stubble before the wind, as chaff that the storm carries away?
19 Paja amati, ‘Mulungu amalanga ana chifukwa cha machimo abambo awo.’ Koma Mulungu amabwezera chilango munthuyo, kuti adziwe kuti Mulungu amalangadi.
You say, 'God lays up his iniquity for his children.' Let him recompense it to himself, that he may know it.
20 Mulole kuti adzionere yekha chilango chake, kuti alawe ukali wa Wamphamvuzonse.
Let his own eyes see his destruction. Let him drink of the wrath of Shaddai.
21 Nanga kodi amalabadira chiyani zabanja lake limene walisiya mʼmbuyo, pamene chiwerengero cha masiku ake chatha?
For what does he care for his house after him, when the number of his months is cut off?
22 “Kodi alipo wina amene angaphunzitse Mulungu nzeru, poti Iye amaweruza ngakhale anthu apamwamba?
"Shall any teach God knowledge, seeing he judges those who are high?
23 Munthu wina amamwalira ali ndi mphamvu zonse, ali pa mtendere ndi pa mpumulo,
One dies in his full strength, being wholly at ease and quiet.
24 thupi lake lili lonenepa, mafupa ake ali odzaza ndi mafuta.
His pails are full of milk. The marrow of his bones is moistened.
25 Munthu wina amamwalira ali wowawidwa mtima, wosalawapo chinthu chabwino chilichonse.
Another dies in bitterness of soul, and never tastes of good.
26 Olemera ndi osauka omwe amamwalira ndi kuyikidwa mʼmanda ndipo onse amatuluka mphutsi.
They lie down alike in the dust. The worm covers them.
27 “Ndikudziwa bwino zimene mukuganiza, ziwembu zanu zomwe mukuti mundichitire.
"Look, I know your thoughts, the devices with which you would wrong me.
28 Inu mukuti, ‘Kodi nyumba ya mkulu uja ili kuti, matenti amene munkakhala anthu oyipa aja ali kuti?’
For you say, 'Where is the house of the prince? Where is the tent in which the wicked lived?'
29 Kodi munawafunsapo anthu amene ali pa ulendo? Kodi munaganizirapo zimene iwo amanena?
Haven't you asked wayfaring men? Do you not know their evidences,
30 Zakuti munthu woyipa amasungidwa chifukwa cha tsiku la tsoka, kuti amapulumutsidwa chifukwa cha tsiku la ukali wa Mulungu?
that the evil man is reserved to the day of calamity, That they are led forth to the day of wrath?
31 Kodi ndani amadzudzula munthu wochimwayo? Ndani amamubwezera zoyipa zimene anachita?
Who shall declare his way to his face? Who shall repay him what he has done?
32 Iye amanyamulidwa kupita ku manda ndipo anthu amachezera pa manda ake.
Yet he will be borne to the grave. Men shall keep watch over the tomb.
33 Dothi la ku chigwa limamukomera; anthu onse amatsatira mtembo wake, ndipo anthu osawerengeka amakhala patsogolo pa chitanda chakecho.
The clods of the valley shall be sweet to him. All men shall draw after him, as there were innumerable before him.
34 “Nanga inu mudzanditonthoza bwanji ine ndi mawu anu opandapakewo palibe chimene chatsala kuti muyankhe koma mabodza basi!”
So how can you comfort me with nonsense, seeing that in your answers there remains only falsehood?"

< Yobu 21 >