< Yobu 21 >
1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Then answered Job, and said,
2 “Mvetserani bwino mawu anga; ichi chikhale chitonthozo changa chochokera kwa inu.
Hear, O hear my speech, and let this be wherewith you give consolations.
3 Ndiloleni ndiyankhule ndipo ndikatha kuyankhula munditonzetonze.
Bear with me that I may indeed speak: and after my speaking, then canst thou mock.
4 “Kodi ine ndikudandaulira munthu? Tsono ndilekerenji kupsa mtima?
As for me, —is against man my complaint? and if this be so, why should my spirit not be impatient?
5 Ndipenyeni ndipo mudabwe; mugwire dzanja pakamwa.
Turn yourselves unto me, and be astounded, and lay your hand upon your mouth.
6 Ndikamaganiza zimenezi ndimachita mantha kwambiri; thupi langa limanjenjemera.
Yea, when I think of it, I am terrified, and shuddering seizeth hold of my flesh.
7 Chifukwa chiyani anthu oyipa amakhalabe ndi moyo, amakalamba ndi kusanduka amphamvu?
Wherefore do the wicked live, become old, yea, grow strong in power?
8 Amaona ana awo akukhazikika pamodzi nawo, zidzukulu zawo zikukula bwino iwo akuona.
Their seed is firmly established in their presence with them. their offspring are before their eyes.
9 Mabanja awo amakhala pa mtendere ndipo sakhala ndi mantha; mkwapulo wa Mulungu suwakhudza nʼkomwe.
Their houses are at peace without any dread, and no rod of God [cometh] over them.
10 Ngʼombe zawo zazimuna sizilephera kubereketsa; ngʼombe zawo zazikazi sizipoloza.
The bull of each one gendereth, and disappointeth not: the cow of each one calveth, and casteth not her young.
11 Amatulutsa ana awo ngati gulu la nkhosa; makanda awo amavinavina pabwalo.
They send forth their little ones like a flock, and their children skip about [with joy].
12 Amayimba nyimbo pogwiritsa ntchito matambolini ndi azeze; amakondwa pakumva kulira kwa chitoliro.
They sing to the timbrel and harp, and rejoice at the sound of the pipe.
13 Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero ndipo amatsikira ku manda mwamtendere. (Sheol )
They wear out their days in happiness, and in a moment they go down to the nether world. (Sheol )
14 Koma anthuwo amawuza Mulungu kuti, ‘Tichokereni!’ Ife tilibe chikhumbokhumbo chofuna kudziwa njira zanu.
And yet they say unto God, “Depart from us; and the knowledge of thy ways we desire not.
15 Kodi Wamphamvuzonseyo ndani kuti timutumikire? Ife tipindula chiyani tikamapemphera kwa Iyeyo?
What is the Almighty, that we should serve him? and what profit shall we have, if we entreat him urgently?”
16 Komatu ulemerero wawo suli mʼmanja mwawo, koma ine ndimakhala patali ndi uphungu wa anthu oyipa.
Lo, not in their hand doth their happiness rest! The counsel of the wicked be [still] far from me.
17 “Koma nʼkangati kamene nyale ya anthu oyipa imazimitsidwa? Nʼkangati kamene tsoka limawagwera? Nʼkangati kamene Mulungu amawakwiyira ndi kuwalanga?
How often is the lamp of the wicked quenched? and how often cometh over them their calamity? and doth [God] distribute their lot in his anger?
18 Nʼkangati kamene iwo amakhala ngati phesi lowuluka ndi mphepo, ngati mungu wowuluzika ndi kamvuluvulu?
Are they as straw before the wind, and as chaff which the stealeth away?
19 Paja amati, ‘Mulungu amalanga ana chifukwa cha machimo abambo awo.’ Koma Mulungu amabwezera chilango munthuyo, kuti adziwe kuti Mulungu amalangadi.
Should God lay up for his children his wrong-doing? it were better that he reward him, that he might know it himself.
20 Mulole kuti adzionere yekha chilango chake, kuti alawe ukali wa Wamphamvuzonse.
His own eyes ought to see his downfall, and from the wrath of the Almighty ought he to drink.
21 Nanga kodi amalabadira chiyani zabanja lake limene walisiya mʼmbuyo, pamene chiwerengero cha masiku ake chatha?
For what care hath he for his household after him, when the number of his months is all apportioned to him?
22 “Kodi alipo wina amene angaphunzitse Mulungu nzeru, poti Iye amaweruza ngakhale anthu apamwamba?
Is this fitting God, who teacheth knowledge? him who judgeth those that are highest?
23 Munthu wina amamwalira ali ndi mphamvu zonse, ali pa mtendere ndi pa mpumulo,
That this one dieth in his full strength, being wholly at ease and quiet;
24 thupi lake lili lonenepa, mafupa ake ali odzaza ndi mafuta.
His vessels being full of healthy fluid, and the marrow of his bones being well moistened:
25 Munthu wina amamwalira ali wowawidwa mtima, wosalawapo chinthu chabwino chilichonse.
While this other dieth with an embittered soul, and hath never partaken of any happiness;
26 Olemera ndi osauka omwe amamwalira ndi kuyikidwa mʼmanda ndipo onse amatuluka mphutsi.
[And yet] together they must lie down in the dust, and the worms will cover them?
27 “Ndikudziwa bwino zimene mukuganiza, ziwembu zanu zomwe mukuti mundichitire.
Behold, I know your thoughts, and the opinions which ye wrongfully devise against me.
28 Inu mukuti, ‘Kodi nyumba ya mkulu uja ili kuti, matenti amene munkakhala anthu oyipa aja ali kuti?’
For ye say, Where is the house of the noble-minded? and where is the tent of the dwelling-places of the wicked?
29 Kodi munawafunsapo anthu amene ali pa ulendo? Kodi munaganizirapo zimene iwo amanena?
Have ye not asked the wayfarers? surely their token ye cannot disregard,
30 Zakuti munthu woyipa amasungidwa chifukwa cha tsiku la tsoka, kuti amapulumutsidwa chifukwa cha tsiku la ukali wa Mulungu?
That the bad man is reserved for the day of calamity, [that the wicked] are carried forward to the day of wrath.
31 Kodi ndani amadzudzula munthu wochimwayo? Ndani amamubwezera zoyipa zimene anachita?
[But] who will tell him to his face of his way? and who will repay him what he hath done?
32 Iye amanyamulidwa kupita ku manda ndipo anthu amachezera pa manda ake.
Yea he will indeed be carried to the grave, and men will quickly think of his monument:
33 Dothi la ku chigwa limamukomera; anthu onse amatsatira mtembo wake, ndipo anthu osawerengeka amakhala patsogolo pa chitanda chakecho.
Sweet are to him the clods of the valley; and after him succeedeth every man, as those that were before him are without number.
34 “Nanga inu mudzanditonthoza bwanji ine ndi mawu anu opandapakewo palibe chimene chatsala kuti muyankhe koma mabodza basi!”
How then will ye comfort me with vanity? and of your answers there remaineth only deception.