< Yobu 21 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
And Job answered and said,
2 “Mvetserani bwino mawu anga; ichi chikhale chitonthozo changa chochokera kwa inu.
Hear attentively my speech, and let this replace your consolations.
3 Ndiloleni ndiyankhule ndipo ndikatha kuyankhula munditonzetonze.
Suffer me and I will speak; and after I have spoken, mock on!
4 “Kodi ine ndikudandaulira munthu? Tsono ndilekerenji kupsa mtima?
As for me, is my complaint to a man? or wherefore should not my spirit be impatient?
5 Ndipenyeni ndipo mudabwe; mugwire dzanja pakamwa.
Mark me, and be astonished, and lay the hand upon the mouth.
6 Ndikamaganiza zimenezi ndimachita mantha kwambiri; thupi langa limanjenjemera.
Even when I think [thereon], I am affrighted, and trembling taketh hold of my flesh.
7 Chifukwa chiyani anthu oyipa amakhalabe ndi moyo, amakalamba ndi kusanduka amphamvu?
Wherefore do the wicked live, grow old, yea, become mighty in power?
8 Amaona ana awo akukhazikika pamodzi nawo, zidzukulu zawo zikukula bwino iwo akuona.
Their seed is established with them in their sight, and their offspring before their eyes.
9 Mabanja awo amakhala pa mtendere ndipo sakhala ndi mantha; mkwapulo wa Mulungu suwakhudza nʼkomwe.
Their houses are safe from fear, neither is the rod of God upon them.
10 Ngʼombe zawo zazimuna sizilephera kubereketsa; ngʼombe zawo zazikazi sizipoloza.
Their bull gendereth, and faileth not; their cow calveth, and casteth not her calf.
11 Amatulutsa ana awo ngati gulu la nkhosa; makanda awo amavinavina pabwalo.
They send forth their little ones like a flock, and their children dance.
12 Amayimba nyimbo pogwiritsa ntchito matambolini ndi azeze; amakondwa pakumva kulira kwa chitoliro.
They shout to the tambour and harp, and rejoice at the sound of the pipe.
13 Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero ndipo amatsikira ku manda mwamtendere. (Sheol h7585)
They spend their days in prosperity, and in a moment go down to Sheol. (Sheol h7585)
14 Koma anthuwo amawuza Mulungu kuti, ‘Tichokereni!’ Ife tilibe chikhumbokhumbo chofuna kudziwa njira zanu.
And they say unto God, Depart from us, for we desire not the knowledge of thy ways!
15 Kodi Wamphamvuzonseyo ndani kuti timutumikire? Ife tipindula chiyani tikamapemphera kwa Iyeyo?
What is the Almighty that we should serve him? and what are we profited if we pray unto him?
16 Komatu ulemerero wawo suli mʼmanja mwawo, koma ine ndimakhala patali ndi uphungu wa anthu oyipa.
Behold, their prosperity is not in their hand. The counsel of the wicked be far from me!
17 “Koma nʼkangati kamene nyale ya anthu oyipa imazimitsidwa? Nʼkangati kamene tsoka limawagwera? Nʼkangati kamene Mulungu amawakwiyira ndi kuwalanga?
How often is the lamp of the wicked put out, and cometh their calamity upon them? Doth he distribute sorrows [to them] in his anger?
18 Nʼkangati kamene iwo amakhala ngati phesi lowuluka ndi mphepo, ngati mungu wowuluzika ndi kamvuluvulu?
Do they become as stubble before the wind, and as chaff that the storm carrieth away?
19 Paja amati, ‘Mulungu amalanga ana chifukwa cha machimo abambo awo.’ Koma Mulungu amabwezera chilango munthuyo, kuti adziwe kuti Mulungu amalangadi.
God layeth up [the punishment of] his iniquity for his children; he rewardeth him, and he shall know [it]:
20 Mulole kuti adzionere yekha chilango chake, kuti alawe ukali wa Wamphamvuzonse.
His eyes shall see his destruction, and he shall drink of the fury of the Almighty.
21 Nanga kodi amalabadira chiyani zabanja lake limene walisiya mʼmbuyo, pamene chiwerengero cha masiku ake chatha?
For what pleasure should he have in his house after him, when the number of his months is cut off?
22 “Kodi alipo wina amene angaphunzitse Mulungu nzeru, poti Iye amaweruza ngakhale anthu apamwamba?
Can any teach God knowledge? And he it is that judgeth those that are high.
23 Munthu wina amamwalira ali ndi mphamvu zonse, ali pa mtendere ndi pa mpumulo,
One dieth in his full strength, being wholly at ease and quiet;
24 thupi lake lili lonenepa, mafupa ake ali odzaza ndi mafuta.
His sides are full of fat, and the marrow of his bones is moistened;
25 Munthu wina amamwalira ali wowawidwa mtima, wosalawapo chinthu chabwino chilichonse.
And another dieth in bitterness of soul, and hath not tasted good:
26 Olemera ndi osauka omwe amamwalira ndi kuyikidwa mʼmanda ndipo onse amatuluka mphutsi.
Together they lie down in the dust, and the worms cover them.
27 “Ndikudziwa bwino zimene mukuganiza, ziwembu zanu zomwe mukuti mundichitire.
Lo, I know your thoughts, and the devices ye wrongfully imagine against me.
28 Inu mukuti, ‘Kodi nyumba ya mkulu uja ili kuti, matenti amene munkakhala anthu oyipa aja ali kuti?’
For ye say, Where is the house of the noble? and where the tent of the dwellings of the wicked?
29 Kodi munawafunsapo anthu amene ali pa ulendo? Kodi munaganizirapo zimene iwo amanena?
Have ye not asked the wayfarers? and do ye not regard their tokens:
30 Zakuti munthu woyipa amasungidwa chifukwa cha tsiku la tsoka, kuti amapulumutsidwa chifukwa cha tsiku la ukali wa Mulungu?
That the wicked is reserved for the day of calamity? They are led forth to the day of wrath.
31 Kodi ndani amadzudzula munthu wochimwayo? Ndani amamubwezera zoyipa zimene anachita?
Who shall declare his way to his face? and who shall repay him what he hath done?
32 Iye amanyamulidwa kupita ku manda ndipo anthu amachezera pa manda ake.
Yet is he carried to the graves, and watch is kept over the tomb.
33 Dothi la ku chigwa limamukomera; anthu onse amatsatira mtembo wake, ndipo anthu osawerengeka amakhala patsogolo pa chitanda chakecho.
The clods of the valley are sweet unto him; and every man followeth suit after him, as there were innumerable before him.
34 “Nanga inu mudzanditonthoza bwanji ine ndi mawu anu opandapakewo palibe chimene chatsala kuti muyankhe koma mabodza basi!”
How then comfort ye me in vain? Your answers remain perfidious.

< Yobu 21 >