< Yobu 21 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Maar Job antwoordde en zeide:
2 “Mvetserani bwino mawu anga; ichi chikhale chitonthozo changa chochokera kwa inu.
Hoort aandachtelijk mijn rede, en laat dit zijn uw vertroostingen.
3 Ndiloleni ndiyankhule ndipo ndikatha kuyankhula munditonzetonze.
Verdraagt mij, en ik zal spreken; en nadat ik gesproken zal hebben, spot dan.
4 “Kodi ine ndikudandaulira munthu? Tsono ndilekerenji kupsa mtima?
Is (mij aangaande) mijn klacht tot den mens? Doch of het zo ware, waarom zou mijn geest niet verdrietig zijn?
5 Ndipenyeni ndipo mudabwe; mugwire dzanja pakamwa.
Ziet mij aan, en wordt verbaasd, en legt de hand op den mond.
6 Ndikamaganiza zimenezi ndimachita mantha kwambiri; thupi langa limanjenjemera.
Ja, wanneer ik daaraan gedenk, zo word ik beroerd, en mijn vlees heeft een gruwen gevat.
7 Chifukwa chiyani anthu oyipa amakhalabe ndi moyo, amakalamba ndi kusanduka amphamvu?
Waarom leven de goddelozen, worden oud, ja, worden geweldig in vermogen?
8 Amaona ana awo akukhazikika pamodzi nawo, zidzukulu zawo zikukula bwino iwo akuona.
Hun zaad is bestendig met hen voor hun aangezicht, en hun spruiten zijn voor hun ogen.
9 Mabanja awo amakhala pa mtendere ndipo sakhala ndi mantha; mkwapulo wa Mulungu suwakhudza nʼkomwe.
Hun huizen hebben vrede zonder vreze, en de roede Gods is op hen niet.
10 Ngʼombe zawo zazimuna sizilephera kubereketsa; ngʼombe zawo zazikazi sizipoloza.
Zijn stier bespringt, en mist niet; zijn koe kalft, en misdraagt niet.
11 Amatulutsa ana awo ngati gulu la nkhosa; makanda awo amavinavina pabwalo.
Hun jonge kinderen zenden zij uit als een kudde, en hun kinderen huppelen.
12 Amayimba nyimbo pogwiritsa ntchito matambolini ndi azeze; amakondwa pakumva kulira kwa chitoliro.
Zij heffen op met de trommel en de harp, en zij verblijden zich op het geluid des orgels.
13 Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero ndipo amatsikira ku manda mwamtendere. (Sheol h7585)
In het goede verslijten zij hun dagen; en in een ogenblik dalen zij in het graf. (Sheol h7585)
14 Koma anthuwo amawuza Mulungu kuti, ‘Tichokereni!’ Ife tilibe chikhumbokhumbo chofuna kudziwa njira zanu.
Nochtans zeggen zij tot God: Wijk van ons, want aan de kennis Uwer wegen hebben wij geen lust.
15 Kodi Wamphamvuzonseyo ndani kuti timutumikire? Ife tipindula chiyani tikamapemphera kwa Iyeyo?
Wat is de Almachtige, dat wij Hem zouden dienen? En wat baat zullen wij hebben, dat wij Hem aanlopen zouden?
16 Komatu ulemerero wawo suli mʼmanja mwawo, koma ine ndimakhala patali ndi uphungu wa anthu oyipa.
Doch ziet, hun goed is niet in hun hand; de raad der goddelozen is verre van mij.
17 “Koma nʼkangati kamene nyale ya anthu oyipa imazimitsidwa? Nʼkangati kamene tsoka limawagwera? Nʼkangati kamene Mulungu amawakwiyira ndi kuwalanga?
Hoe dikwijls geschiedt het, dat de lamp der goddelozen uitgeblust wordt, en hun verderf hun overkomt; dat God hun smarten uitdeelt in Zijn toorn!
18 Nʼkangati kamene iwo amakhala ngati phesi lowuluka ndi mphepo, ngati mungu wowuluzika ndi kamvuluvulu?
Dat zij gelijk stro worden voor den wind, en gelijk kaf, dat de wervelwind wegsteelt;
19 Paja amati, ‘Mulungu amalanga ana chifukwa cha machimo abambo awo.’ Koma Mulungu amabwezera chilango munthuyo, kuti adziwe kuti Mulungu amalangadi.
Dat God Zijn geweld weglegt voor Zijn kinderen, hem vergeldt, dat hij het gewaar wordt;
20 Mulole kuti adzionere yekha chilango chake, kuti alawe ukali wa Wamphamvuzonse.
Dat zijn ogen zijn ondergang zien, en hij drinkt van de grimmigheid des Almachtigen!
21 Nanga kodi amalabadira chiyani zabanja lake limene walisiya mʼmbuyo, pamene chiwerengero cha masiku ake chatha?
Want wat lust zou hij na zich aan zijn huis hebben, als het getal zijner maanden afgesneden is?
22 “Kodi alipo wina amene angaphunzitse Mulungu nzeru, poti Iye amaweruza ngakhale anthu apamwamba?
Zal men God wetenschap leren, daar Hij de hogen richt?
23 Munthu wina amamwalira ali ndi mphamvu zonse, ali pa mtendere ndi pa mpumulo,
Deze sterft in de kracht zijner volkomenheid, daar hij gans stil en gerust was;
24 thupi lake lili lonenepa, mafupa ake ali odzaza ndi mafuta.
Zijn melkvaten waren vol melk, en het merg zijner benen was bevochtigd.
25 Munthu wina amamwalira ali wowawidwa mtima, wosalawapo chinthu chabwino chilichonse.
De ander daarentegen sterft met een bittere ziel, en hij heeft van het goede niet gegeten.
26 Olemera ndi osauka omwe amamwalira ndi kuyikidwa mʼmanda ndipo onse amatuluka mphutsi.
Zij liggen te zamen neder in het stof, en het gewormte overdekt ze.
27 “Ndikudziwa bwino zimene mukuganiza, ziwembu zanu zomwe mukuti mundichitire.
Ziet, ik weet ulieder gedachten, en de boze verdichtselen, waarmede gij tegen mij geweld doet.
28 Inu mukuti, ‘Kodi nyumba ya mkulu uja ili kuti, matenti amene munkakhala anthu oyipa aja ali kuti?’
Want gij zult zeggen: Waar is het huis van den prins, en waar is de tent van de woningen der goddelozen?
29 Kodi munawafunsapo anthu amene ali pa ulendo? Kodi munaganizirapo zimene iwo amanena?
Hebt gijlieden niet gevraagd de voorbijgaanden op den weg, en kent gij hun tekenen niet?
30 Zakuti munthu woyipa amasungidwa chifukwa cha tsiku la tsoka, kuti amapulumutsidwa chifukwa cha tsiku la ukali wa Mulungu?
Dat de boze onttrokken wordt ten dage des verderfs; dat zij ten dage der verbolgenheden ontvoerd worden.
31 Kodi ndani amadzudzula munthu wochimwayo? Ndani amamubwezera zoyipa zimene anachita?
Wie zal hem in het aangezicht zijn weg vertonen? Als hij wat doet, wie zal hem vergelden?
32 Iye amanyamulidwa kupita ku manda ndipo anthu amachezera pa manda ake.
Eindelijk wordt hij naar de graven gebracht, en is gedurig in den aardhoop.
33 Dothi la ku chigwa limamukomera; anthu onse amatsatira mtembo wake, ndipo anthu osawerengeka amakhala patsogolo pa chitanda chakecho.
De kluiten des dals zijn hem zoet, en hij trekt na zich alle mensen; en dergenen, die voor hem geweest zijn, is geen getal.
34 “Nanga inu mudzanditonthoza bwanji ine ndi mawu anu opandapakewo palibe chimene chatsala kuti muyankhe koma mabodza basi!”
Hoe vertroost gij mij dan met ijdelheid, dewijl in uw antwoorden overtreding overig is?

< Yobu 21 >