< Yobu 21 >
1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
A odpovídaje Job, řekl:
2 “Mvetserani bwino mawu anga; ichi chikhale chitonthozo changa chochokera kwa inu.
Poslouchejte pilně řeči mé, a bude mi to za potěšení od vás.
3 Ndiloleni ndiyankhule ndipo ndikatha kuyankhula munditonzetonze.
Postrpte mne, abych i já mluvil, a když odmluvím, posmívejž se.
4 “Kodi ine ndikudandaulira munthu? Tsono ndilekerenji kupsa mtima?
Zdaliž já před člověkem naříkám? A poněvadž jest proč, jakž nemá býti ssoužen duch můj?
5 Ndipenyeni ndipo mudabwe; mugwire dzanja pakamwa.
Pohleďte na mne, a užasněte se, a položte prst na ústa.
6 Ndikamaganiza zimenezi ndimachita mantha kwambiri; thupi langa limanjenjemera.
Ano já sám, když rozvažuji své bídy, tedy se děsím, a spopadá tělo mé hrůza.
7 Chifukwa chiyani anthu oyipa amakhalabe ndi moyo, amakalamba ndi kusanduka amphamvu?
Proč bezbožní živi jsou, k věku starému přicházejí, též i bohatnou?
8 Amaona ana awo akukhazikika pamodzi nawo, zidzukulu zawo zikukula bwino iwo akuona.
Símě jejich stálé jest před oblíčejem jejich s nimi, a rodina jejich před očima jejich.
9 Mabanja awo amakhala pa mtendere ndipo sakhala ndi mantha; mkwapulo wa Mulungu suwakhudza nʼkomwe.
Domové jejich bezpečni jsou před strachem, aniž metla Boží na nich.
10 Ngʼombe zawo zazimuna sizilephera kubereketsa; ngʼombe zawo zazikazi sizipoloza.
Býk jejich připouštín bývá, ale ne na prázdno; kráva jejich rodí, a nepotracuje plodu.
11 Amatulutsa ana awo ngati gulu la nkhosa; makanda awo amavinavina pabwalo.
Vypouštějí jako stádo maličké své, a synové jejich poskakují.
12 Amayimba nyimbo pogwiritsa ntchito matambolini ndi azeze; amakondwa pakumva kulira kwa chitoliro.
Povyšují hlasu při bubnu a harfě, a veselí se k zvuku muziky.
13 Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero ndipo amatsikira ku manda mwamtendere. (Sheol )
Tráví v štěstí dny své, a v okamžení do hrobu sstupují. (Sheol )
14 Koma anthuwo amawuza Mulungu kuti, ‘Tichokereni!’ Ife tilibe chikhumbokhumbo chofuna kudziwa njira zanu.
Kteříž říkají Bohu silnému: Odejdi od nás, nebo známosti cest tvých neoblibujeme.
15 Kodi Wamphamvuzonseyo ndani kuti timutumikire? Ife tipindula chiyani tikamapemphera kwa Iyeyo?
Kdo jest Všemohoucí, abychom sloužili jemu? A jaký toho zisk, že bychom se modlili jemu?
16 Komatu ulemerero wawo suli mʼmanja mwawo, koma ine ndimakhala patali ndi uphungu wa anthu oyipa.
Ale pohleď, že není v moci jejich štěstí jejich, pročež rada bezbožných vzdálena jest ode mne.
17 “Koma nʼkangati kamene nyale ya anthu oyipa imazimitsidwa? Nʼkangati kamene tsoka limawagwera? Nʼkangati kamene Mulungu amawakwiyira ndi kuwalanga?
Èasto-liž svíce bezbožných hasne? Přichází-liž na ně bída jejich? Poděluje-liž je bolestmi Bůh v hněvě svém?
18 Nʼkangati kamene iwo amakhala ngati phesi lowuluka ndi mphepo, ngati mungu wowuluzika ndi kamvuluvulu?
Bývají-liž jako plevy před větrem, a jako drtiny, kteréž zachvacuje vicher?
19 Paja amati, ‘Mulungu amalanga ana chifukwa cha machimo abambo awo.’ Koma Mulungu amabwezera chilango munthuyo, kuti adziwe kuti Mulungu amalangadi.
Odkládá-liž Bůh synům bezbožníka nepravost jeho? Odplacuje-liž jemu tak, aby to znáti mohl,
20 Mulole kuti adzionere yekha chilango chake, kuti alawe ukali wa Wamphamvuzonse.
A aby viděly oči jeho neštěstí jeho, a prchlivost Všemohoucího že by pil?
21 Nanga kodi amalabadira chiyani zabanja lake limene walisiya mʼmbuyo, pamene chiwerengero cha masiku ake chatha?
O dům pak jeho po něm jaká jest péče jeho, když počet měsíců jeho bude umenšen?
22 “Kodi alipo wina amene angaphunzitse Mulungu nzeru, poti Iye amaweruza ngakhale anthu apamwamba?
Zdali Boha silného kdo učiti bude umění, kterýž sám vysokosti soudí?
23 Munthu wina amamwalira ali ndi mphamvu zonse, ali pa mtendere ndi pa mpumulo,
Tento umírá v síle dokonalosti své, všelijak bezpečný a pokojný.
24 thupi lake lili lonenepa, mafupa ake ali odzaza ndi mafuta.
Prsy jeho plné jsou mléka, a mozk kostí jeho svlažován bývá.
25 Munthu wina amamwalira ali wowawidwa mtima, wosalawapo chinthu chabwino chilichonse.
Jiný pak umírá v hořkosti ducha, kterýž nikdy nejídal s potěšením.
26 Olemera ndi osauka omwe amamwalira ndi kuyikidwa mʼmanda ndipo onse amatuluka mphutsi.
Jednostejně v prachu lehnou, a červy se rozlezou.
27 “Ndikudziwa bwino zimene mukuganiza, ziwembu zanu zomwe mukuti mundichitire.
Aj, známť myšlení vaše, a chytrosti, kteréž proti mně neprávě vymýšlíte.
28 Inu mukuti, ‘Kodi nyumba ya mkulu uja ili kuti, matenti amene munkakhala anthu oyipa aja ali kuti?’
Nebo pravíte: Kde jest dům urozeného? A kde stánek příbytků bezbožných?
29 Kodi munawafunsapo anthu amene ali pa ulendo? Kodi munaganizirapo zimene iwo amanena?
Což jste se netázali jdoucích cestou? Zkušení-liž aspoň jejich nepovolíte,
30 Zakuti munthu woyipa amasungidwa chifukwa cha tsiku la tsoka, kuti amapulumutsidwa chifukwa cha tsiku la ukali wa Mulungu?
Že v den neštěstí ochranu mívá bezbožný, v den, pravím, rozhněvání přistřín bývá?
31 Kodi ndani amadzudzula munthu wochimwayo? Ndani amamubwezera zoyipa zimene anachita?
Kdo jemu oznámí zjevně cestu jeho? Aneb za to, co činil, kdo jemu odplatí?
32 Iye amanyamulidwa kupita ku manda ndipo anthu amachezera pa manda ake.
A však i on k hrobu vyprovozen bude, a tam zůstane.
33 Dothi la ku chigwa limamukomera; anthu onse amatsatira mtembo wake, ndipo anthu osawerengeka amakhala patsogolo pa chitanda chakecho.
Sladnou jemu hrudy údolí, nadto za sebou všecky lidi táhne, těch pak, kteříž ho předešli, není počtu.
34 “Nanga inu mudzanditonthoza bwanji ine ndi mawu anu opandapakewo palibe chimene chatsala kuti muyankhe koma mabodza basi!”
Hle, jak vy mne marně troštujete, nebo v odpovědech vašich nezůstává než faleš.