< Yobu 20 >

1 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
Na Naamani Sofar buae se,
2 “Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe chifukwa ndasautsidwa kwambiri.
Me tirim mu ntew me, na ɛhyɛ me sɛ mimmua efisɛ me ho yeraw me yiye.
3 Ndikumva kudzudzula kondinyoza, ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.
Mate animka bi a egu me ho fi, na ntease a minya no hyɛ me sɛ mimmua.
4 “Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale, kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,
“Ampa ara wunim sɛnea nneɛma te fi tete, efi bere a wɔde nnipa duaa asase so no,
5 kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha, chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.
sɛ amumɔyɛfo ani gye bere tiaa bi mu, na wɔn a wonsuro nyame nso anigye nkyɛ.
6 Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba ndipo mutu wake uli nengʼaa,
Ɛwɔ mu sɛ nʼahohoahoa kodu ɔsoro, na ne ti kɔpem omununkum koraa a,
7 iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe; iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’
ɔbɛyera afebɔɔ te sɛ nʼankasa nʼagyanan; na wɔn a wohuu no no bebisa se, ‘Ɔwɔ he?’
8 Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso, adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.
Otu kɔ te sɛ ɔdae, na wɔrenhu no bio, wɔn werɛ fi te sɛ anadwo mu anisoadehu.
9 Diso limene linamuona silidzamuonanso; sadzapezekanso pamalo pake.
Ani a ehuu no no renhu no bio; na ne sibea nso renhu no bio.
10 Ana ake adzabwezera zonse zimene iyeyo analanda anthu osauka;
Ne mma bɛpata ahiafo; ɛsɛ sɛ nʼankasa de nʼahonya san ma.
11 Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake zidzagona naye limodzi mʼfumbi.
Ne mmerantebere mu ahoɔden a ahyɛ ne nnompe ma no ne no bɛkɔ mfutuma mu.
12 “Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,
“Ɛwɔ mu sɛ bɔne yɛ nʼanom dɛ na ɔde sie ne tɛkrɛma ase,
13 ngakhale salola kuzilavula, ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,
ɛwɔ mu sɛ ontumi nnyaa mu na ɔma ɛka ne dudom,
14 koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake; chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.
nanso, nʼaduan bɛyɛ nwen wɔ ne yafunu mu; ɛbɛyɛ ɔwɔ ano bɔre wɔ ne mu.
15 Adzachisanza chuma chimene anachimeza; Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.
Ɔbɛfe ahonyade a ɔmenee no; Onyankopɔn bɛma ne yafunu apuw agu.
16 Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo ululu wa mphiri udzamupha.
Ɔbɛfefe awɔ bɔre; Ɔnanka se bekum no.
17 Sadzasangalala ndi timitsinje, mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.
Ɔrennya nsuwansuwa no nnom nsubɔnten a nufusu ne ɛwo sen wɔ mu no.
18 Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya; sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.
Ɔbɛdan nea ɔbrɛ nyae no aba a ɔrenni bi; ɔremfa nʼaguadi mu mfaso nnye nʼani.
19 Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo; iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.
Efisɛ ɔhyɛɛ ahiafo so ma wodii ohia buruburoo; ɔde ne nsa ato afi a ɛnyɛ ɔno na osii so.
20 “Chifukwa choti umbombo wake sutha, sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.
“Ampa ara ɔrennya ahomegye mfi nea wapere anya no mu; ɔrentumi mfa nʼademude nnye ne ho nkwa.
21 Palibe chatsala kuti iye adye; chuma chake sichidzachedwa kutha.
Wafom nneɛma nyinaa awie; ne nkɔso nnu baabiara.
22 Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera; mavuto aakulu adzamugwera.
Nʼadedodow nyinaa mu no, ɔbɛkɔ ɔhaw mu; na amanehunu a emu yɛ den bɛto no.
23 Akadya nʼkukhuta, Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto ngati mvula yosalekeza.
Bere a nʼafuru ayɛ ma no, Onyankopɔn bɛtɔ nʼabufuw gya agu ne so na wabobɔ no basabasa.
24 Ngakhale athawe mkondo wachitsulo, muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.
Ɛwɔ mu sɛ oguan fi dade akode ano nanso bɛmma a ano yɛ kɔbere mfrafrae bɛwɔ no.
25 Muviwo adzawutulutsira ku msana, songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake. Adzagwidwa ndi mantha aakulu;
Ɔtwe bɛmma no fi nʼakyi, ano hyɛnhyɛn no fi ne brɛbo mu. Ehu bɛba ne so;
26 mdima wandiweyani ukudikira chuma chake. Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.
sum kabii retwɛn nʼademude. Ogya a ɛnnɛw mu bɛhyew no, na asɛe nea aka wɔ ne ntamadan mu.
27 Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake; dziko lapansi lidzamuwukira.
Ɔsoro bɛda nʼafɔdi adi, na asase asɔre atia no.
28 Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake, katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.
Nsuyiri bɛtwe ne fi akɔ, saa ara na asuworo bɛyɛ Onyankopɔn abufuwhyew da no.
29 Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa, mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”
Eyi ne nkrabea a Onyankopɔn de ma amumɔyɛfo, agyapade a Onyankopɔn de ato hɔ ama wɔn ne no.”

< Yobu 20 >