< Yobu 20 >

1 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
Naamalı Sofar şöyle yanıtladı:
2 “Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe chifukwa ndasautsidwa kwambiri.
“Sıkıntılı düşüncelerim beni yanıt vermeye zorluyor, Bu yüzden çok heyecanlıyım.
3 Ndikumva kudzudzula kondinyoza, ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.
Beni utandıran bir azar işitiyorum, Anlayışım yanıt vermemi gerektiriyor.
4 “Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale, kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,
“Bilmiyor musun eskiden beri, İnsan dünyaya geldiğinden beri,
5 kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha, chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.
Kötünün zafer çığlığı kısadır, Tanrısızın sevinciyse bir anlıktır.
6 Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba ndipo mutu wake uli nengʼaa,
Boyu göklere erişse, Başı bulutlara değse bile,
7 iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe; iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’
Sonsuza dek yok olacak, kendi pisliği gibi; Onu görmüş olanlar, ‘Nerede o?’ diyecekler.
8 Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso, adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.
Düş gibi uçacak, bir daha bulunamayacak, Gece görümü gibi yok olacak.
9 Diso limene linamuona silidzamuonanso; sadzapezekanso pamalo pake.
Kendisini görmüş olan gözler bir daha onu görmeyecek, Yaşadığı yerde artık görünmeyecektir.
10 Ana ake adzabwezera zonse zimene iyeyo analanda anthu osauka;
Çocukları yoksulların lütfunu dileyecek, Malını kendi eliyle geri verecektir.
11 Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake zidzagona naye limodzi mʼfumbi.
Kemiklerini dolduran gençlik ateşi Kendisiyle birlikte toprakta yatacak.
12 “Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,
“Kötülük ağzında tatlı gözükse, Onu dilinin altına gizlese bile,
13 ngakhale salola kuzilavula, ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,
Tutsa, bırakmasa, Damağının altına saklasa bile,
14 koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake; chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.
Yediği yiyecek midesinde ekşiyecek, İçinde kobra zehirine dönüşecek.
15 Adzachisanza chuma chimene anachimeza; Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.
Yuttuğu servetleri kusacak, Tanrı onları midesinden çıkaracak.
16 Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo ululu wa mphiri udzamupha.
Kobra zehiri emecek, Engereğin zehir dişi onu öldürecek.
17 Sadzasangalala ndi timitsinje, mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.
Akarsuların, bal ve ayran akan derelerin Sefasını süremeyecek.
18 Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya; sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.
Zahmetle kazandığını Yemeden geri verecek, Elde ettiği kazancın tadını çıkaramayacak.
19 Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo; iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.
Çünkü yoksulları ezip yüzüstü bıraktı, Kendi yapmadığı evi zorla aldı.
20 “Chifukwa choti umbombo wake sutha, sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.
“Hırsı yüzünden rahat nedir bilmedi, Serveti onu kurtaramayacak.
21 Palibe chatsala kuti iye adye; chuma chake sichidzachedwa kutha.
Yediğinden artakalan olmadı, Bu yüzden bolluğu uzun sürmeyecek.
22 Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera; mavuto aakulu adzamugwera.
Varlık içinde yokluk çekecek, Sıkıntı tepesine binecek.
23 Akadya nʼkukhuta, Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto ngati mvula yosalekeza.
Karnını tıka basa doyurduğunda, Tanrı kızgın öfkesini ondan çıkaracak, Üzerine gazap yağdıracak.
24 Ngakhale athawe mkondo wachitsulo, muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.
Demir silahtan kaçacak olsa, Tunç ok onu delip geçecek.
25 Muviwo adzawutulutsira ku msana, songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake. Adzagwidwa ndi mantha aakulu;
Çekilince ok sırtından, Parıldayan ucu ödünden çıkacak, Dehşet çökecek üzerine.
26 mdima wandiweyani ukudikira chuma chake. Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.
Koyu karanlık onun hazinelerini gözlüyor. Körüklenmemiş ateş onu yiyip bitirecek, Çadırında artakalanı tüketecek.
27 Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake; dziko lapansi lidzamuwukira.
Suçunu gökler açığa çıkaracak, Yeryüzü ona karşı ayaklanacak.
28 Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake, katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.
Varlığını seller, Azgın sular götürecek Tanrı'nın öfkelendiği gün.
29 Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa, mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”
Budur kötünün Tanrı'dan aldığı pay, Budur Tanrı'nın ona verdiği miras.”

< Yobu 20 >