< Yobu 20 >

1 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
Entonces Sofar naamatita respondió:
2 “Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe chifukwa ndasautsidwa kwambiri.
Ciertamente mis pensamientos me impulsan a responder, a causa de mi agitación interna.
3 Ndikumva kudzudzula kondinyoza, ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.
Oí una reprensión que me afrenta, y el espíritu de mi entendimiento hace que responda.
4 “Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale, kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,
¿No sabes que desde la antigüedad, desde cuando el hombre fue puesto en la tierra,
5 kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha, chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.
el triunfo de los perversos es efímero, y la alegría del impío es momentánea?
6 Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba ndipo mutu wake uli nengʼaa,
Aunque su altivez suba hasta el cielo, y su cabeza toque las nubes,
7 iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe; iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’
como su estiércol perecerá para siempre. Los que lo veían preguntarán: ¿Dónde está?
8 Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso, adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.
Se esfumará como un sueño, y no será hallado. Se disipará como visión nocturna.
9 Diso limene linamuona silidzamuonanso; sadzapezekanso pamalo pake.
El ojo que lo miraba ya no lo verá, ni su lugar volverá a contemplarlo.
10 Ana ake adzabwezera zonse zimene iyeyo analanda anthu osauka;
Tendrá que devolver sus riquezas. Sus hijos pedirán el favor de los pobres.
11 Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake zidzagona naye limodzi mʼfumbi.
Sus huesos aún llenos de vigor juvenil se acostarán con él en el polvo.
12 “Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,
Aunque la maldad sea dulce en su boca, la oculte debajo de su lengua,
13 ngakhale salola kuzilavula, ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,
la retenga y no la quiera soltar, y la mantenga en su paladar,
14 koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake; chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.
su comida se pudrirá en sus intestinos. Veneno de víboras hay dentro de él.
15 Adzachisanza chuma chimene anachimeza; Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.
Devoró riquezas, pero las vomitará. ʼElohim las sacará de su sistema digestivo.
16 Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo ululu wa mphiri udzamupha.
Chupará el veneno de la víbora, y la lengua de la serpiente lo matará.
17 Sadzasangalala ndi timitsinje, mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.
No verá los arroyos que fluyen, los torrentes que fluyen leche y miel.
18 Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya; sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.
Devolverá el fruto de su labor sin tragarlo, y no disfrutará el lucro de su negocio,
19 Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo; iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.
porque oprimió y desamparó al pobre, y se apoderó de casas que no construyó.
20 “Chifukwa choti umbombo wake sutha, sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.
Porque su sistema digestivo no conoció la tranquilidad, nada retendrá de lo que más codiciaba.
21 Palibe chatsala kuti iye adye; chuma chake sichidzachedwa kutha.
Por cuanto nada escapó a su rapacidad, su prosperidad no será duradera.
22 Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera; mavuto aakulu adzamugwera.
En la plenitud de su abundancia sufrirá estrechez. La mano de todo el que sufre se levantará contra él.
23 Akadya nʼkukhuta, Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto ngati mvula yosalekeza.
Cuando en su estómago ya no entre más, ʼElohim enviará sobre él el furor de su ira, y la hará llover sobre él mientras come.
24 Ngakhale athawe mkondo wachitsulo, muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.
Huirá de las armas de hierro, pero lo traspasará una flecha de bronce.
25 Muviwo adzawutulutsira ku msana, songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake. Adzagwidwa ndi mantha aakulu;
Si logra sacarse la flecha, ciertamente le sale por la espalda. ¡Ciertamente, la punta reluciente sale de su hiel! Sobre él se vienen terrores.
26 mdima wandiweyani ukudikira chuma chake. Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.
Toda la tenebrosidad está reservada para sus tesoros. Un fuego no atizado los devorará, y consumirá lo que quede en su vivienda.
27 Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake; dziko lapansi lidzamuwukira.
El cielo revelará su iniquidad, y la tierra se levantará contra él.
28 Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake, katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.
Las riquezas de su casa se perderán. Serán arrasadas en el día de su furor.
29 Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa, mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”

< Yobu 20 >