< Yobu 20 >

1 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
Entonces Zofar, el naamatita, respondió,
2 “Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe chifukwa ndasautsidwa kwambiri.
“Por eso me responden mis pensamientos, incluso a causa de la prisa que hay en mí.
3 Ndikumva kudzudzula kondinyoza, ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.
He oído la reprimenda que me avergüenza. El espíritu de mi entendimiento me responde.
4 “Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale, kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,
¿No sabes esto desde hace tiempo, desde que el hombre fue puesto en la tierra,
5 kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha, chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.
que el triunfo de los malvados es corto, la alegría de los impíos sino por un momento?
6 Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba ndipo mutu wake uli nengʼaa,
Aunque su altura llegue hasta los cielos, y su cabeza llega a las nubes,
7 iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe; iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’
pero perecerá para siempre como su propio estiércol. Los que lo han visto dirán: “¿Dónde está?”.
8 Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso, adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.
Se irá volando como un sueño, y no será encontrado. Sí, se le ahuyentará como una visión de la noche.
9 Diso limene linamuona silidzamuonanso; sadzapezekanso pamalo pake.
El ojo que lo vio no lo verá más, ni su lugar lo verá más.
10 Ana ake adzabwezera zonse zimene iyeyo analanda anthu osauka;
Sus hijos buscarán el favor de los pobres. Sus manos devolverán su riqueza.
11 Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake zidzagona naye limodzi mʼfumbi.
Sus huesos están llenos de su juventud, pero la juventud se acostará con él en el polvo.
12 “Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,
“Aunque la maldad es dulce en su boca, aunque lo esconde bajo la lengua,
13 ngakhale salola kuzilavula, ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,
aunque la perdona, y no la deja ir, pero mantenerlo quieto dentro de su boca,
14 koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake; chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.
sin embargo, su comida en sus intestinos se vuelve. Es el veneno de la cobra dentro de él.
15 Adzachisanza chuma chimene anachimeza; Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.
Se ha tragado las riquezas y las volverá a vomitar. Dios los echará de su vientre.
16 Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo ululu wa mphiri udzamupha.
Chupará el veneno de la cobra. La lengua de la víbora lo matará.
17 Sadzasangalala ndi timitsinje, mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.
No mirará los ríos, los flujos de miel y mantequilla.
18 Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya; sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.
El restaurará aquello por lo que trabajó, y no se lo tragará. No se regocijará según la sustancia que haya obtenido.
19 Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo; iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.
Porque ha oprimido y abandonado a los pobres. Ha quitado violentamente una casa, y no la construirá.
20 “Chifukwa choti umbombo wake sutha, sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.
“Porque no conoció la tranquilidad en su interior, no guardará nada de aquello en lo que se deleita.
21 Palibe chatsala kuti iye adye; chuma chake sichidzachedwa kutha.
No quedó nada que no devorara, por lo que su prosperidad no perdurará.
22 Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera; mavuto aakulu adzamugwera.
En la plenitud de su suficiencia, la angustia lo alcanzará. La mano de todos los que están en la miseria vendrá sobre él.
23 Akadya nʼkukhuta, Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto ngati mvula yosalekeza.
Cuando esté a punto de llenar su vientre, Dios arrojará sobre él el ardor de su ira. Le lloverá encima mientras come.
24 Ngakhale athawe mkondo wachitsulo, muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.
Huirá del arma de hierro. La flecha de bronce lo atravesará.
25 Muviwo adzawutulutsira ku msana, songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake. Adzagwidwa ndi mantha aakulu;
Lo extrae y sale de su cuerpo. Sí, el punto brillante sale de su hígado. Los terrores están sobre él.
26 mdima wandiweyani ukudikira chuma chake. Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.
Toda la oscuridad está guardada para sus tesoros. Un fuego no avivado lo devorará. Consumirá lo que queda en su tienda.
27 Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake; dziko lapansi lidzamuwukira.
Los cielos revelarán su iniquidad. La tierra se levantará contra él.
28 Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake, katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.
El aumento de su casa se irá. Se precipitarán en el día de su ira.
29 Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa, mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”
Esta es la porción de un hombre malvado de Dios, la herencia que le ha sido asignada por Dios”.

< Yobu 20 >