< Yobu 20 >

1 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
Potem je odgovoril Cofár Naámčan in rekel:
2 “Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe chifukwa ndasautsidwa kwambiri.
»Zato mi moje misli povzročajo, da odgovorim in zaradi tega hitim.
3 Ndikumva kudzudzula kondinyoza, ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.
Slišal sem preverjanje svoje graje in duh mojega razumevanja mi povzroča, da odgovorim.
4 “Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale, kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,
Mar ne veš tega od davnine, odkar je bil človek postavljen na zemljo,
5 kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha, chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.
da je zmagoslavje zlobnega kratko, radost hinavca pa le za trenutek?
6 Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba ndipo mutu wake uli nengʼaa,
Čeprav se njegova odličnost vzpenja do neba in njegova glava sega do oblakov,
7 iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe; iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’
se bo vendarle pogubil za vedno, kot njegov lastni iztrebek. Tisti, ki so ga videli, bodo rekli: ›Kje je?‹
8 Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso, adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.
Odletel bo proč kakor sanje in ne bo ga najti. Da, pregnan bo kakor nočno videnje.
9 Diso limene linamuona silidzamuonanso; sadzapezekanso pamalo pake.
Tudi oko, ki ga je videlo, ga ne bo več videlo niti ga njegov kraj ne bo več gledal.
10 Ana ake adzabwezera zonse zimene iyeyo analanda anthu osauka;
Njegovi otroci bodo iskali, da ugodijo revnemu in njegove roke bodo obnovile njihove dobrine.
11 Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake zidzagona naye limodzi mʼfumbi.
Njegove kosti so polne greha iz njegove mladosti, ki se bodo ulegle z njim v prah.
12 “Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,
Čeprav je zlobnost sladka v njegovih ustih, čeprav to skriva pod svojim jezikom,
13 ngakhale salola kuzilavula, ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,
čeprav temu prizanaša in tega ne zapusti, temveč to mirno drži znotraj svojih ust,
14 koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake; chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.
je vendar njegova hrana v njegovi notranjosti spremenjena, to je žolč kober znotraj njega.
15 Adzachisanza chuma chimene anachimeza; Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.
Pogoltnil je bogastva in ponovno jih bo izbljuval. Bog jih bo izvrgel iz njegovega trebuha.
16 Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo ululu wa mphiri udzamupha.
Sesal bo strup kober, gadov jezik ga bo ubil.
17 Sadzasangalala ndi timitsinje, mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.
Ne bo videl rek, poplav, potokov iz meda in masla.
18 Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya; sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.
To, za kar se je trudil, bo povrnil in tega ne bo pogoltnil. Glede na njegovo imetje bo povračilo in v tem se ne bo veselil.
19 Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo; iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.
Ker je zatiral in zapustil ubogega, ker je nasilno odvzel hišo, ki je ni zgradil,
20 “Chifukwa choti umbombo wake sutha, sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.
zagotovo ne bo čutil spokojnosti v svojem trebuhu, ne bo rešil od tega, kar si je želel.
21 Palibe chatsala kuti iye adye; chuma chake sichidzachedwa kutha.
Ničesar ne bo ostalo od njegove hrane, zato noben človek ne bo gledal za njegovimi dobrinami.
22 Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera; mavuto aakulu adzamugwera.
V polnosti svoje zadostnosti bo v stiskah; vsaka roka zlobnega bo prišla nadenj.
23 Akadya nʼkukhuta, Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto ngati mvula yosalekeza.
Ko si namerava napolniti svoj trebuh, bo Bog nadenj vrgel razjarjenost svojega besa in ta bo deževala nadenj, medtem ko jé.
24 Ngakhale athawe mkondo wachitsulo, muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.
Pobegnil bo pred železnim orožjem in lok iz jekla ga bo prebodel.
25 Muviwo adzawutulutsira ku msana, songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake. Adzagwidwa ndi mantha aakulu;
Ta je izvlečen in prihaja iz telesa. Da, lesketajoč meč prihaja iz njegovega žolča; strahote so nad njim.
26 mdima wandiweyani ukudikira chuma chake. Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.
Vsa tema bo skrita v njegovih skritih krajih. Ogenj, ki se ni razgorel, ga bo požrl; slabo bo šlo s tistim, ki je ostal v njegovem šotoru.
27 Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake; dziko lapansi lidzamuwukira.
Nebesa bodo razodela njegovo krivičnost in zemlja se bo dvignila zoper njega.
28 Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake, katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.
Donos njegove hiše bo odšel in njegove dobrine bodo odtekle na dan njegovega besa.
29 Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa, mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”
To je delež zlobnemu človeku od Boga in od Boga določena mu dediščina.«

< Yobu 20 >