< Yobu 20 >

1 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
Respondens autem Sophar Naamathites, dixit:
2 “Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe chifukwa ndasautsidwa kwambiri.
[Idcirco cogitationes meæ variæ succedunt sibi, et mens in diversa rapitur.
3 Ndikumva kudzudzula kondinyoza, ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.
Doctrinam qua me arguis audiam, et spiritus intelligentiæ meæ respondebit mihi.
4 “Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale, kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,
Hoc scio a principio, ex quo positus est homo super terram,
5 kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha, chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.
quod laus impiorum brevis sit, et gaudium hypocritæ ad instar puncti.
6 Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba ndipo mutu wake uli nengʼaa,
Si ascenderit usque ad cælum superbia ejus, et caput ejus nubes tetigerit,
7 iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe; iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’
quasi sterquilinium in fine perdetur, et qui eum viderant, dicent: Ubi est?
8 Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso, adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.
Velut somnium avolans non invenietur: transiet sicut visio nocturna.
9 Diso limene linamuona silidzamuonanso; sadzapezekanso pamalo pake.
Oculus qui eum viderat non videbit, neque ultra intuebitur eum locus suus.
10 Ana ake adzabwezera zonse zimene iyeyo analanda anthu osauka;
Filii ejus atterentur egestate, et manus illius reddent ei dolorem suum.
11 Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake zidzagona naye limodzi mʼfumbi.
Ossa ejus implebuntur vitiis adolescentiæ ejus, et cum eo in pulvere dormient.
12 “Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,
Cum enim dulce fuerit in ore ejus malum, abscondet illud sub lingua sua.
13 ngakhale salola kuzilavula, ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,
Parcet illi, et non derelinquet illud, et celabit in gutture suo.
14 koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake; chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.
Panis ejus in utero illius vertetur in fel aspidum intrinsecus.
15 Adzachisanza chuma chimene anachimeza; Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.
Divitias quas devoravit evomet, et de ventre illius extrahet eas Deus.
16 Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo ululu wa mphiri udzamupha.
Caput aspidum suget, et occidet eum lingua viperæ.
17 Sadzasangalala ndi timitsinje, mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.
(Non videat rivulos fluminis, torrentes mellis et butyri.)
18 Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya; sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.
Luet quæ fecit omnia, nec tamen consumetur: juxta multitudinem adinventionum suarum, sic et sustinebit.
19 Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo; iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.
Quoniam confringens nudavit pauperes: domum rapuit, et non ædificavit eam.
20 “Chifukwa choti umbombo wake sutha, sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.
Nec est satiatus venter ejus: et cum habuerit quæ concupierat, possidere non poterit.
21 Palibe chatsala kuti iye adye; chuma chake sichidzachedwa kutha.
Non remansit de cibo ejus, et propterea nihil permanebit de bonis ejus.
22 Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera; mavuto aakulu adzamugwera.
Cum satiatus fuerit, arctabitur: æstuabit, et omnis dolor irruet super eum.
23 Akadya nʼkukhuta, Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto ngati mvula yosalekeza.
Utinam impleatur venter ejus, ut emittat in eum iram furoris sui, et pluat super illum bellum suum.
24 Ngakhale athawe mkondo wachitsulo, muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.
Fugiet arma ferrea, et irruet in arcum æreum.
25 Muviwo adzawutulutsira ku msana, songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake. Adzagwidwa ndi mantha aakulu;
Eductus, et egrediens de vagina sua, et fulgurans in amaritudine sua: vadent et venient super eum horribiles.
26 mdima wandiweyani ukudikira chuma chake. Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.
Omnes tenebræ absconditæ sunt in occultis ejus; devorabit eum ignis qui non succenditur: affligetur relictus in tabernaculo suo.
27 Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake; dziko lapansi lidzamuwukira.
Revelabunt cæli iniquitatem ejus, et terra consurget adversus eum.
28 Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake, katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.
Apertum erit germen domus illius: detrahetur in die furoris Dei.
29 Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa, mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”
Hæc est pars hominis impii a Deo, et hæreditas verborum ejus a Domino.]

< Yobu 20 >