< Yobu 20 >
1 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
Da antwortete Zophar, der Naamatiter, und sprach:
2 “Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe chifukwa ndasautsidwa kwambiri.
Darum veranlassen mich meine Gedanken zu einer Antwort, und deswegen drängt es mich [zu reden].
3 Ndikumva kudzudzula kondinyoza, ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.
Einen Verweis, mir zur Schande, muß ich vernehmen; aber mein Geist treibt mich zu antworten um meiner Einsicht willen.
4 “Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale, kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,
Weißt du nicht, daß von alters her, seit Menschen auf Erden sind,
5 kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha, chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.
der Gottlosen Frohlocken kurz ist und die Freude der Frevler nur einen Augenblick währt?
6 Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba ndipo mutu wake uli nengʼaa,
Wenn er schon bis zum Himmel erhoben würde und sein Haupt bis an die Wolken reichte,
7 iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe; iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’
so geht er doch, gleich seinem Kot, auf ewig unter, und die ihn gesehen, werden sagen: Wo ist er?
8 Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso, adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.
Wie ein Traum wird er verschwinden, man wird ihn nimmer finden, er vergeht wie ein Nachtgesicht.
9 Diso limene linamuona silidzamuonanso; sadzapezekanso pamalo pake.
Das Auge, das ihn gesehen, sieht ihn nimmer wieder, und seine Stätte kennt ihn nicht mehr.
10 Ana ake adzabwezera zonse zimene iyeyo analanda anthu osauka;
Seine Söhne müssen die Armen entschädigen und ihre Hände sein Vermögen wieder herausgeben.
11 Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake zidzagona naye limodzi mʼfumbi.
Seine Gebeine waren voller Jugendkraft: die liegt nun mit ihm im Staub.
12 “Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,
Ist das Böse noch so süß in seinem Munde, daß er es unter seiner Zunge birgt,
13 ngakhale salola kuzilavula, ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,
daß er es hegt und nicht lassen kann und an seinem Gaumen festhält:
14 koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake; chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.
so verwandelt sich doch seine Speise in seinem Eingeweide und wird in seinem Innern zu Schlangengift.
15 Adzachisanza chuma chimene anachimeza; Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.
Das verschlungene Gut muß er wieder von sich geben, Gott treibt es ihm aus dem Leibe heraus.
16 Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo ululu wa mphiri udzamupha.
Schlangengift hat er gesaugt: darum wird ihn die Zunge der Otter töten.
17 Sadzasangalala ndi timitsinje, mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.
Er wird seine Lust nicht sehen an den Bächen, den Strömen von Honig und von Milch.
18 Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya; sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.
Das Erworbene muß er zurückgeben, und er kann es nicht verschlingen; seines eingetauschten Gutes wird er nicht froh;
19 Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo; iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.
denn er hat Arme unterdrückt und sie liegen lassen, ein Haus beraubt, anstatt gebaut.
20 “Chifukwa choti umbombo wake sutha, sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.
Sein Bauch wußte nichts von Genügsamkeit; vor seiner Begehrlichkeit blieb nichts verschont.
21 Palibe chatsala kuti iye adye; chuma chake sichidzachedwa kutha.
Nichts entging seiner Freßgier, darum wird auch sein Gut nicht beständig sein.
22 Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera; mavuto aakulu adzamugwera.
Mitten in seinem Überfluß wird ihm angst, alle Hände der Unglücklichen kommen über ihn.
23 Akadya nʼkukhuta, Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto ngati mvula yosalekeza.
Es wird geschehen, während er seinen Bauch noch füllt, wird Er über ihn senden die Glut seines Zornes und wird auf ihn regnen lassen, in seine Speise hinein.
24 Ngakhale athawe mkondo wachitsulo, muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.
Flieht er vor der eisernen Rüstung, so wird ihn der eherne Bogen durchbohren.
25 Muviwo adzawutulutsira ku msana, songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake. Adzagwidwa ndi mantha aakulu;
Er zieht [daran], und der Pfeil geht aus seinem Leibe hervor, blitzend fährt er aus seiner Galle, und Todesschrecken kommen über ihn.
26 mdima wandiweyani ukudikira chuma chake. Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.
Alle Finsternis ist aufgespart für seine Schätze, ihn wird ein Feuer verzehren, das nicht ausgeblasen wird; es frißt weg, was in seinem Zelte übriggeblieben ist.
27 Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake; dziko lapansi lidzamuwukira.
Der Himmel wird seine Schuld offenbaren und die Erde sich wider ihn empören.
28 Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake, katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.
Der Reichtum seines Hauses fährt dahin, muß zerrinnen am Tage seines Zornes.
29 Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa, mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”
Das ist des gottlosen Menschen Teil von Gott, das Erbe, das Gott ihm zugesprochen hat.