< Yobu 20 >

1 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
Çophar de Naama prit la parole et dit:
2 “Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe chifukwa ndasautsidwa kwambiri.
Eh bien! Mes réflexions m’incitent à répliquer et aussi les impressions que je ressens.
3 Ndikumva kudzudzula kondinyoza, ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.
Quand j’entends des reproches qui sont un affront pour moi, ma raison me dicte une réponse.
4 “Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale, kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,
Connais-tu ce fait qui a existé de tout temps, depuis que l’homme est placé sur la terre:
5 kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha, chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.
que le triomphe des méchants est éphémère et que la joie du pervers ne dure qu’un instant?
6 Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba ndipo mutu wake uli nengʼaa,
Dût sa stature monter jusqu’au ciel et sa tête atteindre les nuages,
7 iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe; iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’
aussi sûrement que ses excréments, il périra sans retour: ceux qui le voyaient diront: "Où est-il?"
8 Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso, adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.
Comme un songe, il s’envole, et l’on perd ses traces; il s’évanouit comme une vision nocturne.
9 Diso limene linamuona silidzamuonanso; sadzapezekanso pamalo pake.
L’Œil qui l’a contemplé ne le découvre plus; sa demeure n’a plus de regard pour lui.
10 Ana ake adzabwezera zonse zimene iyeyo analanda anthu osauka;
Ses fils devront solliciter la pitié des pauvres, et ses propres mains restituer la fortune acquise.
11 Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake zidzagona naye limodzi mʼfumbi.
Ses membres, tout pleins encore de vigueur juvénile, se verront couchés dans la poussière.
12 “Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,
S’Il arrive que la perversité soit douce à sa bouche, qu’il la fasse glisser sous sa langue;
13 ngakhale salola kuzilavula, ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,
qu’il la ménage longtemps, ne cessant de la savourer, et la retienne encore au fond de son palais,
14 koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake; chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.
alors son aliment se transforme dans ses entrailles et devient dans son sein l’amer venin de l’aspic.
15 Adzachisanza chuma chimene anachimeza; Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.
Il a dévoré une fortune et il faut qu’il la rejette: Dieu l’expulsera de ses intestins.
16 Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo ululu wa mphiri udzamupha.
C’Est du poison d’aspic qu’il suçait: il périra par la langue de la vipère.
17 Sadzasangalala ndi timitsinje, mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.
Qu’il n’espère point se délecter aux flots des ruisseaux de miel, des torrents de lait!
18 Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya; sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.
Il faut qu’il rende le fruit de son labeur, avant de le consommer; il en sera de même des biens qu’il s’est acquis par ses échanges: il n’en tirera aucun plaisir.
19 Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo; iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.
C’Est qu’il a écrasé les faibles et les a abandonnés à eux-mêmes; il a ruiné des maisons par la rapine et ne les a point rebâties.
20 “Chifukwa choti umbombo wake sutha, sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.
C’Est qu’il n’a pas connu la paix intérieure: il ne sauvera rien de ses plus chers trésors.
21 Palibe chatsala kuti iye adye; chuma chake sichidzachedwa kutha.
Rien n’échappait à ses appétits; aussi son bien-être n’aura-t-il aucune durée.
22 Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera; mavuto aakulu adzamugwera.
Alors qu’il regorge de biens, il est dans la gêne; la main de tout misérable s’abattra sur lui.
23 Akadya nʼkukhuta, Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto ngati mvula yosalekeza.
Dieu se dispose à lui bourrer le ventre en lâchant contre lui son ardente colère, en la faisant pleuvoir sur lui en guise de nourriture.
24 Ngakhale athawe mkondo wachitsulo, muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.
II voudra fuir les armes de fer: il sera transpercé par un arc d’airain.
25 Muviwo adzawutulutsira ku msana, songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake. Adzagwidwa ndi mantha aakulu;
La flèche qui l’atteint, il la retire de son corps; elle sort étincelante du foie qu’elle a percé; l’épouvante le saisit.
26 mdima wandiweyani ukudikira chuma chake. Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.
Tous les noirs désastres menacent les trésors qu’il a amassés; un feu que personne n’a attisé le consume et dévore tout ce qui est resté dans sa demeure.
27 Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake; dziko lapansi lidzamuwukira.
Les cieux dénoncent son crime et la terre se soulève contre lui.
28 Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake, katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.
Les biens de sa maison s’en vont; tout s’écroule au jour de la colère divine.
29 Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa, mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”
Telle est la part que Dieu réserve à l’homme pervers; tel est l’héritage qui lui est destiné par la parole du Tout-Puissant.

< Yobu 20 >