< Yobu 20 >
1 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
Et Zophar, le Naamathite, prit la parole,
2 “Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe chifukwa ndasautsidwa kwambiri.
« C'est pourquoi mes pensées me répondent, à cause de la précipitation qui est en moi.
3 Ndikumva kudzudzula kondinyoza, ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.
J'ai entendu la réprimande qui me couvre de honte. L'esprit de mon intelligence me répond.
4 “Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale, kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,
Tu ne connais pas ça depuis longtemps, depuis que l'homme a été placé sur terre,
5 kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha, chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.
que le triomphe des méchants est court, la joie des impies, mais pour un moment?
6 Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba ndipo mutu wake uli nengʼaa,
Même si sa hauteur s'élève jusqu'aux cieux, et sa tête s'élève vers les nuages,
7 iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe; iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’
mais il périra à jamais comme son propre fumier. Ceux qui l'ont vu diront: « Où est-il? ».
8 Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso, adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.
Il s'envolera comme un rêve, et on ne le retrouvera pas. Oui, il sera chassé comme une vision de la nuit.
9 Diso limene linamuona silidzamuonanso; sadzapezekanso pamalo pake.
L'œil qui l'a vu ne le verra plus, et sa place ne le verra plus.
10 Ana ake adzabwezera zonse zimene iyeyo analanda anthu osauka;
Ses enfants rechercheront la faveur des pauvres. Ses mains lui rendront sa richesse.
11 Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake zidzagona naye limodzi mʼfumbi.
Ses os sont pleins de sa jeunesse, mais la jeunesse se couchera avec lui dans la poussière.
12 “Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,
« Bien que la méchanceté soit douce dans sa bouche, bien qu'il le cache sous sa langue,
13 ngakhale salola kuzilavula, ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,
bien qu'il l'épargne, et ne le lâche pas, mais la garder dans sa bouche,
14 koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake; chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.
mais sa nourriture dans ses entrailles est transformée. C'est du venin de cobra en lui.
15 Adzachisanza chuma chimene anachimeza; Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.
Il a englouti les richesses, et il les vomira. Dieu les chassera de son ventre.
16 Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo ululu wa mphiri udzamupha.
Il sucera du venin de cobra. La langue de la vipère va le tuer.
17 Sadzasangalala ndi timitsinje, mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.
Il ne regardera pas les fleuves, les ruisseaux de miel et de beurre qui coulent.
18 Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya; sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.
Il rétablira ce pour quoi il a travaillé, et ne l'engloutira pas. Il ne se réjouira pas selon la substance qu'il a obtenue.
19 Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo; iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.
Car il a opprimé et abandonné les pauvres. Il a violemment enlevé une maison, et il ne la reconstruira pas.
20 “Chifukwa choti umbombo wake sutha, sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.
« Parce qu'il ne connaissait pas le calme en lui, il n'épargnera rien de ce qui lui fait plaisir.
21 Palibe chatsala kuti iye adye; chuma chake sichidzachedwa kutha.
Il ne restait rien qu'il ne dévorât, donc sa prospérité ne durera pas.
22 Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera; mavuto aakulu adzamugwera.
Dans la plénitude de sa suffisance, la détresse le saisira. La main de tous ceux qui sont dans la misère viendra sur lui.
23 Akadya nʼkukhuta, Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto ngati mvula yosalekeza.
Quand il sera sur le point de se remplir le ventre, Dieu jettera sur lui l'ardeur de sa colère. Il va pleuvoir sur lui pendant qu'il mange.
24 Ngakhale athawe mkondo wachitsulo, muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.
Il fuira devant l'arme de fer. La flèche de bronze le transpercera.
25 Muviwo adzawutulutsira ku msana, songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake. Adzagwidwa ndi mantha aakulu;
Il la tire, et elle sort de son corps. Oui, le point brillant sort de son foie. Les terreurs sont sur lui.
26 mdima wandiweyani ukudikira chuma chake. Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.
Toutes les ténèbres sont mises en réserve pour ses trésors. Un feu non attisé le dévorera. Il consumera ce qui reste dans sa tente.
27 Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake; dziko lapansi lidzamuwukira.
Les cieux révéleront son iniquité. La terre se soulèvera contre lui.
28 Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake, katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.
L'accroissement de sa maison s'en ira. Ils s'enfuiront au jour de sa colère.
29 Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa, mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”
C'est la part de Dieu pour un méchant, l'héritage qui lui a été attribué par Dieu ».