< Yobu 20 >

1 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
and to answer Zophar [the] Naamathite and to say
2 “Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe chifukwa ndasautsidwa kwambiri.
to/for so disquietings my to return: reply me and in/on/with for the sake of to hasten I in/on/with me
3 Ndikumva kudzudzula kondinyoza, ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.
discipline shame my to hear: hear and spirit from understanding my to answer me
4 “Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale, kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,
this to know from perpetuity from to set: put man upon land: country/planet
5 kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha, chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.
for triumphing wicked from near and joy profane till moment
6 Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba ndipo mutu wake uli nengʼaa,
if to ascend: rise to/for heaven loftiness his and head his to/for cloud to touch
7 iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe; iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’
like/as dung his to/for perpetuity to perish to see: see him to say where? he
8 Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso, adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.
like/as dream to fly and not to find him and to wander like/as vision night
9 Diso limene linamuona silidzamuonanso; sadzapezekanso pamalo pake.
eye to see him and not to add: again and not still to see him place his
10 Ana ake adzabwezera zonse zimene iyeyo analanda anthu osauka;
son: child his to accept poor and hand his to return: return strength his
11 Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake zidzagona naye limodzi mʼfumbi.
bone his to fill (youth his *Q(K)*) and with him upon dust to lie down: lay down
12 “Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,
if be sweet in/on/with lip his distress: evil to hide her underneath: under tongue his
13 ngakhale salola kuzilavula, ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,
to spare upon her and not to leave: release her and to withhold her in/on/with midst palate his
14 koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake; chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.
food his in/on/with belly his to overturn gall cobra in/on/with entrails: among his
15 Adzachisanza chuma chimene anachimeza; Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.
strength: rich to swallow up and to vomit him from belly: abdomen his to possess: take him God
16 Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo ululu wa mphiri udzamupha.
poison cobra to suckle to kill him tongue viper
17 Sadzasangalala ndi timitsinje, mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.
not to see: see in/on/with stream river torrent: river honey and curd
18 Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya; sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.
to return: return toil and not to swallow up like/as strength: rich exchange his and not to rejoice
19 Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo; iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.
for to crush to leave: neglect poor house: home to plunder and not to build him
20 “Chifukwa choti umbombo wake sutha, sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.
for not to know at ease in/on/with belly: abdomen his in/on/with to desire his not to escape
21 Palibe chatsala kuti iye adye; chuma chake sichidzachedwa kutha.
nothing survivor to/for to eat he upon so not be firm goodness his
22 Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera; mavuto aakulu adzamugwera.
in/on/with to fill sufficiency his be distressed to/for him all hand labour(er) to come (in): come him
23 Akadya nʼkukhuta, Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto ngati mvula yosalekeza.
to be to/for to fill belly: abdomen his to send: depart in/on/with him burning anger face: anger his and to rain upon them in/on/with intestine his
24 Ngakhale athawe mkondo wachitsulo, muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.
to flee from weapon iron to pass him bow bronze
25 Muviwo adzawutulutsira ku msana, songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake. Adzagwidwa ndi mantha aakulu;
to draw and to come out: come from back and lightning from gall his to go: come upon him terror
26 mdima wandiweyani ukudikira chuma chake. Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.
all darkness to hide to/for to treasure his to eat him fire not to breathe be evil survivor in/on/with tent his
27 Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake; dziko lapansi lidzamuwukira.
to reveal: reveal heaven iniquity: crime his and land: country/planet to arise: attack to/for him
28 Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake, katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.
to reveal: remove crops house: home his to pour in/on/with day face: anger his
29 Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa, mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”
this portion man wicked from God and inheritance word his from God

< Yobu 20 >