< Yobu 20 >
1 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
Then responded Zophar the Naamathite, and said: —
2 “Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe chifukwa ndasautsidwa kwambiri.
Not so, do my thoughts answer me, and to this end, is my haste within me:
3 Ndikumva kudzudzula kondinyoza, ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.
The correction meant to confound me, I must hear, but, the spirit—out of my understanding, will give me a reply.
4 “Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale, kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,
Knowest thou, this—from antiquity, from the placing of man upon earth: —
5 kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha, chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.
That, the joy-shout of the lawless, is short, and, the rejoicing of the impious, for a moment?
6 Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba ndipo mutu wake uli nengʼaa,
Though his elevation mount up to the heavens, and, his head, to the clouds, doth reach,
7 iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe; iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’
Like his own stubble, shall he utterly perish, They who had seen him, shall say, Where is he?
8 Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso, adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.
Like a dream, shall he fly away, and they shall not find him, yea he shall be chased away, as a vision of the night.
9 Diso limene linamuona silidzamuonanso; sadzapezekanso pamalo pake.
The eye that hath scanned him, shall not do it again, neither, any more, shall his place behold him:
10 Ana ake adzabwezera zonse zimene iyeyo analanda anthu osauka;
His children, shall seek the favour of the poor, and, his own hand, shall give back his wealth.
11 Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake zidzagona naye limodzi mʼfumbi.
His bones, are full of youthful vigour, yet, with him—in the dust, shall it lie down.
12 “Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,
Though, a sweet taste in his mouth, be given by vice, though he hide it under his tongue;
13 ngakhale salola kuzilavula, ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,
Though he spare it, and will not let it go, but retain it in the midst of his mouth,
14 koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake; chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.
His food, in his stomach, is changed, the gall of adders, within him!
15 Adzachisanza chuma chimene anachimeza; Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.
Wealth, hath he swallowed, and hath vomited the same, Out of his belly, shall, GOD, drive it forth:
16 Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo ululu wa mphiri udzamupha.
The poison of adders, shall he suck, The tongue of the viper shall slay him;
17 Sadzasangalala ndi timitsinje, mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.
Let him not see in the channels the flowings of torrents of honey and milk.
18 Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya; sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.
In vain, he toiled, he shall not swallow, like wealth to be restored, in which he cannot exult!
19 Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo; iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.
For he hath oppressed—hath forsaken the poor, A house, hath he seized, which he cannot rebuild.
20 “Chifukwa choti umbombo wake sutha, sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.
Surely he hath known no peace in his inmost mind, —With his dearest thing, shall he not get away:
21 Palibe chatsala kuti iye adye; chuma chake sichidzachedwa kutha.
Nothing escaped his devouring greed, —For this cause, shall his prosperity not continue:
22 Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera; mavuto aakulu adzamugwera.
When his abundance is gone, he shall be in straits, All the power of distress, shall come upon him.
23 Akadya nʼkukhuta, Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto ngati mvula yosalekeza.
It shall be that, to fill his belly, he will thrust at him the glow of his anger, and rain [it] upon him for his punishment.
24 Ngakhale athawe mkondo wachitsulo, muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.
He shall flee from the armour of iron, —There shall pierce him, a bow of bronze!
25 Muviwo adzawutulutsira ku msana, songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake. Adzagwidwa ndi mantha aakulu;
He hath drawn it out, and it hath come forth out of his back, —yea the flashing arrow-head, out of his gall, There shall march on him—terrors:
26 mdima wandiweyani ukudikira chuma chake. Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.
Every misfortune, is laid up for his treasures, —There shall consume, a fire, not blown up, —it shall destroy what remaineth in his tent:
27 Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake; dziko lapansi lidzamuwukira.
The heavens shall reveal his iniquity, and, the earth, be rising up against him:
28 Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake, katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.
The increase of his house shall vanish, melting away in the day of his anger.
29 Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa, mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”
This, is the portion of the lawless man, from God, and the inheritance decreed him from the Mighty One.