< Yobu 20 >

1 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
Then answered Zophar the Naamathite, and said:
2 “Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe chifukwa ndasautsidwa kwambiri.
For this do my thoughts lead me to reply, And for this is my ardor within me.
3 Ndikumva kudzudzula kondinyoza, ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.
I have heard my shameful rebuke; And the spirit, from my understanding, answereth for me.
4 “Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale, kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,
Knowest thou not, that from the days of old, From the time when man was placed upon the earth,
5 kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha, chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.
The triumphing of the wicked hath been short, And the joy of the impious but for a moment?
6 Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba ndipo mutu wake uli nengʼaa,
Though his greatness mount up to the heavens, And his head reach to the clouds,
7 iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe; iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’
Yet shall he perish for ever, and be mingled with dust; They who saw him shall say, Where is he?
8 Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso, adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.
He shall flee away like a dream, and shall not be found; Yea, he shall disappear like a vision of the nigh.
9 Diso limene linamuona silidzamuonanso; sadzapezekanso pamalo pake.
The eye also which saw him shall see him no more, And his dwelling-place shall never more behold him.
10 Ana ake adzabwezera zonse zimene iyeyo analanda anthu osauka;
His sons shall seek the favor of the poor, And their hands shall give back his wealth.
11 Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake zidzagona naye limodzi mʼfumbi.
His bones are full of his youth, But they shall lie down with him in the dust.
12 “Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,
Though wickedness be sweet in his mouth, Though he hide it under his tongue,
13 ngakhale salola kuzilavula, ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,
Though he cherish it, and will not part with it, And keep it fast in his mouth,
14 koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake; chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.
Yet his meat shall be changed within him, And become to him the poison of asps.
15 Adzachisanza chuma chimene anachimeza; Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.
He hath glutted himself with riches, And he shall throw them up again; Yea, God shall cast them out of his body.
16 Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo ululu wa mphiri udzamupha.
He shall suck the poison of asps; The tongue of the viper shall destroy him.
17 Sadzasangalala ndi timitsinje, mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.
He shall never see the flowing streams, And the rivers of honey and milk.
18 Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya; sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.
The fruits of his toil he shall give back, and shall not enjoy them: It is substance to be restored, and he shall not rejoice therein.
19 Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo; iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.
Because he hath oppressed and abandoned the poor, And seized upon the house which he did not build;
20 “Chifukwa choti umbombo wake sutha, sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.
Because he knew no rest in his bosom, He shall not save that in which he delighteth.
21 Palibe chatsala kuti iye adye; chuma chake sichidzachedwa kutha.
Because nothing escaped his greediness, His prosperity shall not endure.
22 Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera; mavuto aakulu adzamugwera.
In the fulness of his abundance he shall be brought low; Every hand of the wretched shall come upon him.
23 Akadya nʼkukhuta, Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto ngati mvula yosalekeza.
He shall, indeed, have wherewith to fill himself: God shall send upon him the fury of his anger, And rain it down upon him for his food.
24 Ngakhale athawe mkondo wachitsulo, muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.
If he fleeth from the iron weapon, The bow of brass shall pierce him through.
25 Muviwo adzawutulutsira ku msana, songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake. Adzagwidwa ndi mantha aakulu;
He draweth the arrow, and it cometh forth from his body; Yea, the glittering steel cometh out of his gall. Terrors are upon him;
26 mdima wandiweyani ukudikira chuma chake. Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.
Calamity of every kind is treasured up for him. A fire not blown shall consume him; It shall consume whatever is left in his tent.
27 Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake; dziko lapansi lidzamuwukira.
The heavens shall reveal his iniquity, And the earth shall rise up against him.
28 Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake, katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.
The substance of his house shall disappear; It shall flow away in the day of His wrath.
29 Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa, mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”
Such is the portion of the wicked man from God, And the inheritance appointed for him by the Almighty.

< Yobu 20 >