< Yobu 20 >

1 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
Then Zophar the Naamathite answered,
2 “Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe chifukwa ndasautsidwa kwambiri.
"Therefore do my thoughts give answer to me, even by reason of my haste that is in me.
3 Ndikumva kudzudzula kondinyoza, ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.
I have heard the reproof which puts me to shame. The spirit of my understanding answers me.
4 “Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale, kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,
Do you not know this from old time, since humankind was placed on earth,
5 kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha, chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.
that the triumphing of the wicked is short, the joy of the godless but for a moment?
6 Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba ndipo mutu wake uli nengʼaa,
Though his height mount up to the heavens, and his head reach to the clouds,
7 iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe; iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’
yet he shall perish forever like his own dung. Those who have seen him shall say, 'Where is he?'
8 Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso, adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.
He shall fly away as a dream, and shall not be found. Yes, he shall be chased away like a vision of the night.
9 Diso limene linamuona silidzamuonanso; sadzapezekanso pamalo pake.
The eye which saw him shall see him no more, neither shall his place any more see him.
10 Ana ake adzabwezera zonse zimene iyeyo analanda anthu osauka;
His children shall seek the favor of the poor. His hands shall give back his wealth.
11 Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake zidzagona naye limodzi mʼfumbi.
His bones are full of his youth, but youth shall lie down with him in the dust.
12 “Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,
"Though wickedness is sweet in his mouth, though he hide it under his tongue,
13 ngakhale salola kuzilavula, ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,
though he spare it, and will not let it go, but keep it still within his mouth;
14 koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake; chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.
yet his food in his bowels is turned. It is cobra venom within him.
15 Adzachisanza chuma chimene anachimeza; Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.
He has swallowed down riches, and he shall vomit them up again. God will cast them out of his belly.
16 Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo ululu wa mphiri udzamupha.
He shall suck cobra venom. The viper's tongue shall kill him.
17 Sadzasangalala ndi timitsinje, mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.
He shall not look at the rivers, the flowing streams of honey and butter.
18 Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya; sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.
That for which he labored he shall restore, and shall not swallow it down. According to the substance that he has gotten, he shall not rejoice.
19 Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo; iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.
For he has oppressed and forsaken the poor. He has violently taken away a house, and he shall not build it up.
20 “Chifukwa choti umbombo wake sutha, sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.
"Because he knew no quietness within him, he shall not save anything of that in which he delights.
21 Palibe chatsala kuti iye adye; chuma chake sichidzachedwa kutha.
There was nothing left that he did not devour, therefore his prosperity shall not endure.
22 Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera; mavuto aakulu adzamugwera.
In the fullness of his sufficiency, distress shall overtake him. The hand of everyone who is in misery shall come on him.
23 Akadya nʼkukhuta, Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto ngati mvula yosalekeza.
When he is about to fill his belly, he will cast the fierceness of his wrath on him. It will rain on him while he is eating.
24 Ngakhale athawe mkondo wachitsulo, muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.
He shall flee from the iron weapon. The bronze arrow shall strike him through.
25 Muviwo adzawutulutsira ku msana, songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake. Adzagwidwa ndi mantha aakulu;
He draws it forth, and it comes out of his body. Yes, the glittering point comes out of his liver. Terrors are on him.
26 mdima wandiweyani ukudikira chuma chake. Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.
All darkness is laid up for his treasures. An unfanned fire shall devour him. It shall consume that which is left in his tent.
27 Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake; dziko lapansi lidzamuwukira.
The heavens shall reveal his iniquity. The earth shall rise up against him.
28 Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake, katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.
The increase of his house shall depart. They shall rush away in the day of his wrath.
29 Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa, mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”
This is the portion of a wicked man from God, the heritage appointed to him by God."

< Yobu 20 >