< Yobu 20 >
1 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
And Zophar the Naamathite answers and says:
2 “Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe chifukwa ndasautsidwa kwambiri.
“Therefore my thoughts cause me to answer, And because of my sensations in me.
3 Ndikumva kudzudzula kondinyoza, ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.
I hear the discipline of my shame, And the spirit of my understanding causes me to answer:
4 “Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale, kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,
Have you known this from antiquity? Since the placing of man on earth?
5 kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha, chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.
That the singing of the wicked [is] short, And the joy of the profane for a moment,
6 Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba ndipo mutu wake uli nengʼaa,
Though his excellence goes up to the heavens, He strikes his head against a cloud—
7 iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe; iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’
He perishes as his own dung forever, His beholders say, Where [is] he?
8 Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso, adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.
He flees as a dream, and they do not find him, And he is driven away as a vision of the night,
9 Diso limene linamuona silidzamuonanso; sadzapezekanso pamalo pake.
The eye has not seen him, and does not add. And his place does not behold him again.
10 Ana ake adzabwezera zonse zimene iyeyo analanda anthu osauka;
His sons oppress the poor, And his hands give back his wealth.
11 Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake zidzagona naye limodzi mʼfumbi.
His bones have been full of his youth, and it lies down with him on the dust.
12 “Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,
Though he sweetens evil in his mouth, hides it under his tongue,
13 ngakhale salola kuzilavula, ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,
has pity on it, and does not forsake it, and keeps it back in the midst of his palate,
14 koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake; chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.
his food is turned in his bowels, the bitterness of cobras [is] in his heart.
15 Adzachisanza chuma chimene anachimeza; Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.
He has swallowed wealth, and vomits it. God drives it out from his belly.
16 Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo ululu wa mphiri udzamupha.
He sucks [the] gall of cobras, the tongue of a viper slays him.
17 Sadzasangalala ndi timitsinje, mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.
He does not look on streams, Flowing of brooks of honey and butter.
18 Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya; sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.
He is giving back [what] he labored for, and does not consume [it]; As a bulwark [is] his exchange, and he does not exult.
19 Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo; iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.
For he oppressed—he forsook the poor, He has taken a house away violently, And he does not build it.
20 “Chifukwa choti umbombo wake sutha, sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.
For he has not known ease in his belly. With his desirable thing he does not deliver himself.
21 Palibe chatsala kuti iye adye; chuma chake sichidzachedwa kutha.
There is not a remnant to his food, Therefore his good does not stay.
22 Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera; mavuto aakulu adzamugwera.
In the fullness of his sufficiency he is constricted. Every perverse hand meets him.
23 Akadya nʼkukhuta, Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto ngati mvula yosalekeza.
It comes to pass, at the filling of his belly, He sends forth against him The fierceness of His anger, Indeed, He rains on him in his eating.
24 Ngakhale athawe mkondo wachitsulo, muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.
He flees from an iron weapon, A bow of bronze passes through him.
25 Muviwo adzawutulutsira ku msana, songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake. Adzagwidwa ndi mantha aakulu;
One has drawn, And it comes out from the body, And a glittering weapon proceeds from his gall. Terrors [are] on him.
26 mdima wandiweyani ukudikira chuma chake. Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.
All darkness is hid for his treasures, A fire not blown consumes him, The remnant is broken in his tent.
27 Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake; dziko lapansi lidzamuwukira.
The heavens reveal his iniquity, And earth is raising itself against him.
28 Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake, katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.
The increase of his house is removed, Poured forth in a day of His anger.
29 Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa, mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”
This [is] the portion of a wicked man from God. And an inheritance appointed him by God.”