< Yobu 20 >
1 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
Then Zophar the Naamathite answered by saying:
2 “Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe chifukwa ndasautsidwa kwambiri.
In response, various thoughts succeed one another in me, and my mind moves quickly through different ideas.
3 Ndikumva kudzudzula kondinyoza, ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.
The teaching you use to admonish me, I will hear, and the spirit of my understanding will respond for me.
4 “Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale, kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,
This, I know, is from the beginning, from the time that man was set over the earth:
5 kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha, chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.
that the praise of the impious shall be short, and the joy of the hypocrite lasts only a moment.
6 Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba ndipo mutu wake uli nengʼaa,
If his pride ascends even towards the heavens, and his head touches the clouds,
7 iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe; iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’
in the end, he will be destroyed like a trash heap, and those who had seen him will say: “Where is he?”
8 Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso, adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.
Like a dream that flies away, he will not be found; he will pass away like a nightmare.
9 Diso limene linamuona silidzamuonanso; sadzapezekanso pamalo pake.
The eyes that had seen him, will not see him; no longer will his own place admire him.
10 Ana ake adzabwezera zonse zimene iyeyo analanda anthu osauka;
His sons will be worn away by poverty, and his own hands will deliver his grief to him.
11 Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake zidzagona naye limodzi mʼfumbi.
His bones will be filled with the vices of his youth, and they will sleep with him in the dust.
12 “Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,
For, when evil will be sweet in his mouth, he will hide it under his tongue.
13 ngakhale salola kuzilavula, ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,
He will permit it, and not abandon it, and he will conceal it in his throat.
14 koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake; chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.
His bread in his belly will be turned into the venom of snakes within him.
15 Adzachisanza chuma chimene anachimeza; Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.
The riches that he devours, he will vomit up, and from his stomach God will draw them out.
16 Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo ululu wa mphiri udzamupha.
He will suck the head of snakes, and the tongue of the viper will kill him.
17 Sadzasangalala ndi timitsinje, mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.
(May he never see the streams of the river, the torrents of honey and butter.)
18 Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya; sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.
He will be repaid for all he has done, yet he will not be consumed; according to the multitude of his schemes, so also will he suffer.
19 Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo; iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.
For, having broken in, he stripped the poor. He has quickly stolen away a house he did not build.
20 “Chifukwa choti umbombo wake sutha, sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.
And yet his stomach will not be satisfied, and when he has the things he desires, he will not be able to possess them.
21 Palibe chatsala kuti iye adye; chuma chake sichidzachedwa kutha.
Nothing remained of his portion, and, because of this, nothing will continue of his kind.
22 Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera; mavuto aakulu adzamugwera.
When he will be satisfied, he will be constrained; he will seethe, and all anguish will fall upon him.
23 Akadya nʼkukhuta, Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto ngati mvula yosalekeza.
May his stomach be filled, so that God may send forth the fury of his wrath to him and may rain down his battle upon him.
24 Ngakhale athawe mkondo wachitsulo, muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.
He will flee from weapons of iron, and he will fall in an arc of brass,
25 Muviwo adzawutulutsira ku msana, songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake. Adzagwidwa ndi mantha aakulu;
which had been drawn and had issued forth from its sheath, glittering in its bitterness: the horrible ones will go forth and approach over him.
26 mdima wandiweyani ukudikira chuma chake. Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.
All darkness has been hidden in his secrecy. A fire that has not been set will devour him; he will be thrown down and forsaken in his tabernacle.
27 Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake; dziko lapansi lidzamuwukira.
The heavens will reveal his sinfulness, and the earth will rise up against him.
28 Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake, katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.
The offspring of his house will be exposed; he will be pulled down in the day of God’s wrath.
29 Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa, mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”
This is the portion of a wicked man from God, and the inheritance of his words from the Lord.