< Yobu 2 >
1 Tsiku linanso pamene ana a Mulungu anabwera kudzadzionetsa pamaso pa Yehova, nayenso Satana anabwera nawo limodzi kudzadzionetsa pamaso pa Yehova.
Ponovno je bil dan, ko so prišli Božji sinovi, da se predstavijo pred Gospodom in tudi Satan je prišel med njimi, da se predstavi pred Gospodom.
2 Ndipo Yehova anati kwa Satana, “Kodi iwe ukuchokera kuti?” Satana anayankha Yehova kuti, “Ndakhala ndikungoyendayenda ndi kumangozungulira mʼdzikoli.”
Gospod je rekel Satanu: »Od kod prihajaš?« Satan je Gospodu odgovoril in rekel: »Od potikanja sem ter tja po zemlji in od hoje gor in dol po njej.«
3 Pamenepo Yehova anati kwa Satana, “Kodi unalingalirapo za mtumiki wanga Yobu? Palibe wina pa dziko lapansi wofanana naye; ndi munthu wosalakwa ndi wolungama mtima, munthu amene amaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa. Ndipo iye akanalibe wangwiro, ngakhale iwe unandiwumiriza kuti ndikulole kuti umuvutitse popanda chifukwa.”
Gospod je rekel Satanu: »Si preudaril [o] mojem služabniku Jobu, da tam ni nikogar podobnega njemu na zemlji? Popoln in iskren človek je, nekdo, ki se boji Boga in se ogiblje zla. Še vedno se trdno drži svoje neokrnjenosti, čeprav me spodbujaš zoper njega, da bi ga uničil brez razloga.«
4 Satana anayankha kuti, “Iye ayesedwe mʼthupi mwake. Munthu angathe kupereka zonse ali nazo malingana iyeyo ali ndi moyo.
Satan je Gospodu odgovoril in rekel: »Kožo za kožo, da, vse, kar človek ima, bo dal za svoje življenje.
5 Koma tatambasulani dzanja lanu ndi kuwononga thupi lake, ndipo iyeyo adzakutukwanani ndithu pamaso panu.”
Toda iztegni sedaj svojo roko in se dotakni njegove kosti in njegovega mesa in preklel te bo v tvoj obraz.«
6 Yehova anati kwa Satana, “Chabwino, iye ali mʼmanja mwako; koma moyo wake usawuchotse.”
Gospod je rekel Satanu: »Glej, on je v tvoji roki, toda ohrani njegovo življenje.«
7 Choncho Satana anachoka pamaso pa Yehova napita kukazunza Yobu ndi zilonda zaululu pa thupi lake lonse.
Tako je Satan odšel izpred Gospodove prisotnosti in Joba udaril s hudimi tvori od podplata njegovega stopala do njegovega temena.
8 Pamenepo Yobu anatenga phale ndi kumadzikanda nalo atakhala pa dzala la phulusa.
Ta si je vzel črepinjo, se strgal z njo in se usedel med pepel.
9 Mkazi wake anati kwa iye, “Kodi ukuwumirirabe kukhala wangwiro? Tukwana Mulungu kuti ufe!”
Potem mu je njegova žena rekla: »Mar še vedno ohranjaš svojo neokrnjenost? Prekolni Boga in umri.«
10 Yobu anayankha kuti, “Ukuyankhula ngati mkazi wopusa. Kodi tidzalandira zokoma zokhazokha kwa Mulungu, osalandiranso zowawa?” Mu zonsezi, Yobu sanachimwe pa zimene anayankhula.
Toda rekel ji je: »Govoriš kot govori ena izmed nespametnih žensk. Kaj? Dobro smo sprejeli iz Božje roke, pa ne bi sprejeli hudega?« V vsem tem Job s svojimi ustnicami ni grešil.
11 Abwenzi atatu a Yobu, Elifazi wa ku Temani, Bilidadi wa ku Suki ndi Zofari wa ku Naama, atamva za tsoka lonse limene linamugwera iye, ananyamuka ku nyumba zawo nakumana malo amodzi mopangana kuti apite ndi kukamupepesa Yobu ndi kumutonthoza.
Torej ko so Jobovi trije prijatelji slišali o vsem tem zlu, ki je prišlo nadenj, so prišli, vsak iz svojega lastnega kraja: Elifáz Temánec, Bildád Suhéjec in Cofár Naámčan, kajti skupaj so se dogovorili, da pridejo in da žalujejo z njim in da ga tolažijo.
12 Atamuona Yobuyo, iwo ali chapatalipo, sanathe kumuzindikira. Choncho anayamba kulira mokweza mawu ndipo anangʼamba mikanjo yawo ndi kuwaza fumbi pa mitu yawo.
Ko pa so od daleč povzdignili svoje oči in ga niso spoznali, so povzdignili svoj glas ter zajokali. Vsak izmed njih je pretrgal svoje ogrinjalo in proti nebu so potresli prah na svoje glave.
13 Tsono anakhala naye pamodzi pansi kwa masiku asanu ndi awiri, usana ndi usiku omwe. Palibe ndi mmodzi yemwe anayankhula naye, chifukwa anazindikira kuti Yobu amavutika kwambiri.
Tako so sedeli z njim na tleh sedem dni in sedem noči in nihče mu ni spregovoril niti besede, kajti videli so, da je bila njegova žalost zelo velika.