< Yobu 2 >

1 Tsiku linanso pamene ana a Mulungu anabwera kudzadzionetsa pamaso pa Yehova, nayenso Satana anabwera nawo limodzi kudzadzionetsa pamaso pa Yehova.
Le jour où les fils de Dieu vinrent se présenter devant Yahvé, Satan vint aussi parmi eux pour se présenter devant Yahvé.
2 Ndipo Yehova anati kwa Satana, “Kodi iwe ukuchokera kuti?” Satana anayankha Yehova kuti, “Ndakhala ndikungoyendayenda ndi kumangozungulira mʼdzikoli.”
Yahvé dit à Satan: « D'où viens-tu? » Satan répondit à Yahvé: « D'aller et de venir sur la terre, et d'y marcher de haut en bas. »
3 Pamenepo Yehova anati kwa Satana, “Kodi unalingalirapo za mtumiki wanga Yobu? Palibe wina pa dziko lapansi wofanana naye; ndi munthu wosalakwa ndi wolungama mtima, munthu amene amaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa. Ndipo iye akanalibe wangwiro, ngakhale iwe unandiwumiriza kuti ndikulole kuti umuvutitse popanda chifukwa.”
Yahvé dit à Satan: « As-tu considéré mon serviteur Job? Car il n'y a personne comme lui sur la terre, un homme irréprochable et droit, qui craint Dieu et se détourne du mal. Il a gardé son intégrité, bien que tu m'aies incité contre lui, pour le ruiner sans raison. »
4 Satana anayankha kuti, “Iye ayesedwe mʼthupi mwake. Munthu angathe kupereka zonse ali nazo malingana iyeyo ali ndi moyo.
Satan répondit à Yahvé et dit: « Peau pour peau. Oui, tout ce que possède un homme, il le donnera pour sa vie.
5 Koma tatambasulani dzanja lanu ndi kuwononga thupi lake, ndipo iyeyo adzakutukwanani ndithu pamaso panu.”
Mais étends maintenant ta main, touche ses os et sa chair, et il te reniera en face. »
6 Yehova anati kwa Satana, “Chabwino, iye ali mʼmanja mwako; koma moyo wake usawuchotse.”
Yahvé dit à Satan: « Voici, il est entre tes mains. Seulement, épargne sa vie. »
7 Choncho Satana anachoka pamaso pa Yehova napita kukazunza Yobu ndi zilonda zaululu pa thupi lake lonse.
Satan sortit de la présence de Yahvé et frappa Job de plaies douloureuses, depuis la plante du pied jusqu'à la tête.
8 Pamenepo Yobu anatenga phale ndi kumadzikanda nalo atakhala pa dzala la phulusa.
Il se prit un tesson pour se gratter et s'assit au milieu des cendres.
9 Mkazi wake anati kwa iye, “Kodi ukuwumirirabe kukhala wangwiro? Tukwana Mulungu kuti ufe!”
Alors sa femme lui dit: « Gardes-tu encore ton intégrité? Renonce à Dieu, et meurs. »
10 Yobu anayankha kuti, “Ukuyankhula ngati mkazi wopusa. Kodi tidzalandira zokoma zokhazokha kwa Mulungu, osalandiranso zowawa?” Mu zonsezi, Yobu sanachimwe pa zimene anayankhula.
Mais il lui dit: « Tu parles comme parlerait une femme insensée. Quoi? Recevrons-nous du bien de la main de Dieu, et ne recevrons-nous pas du mal? » Dans tout cela, Job n'a pas péché des lèvres.
11 Abwenzi atatu a Yobu, Elifazi wa ku Temani, Bilidadi wa ku Suki ndi Zofari wa ku Naama, atamva za tsoka lonse limene linamugwera iye, ananyamuka ku nyumba zawo nakumana malo amodzi mopangana kuti apite ndi kukamupepesa Yobu ndi kumutonthoza.
Et lorsque les trois amis de Job apprirent tout ce malheur qui l'atteignait, ils vinrent chacun de leur côté: Éliphaz, le Témanite, Bildad, le Shuhite, et Zophar, le Naamathite; et ils se donnèrent rendez-vous pour venir compatir avec lui et le consoler.
12 Atamuona Yobuyo, iwo ali chapatalipo, sanathe kumuzindikira. Choncho anayamba kulira mokweza mawu ndipo anangʼamba mikanjo yawo ndi kuwaza fumbi pa mitu yawo.
Lorsqu'ils levèrent les yeux de loin et ne le reconnurent pas, ils élevèrent la voix et pleurèrent; ils déchirèrent chacun leur robe et répandirent de la poussière sur leur tête vers le ciel.
13 Tsono anakhala naye pamodzi pansi kwa masiku asanu ndi awiri, usana ndi usiku omwe. Palibe ndi mmodzi yemwe anayankhula naye, chifukwa anazindikira kuti Yobu amavutika kwambiri.
Ils s'assirent avec lui à terre, sept jours et sept nuits, et personne ne lui adressa la parole, car ils voyaient que son chagrin était très grand.

< Yobu 2 >