< Yobu 2 >
1 Tsiku linanso pamene ana a Mulungu anabwera kudzadzionetsa pamaso pa Yehova, nayenso Satana anabwera nawo limodzi kudzadzionetsa pamaso pa Yehova.
And it happened [again] on a certain day, when the sons of God came to present themselves before the Lord, that the Accuser also came in the midst of them to present himself before the Lord.
2 Ndipo Yehova anati kwa Satana, “Kodi iwe ukuchokera kuti?” Satana anayankha Yehova kuti, “Ndakhala ndikungoyendayenda ndi kumangozungulira mʼdzikoli.”
Then said the Lord unto the Accuser, Whence comest thou now? And the Accuser answered the Lord, and said, From roaming over the earth, and from wandering through it.
3 Pamenepo Yehova anati kwa Satana, “Kodi unalingalirapo za mtumiki wanga Yobu? Palibe wina pa dziko lapansi wofanana naye; ndi munthu wosalakwa ndi wolungama mtima, munthu amene amaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa. Ndipo iye akanalibe wangwiro, ngakhale iwe unandiwumiriza kuti ndikulole kuti umuvutitse popanda chifukwa.”
Then said the Lord unto the Accuser, Hast thou directed thy attention toward my servant Job: for there is none like him on the earth, a man perfect and upright, who feareth God, and escheweth evil? and he is still holding fast to his integrity, and thou hast incited me against him, to destroy him without cause.
4 Satana anayankha kuti, “Iye ayesedwe mʼthupi mwake. Munthu angathe kupereka zonse ali nazo malingana iyeyo ali ndi moyo.
Then answered the Accuser the Lord, and said, Skin for skin: yea, all that a man hath will he give in behalf of his life.
5 Koma tatambasulani dzanja lanu ndi kuwononga thupi lake, ndipo iyeyo adzakutukwanani ndithu pamaso panu.”
But stretch only forth thy hand, and touch his bone and his flesh, and [see] whether he will not renounce thee to thy face.
6 Yehova anati kwa Satana, “Chabwino, iye ali mʼmanja mwako; koma moyo wake usawuchotse.”
Then said the Lord unto the Accuser, Behold, he is in thy hand: only take care of his life.
7 Choncho Satana anachoka pamaso pa Yehova napita kukazunza Yobu ndi zilonda zaululu pa thupi lake lonse.
Thereupon went the Accuser forth from the presence of the Lord, and he smote Job with a sore inflammation, from the sole of his foot unto the crown of his head.
8 Pamenepo Yobu anatenga phale ndi kumadzikanda nalo atakhala pa dzala la phulusa.
And [Job] took himself a potsherd to scrape himself there with, while he was sitting down among the ashes.
9 Mkazi wake anati kwa iye, “Kodi ukuwumirirabe kukhala wangwiro? Tukwana Mulungu kuti ufe!”
Then said his wife unto him, Art thou still holding fast to thy integrity? renounce God, and die.
10 Yobu anayankha kuti, “Ukuyankhula ngati mkazi wopusa. Kodi tidzalandira zokoma zokhazokha kwa Mulungu, osalandiranso zowawa?” Mu zonsezi, Yobu sanachimwe pa zimene anayankhula.
But he said unto her, Thou speakest as one of the worthless women would speak. What? should we accept the good alone, from God, and the evil we should not accept? With all this did Job not sin with his lips.
11 Abwenzi atatu a Yobu, Elifazi wa ku Temani, Bilidadi wa ku Suki ndi Zofari wa ku Naama, atamva za tsoka lonse limene linamugwera iye, ananyamuka ku nyumba zawo nakumana malo amodzi mopangana kuti apite ndi kukamupepesa Yobu ndi kumutonthoza.
When now the three friends of Job had heard of all this evil that was come over him, they came every one from his own place, Eliphaz the Themanite, and Bildad the Shuchite, and Zophar the Na'amthite; and they met together to come to condole with him and to comfort him.
12 Atamuona Yobuyo, iwo ali chapatalipo, sanathe kumuzindikira. Choncho anayamba kulira mokweza mawu ndipo anangʼamba mikanjo yawo ndi kuwaza fumbi pa mitu yawo.
And when they lifted up their eyes afar off, and they recognised him not, they lifted up their voice, and wept; and they rent every one his robe, and strewed dust upon their heads toward heaven.
13 Tsono anakhala naye pamodzi pansi kwa masiku asanu ndi awiri, usana ndi usiku omwe. Palibe ndi mmodzi yemwe anayankhula naye, chifukwa anazindikira kuti Yobu amavutika kwambiri.
They likewise sat down with him on the ground seven days and seven nights; but no one spoke a word unto him; for they saw that his pain was very great.