< Yobu 2 >
1 Tsiku linanso pamene ana a Mulungu anabwera kudzadzionetsa pamaso pa Yehova, nayenso Satana anabwera nawo limodzi kudzadzionetsa pamaso pa Yehova.
Again it came to pass on the day when the sons of God came to present themselves before Jehovah, that Satan came also among them to present himself before Jehovah.
2 Ndipo Yehova anati kwa Satana, “Kodi iwe ukuchokera kuti?” Satana anayankha Yehova kuti, “Ndakhala ndikungoyendayenda ndi kumangozungulira mʼdzikoli.”
And Jehovah said to Satan, From where did thou come? And Satan answered Jehovah, and said, From going to and fro on the earth, and from walking up and down on it.
3 Pamenepo Yehova anati kwa Satana, “Kodi unalingalirapo za mtumiki wanga Yobu? Palibe wina pa dziko lapansi wofanana naye; ndi munthu wosalakwa ndi wolungama mtima, munthu amene amaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa. Ndipo iye akanalibe wangwiro, ngakhale iwe unandiwumiriza kuti ndikulole kuti umuvutitse popanda chifukwa.”
And Jehovah said to Satan, Have thou considered my servant Job? For there is none like him in the earth, a perfect and an upright man, one who fears God, and turns away from evil. And he still holds fast his integrity, although thou moved me against him, to destroy him without cause.
4 Satana anayankha kuti, “Iye ayesedwe mʼthupi mwake. Munthu angathe kupereka zonse ali nazo malingana iyeyo ali ndi moyo.
And Satan answered Jehovah, and said, Skin for skin, yea, all that a man has he will give for his life.
5 Koma tatambasulani dzanja lanu ndi kuwononga thupi lake, ndipo iyeyo adzakutukwanani ndithu pamaso panu.”
But put forth thy hand now, and touch his bone and his flesh, and he will renounce thee to thy face.
6 Yehova anati kwa Satana, “Chabwino, iye ali mʼmanja mwako; koma moyo wake usawuchotse.”
And Jehovah said to Satan, Behold, he is in thy hand, only spare his life.
7 Choncho Satana anachoka pamaso pa Yehova napita kukazunza Yobu ndi zilonda zaululu pa thupi lake lonse.
So Satan went forth from the presence of Jehovah, and smote Job with severe boils from the sole of his foot to his crown.
8 Pamenepo Yobu anatenga phale ndi kumadzikanda nalo atakhala pa dzala la phulusa.
And he took a potsherd for him to scrape himself with it, and he sat among the ashes.
9 Mkazi wake anati kwa iye, “Kodi ukuwumirirabe kukhala wangwiro? Tukwana Mulungu kuti ufe!”
Then his wife said to him, Do thou still hold fast thine integrity? Renounce God, and die.
10 Yobu anayankha kuti, “Ukuyankhula ngati mkazi wopusa. Kodi tidzalandira zokoma zokhazokha kwa Mulungu, osalandiranso zowawa?” Mu zonsezi, Yobu sanachimwe pa zimene anayankhula.
But he said to her, Thou speak as one of the foolish women speaks. What? Shall we receive good at the hand of God, and shall we not receive evil? In all this Job did not sin with his lips.
11 Abwenzi atatu a Yobu, Elifazi wa ku Temani, Bilidadi wa ku Suki ndi Zofari wa ku Naama, atamva za tsoka lonse limene linamugwera iye, ananyamuka ku nyumba zawo nakumana malo amodzi mopangana kuti apite ndi kukamupepesa Yobu ndi kumutonthoza.
Now when Job's three friends heard of all this evil that came upon him, they came each one from his own place-Eliphaz the Temanite, and Bildad the Shuhite, and Zophar the Naamathite-and they made an appointment together to come to bemoan him and to comfort him.
12 Atamuona Yobuyo, iwo ali chapatalipo, sanathe kumuzindikira. Choncho anayamba kulira mokweza mawu ndipo anangʼamba mikanjo yawo ndi kuwaza fumbi pa mitu yawo.
And when they lifted up their eyes afar off, and did not recognize him, they lifted up their voice, and wept. And each one tore his robe, and sprinkled dust upon their heads toward heaven.
13 Tsono anakhala naye pamodzi pansi kwa masiku asanu ndi awiri, usana ndi usiku omwe. Palibe ndi mmodzi yemwe anayankhula naye, chifukwa anazindikira kuti Yobu amavutika kwambiri.
So they sat down with him upon the ground seven days and seven nights. And none spoke a word to him, for they saw that his grief was very great.