< Yobu 2 >

1 Tsiku linanso pamene ana a Mulungu anabwera kudzadzionetsa pamaso pa Yehova, nayenso Satana anabwera nawo limodzi kudzadzionetsa pamaso pa Yehova.
Og det skete en Dag, der Guds Børn kom for at fremstille sig for Herren, da kom ogsaa Satan midt iblandt dem for at fremstille sig for Herren.
2 Ndipo Yehova anati kwa Satana, “Kodi iwe ukuchokera kuti?” Satana anayankha Yehova kuti, “Ndakhala ndikungoyendayenda ndi kumangozungulira mʼdzikoli.”
Da sagde Herren til Satan: Hvorfra kommer du? og Satan svarede Herren og sagde: Fra at gaa omkring i Landet og vandre om derudi.
3 Pamenepo Yehova anati kwa Satana, “Kodi unalingalirapo za mtumiki wanga Yobu? Palibe wina pa dziko lapansi wofanana naye; ndi munthu wosalakwa ndi wolungama mtima, munthu amene amaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa. Ndipo iye akanalibe wangwiro, ngakhale iwe unandiwumiriza kuti ndikulole kuti umuvutitse popanda chifukwa.”
Og Herren sagde til Satan: Har du givet Agt paa min Tjener Job? thi der er ingen som han i Landet, en oprigtig og retskaffen Mand, som frygter Gud og viger fra det onde, og han holder endnu fast ved sin Retsindighed; men du har tilskyndet mig imod ham at ødelægge ham uden Aarsag.
4 Satana anayankha kuti, “Iye ayesedwe mʼthupi mwake. Munthu angathe kupereka zonse ali nazo malingana iyeyo ali ndi moyo.
Da svarede Satan Herren og sagde: Hud for Hud, ja alt det, en Mand har, giver han for sit Liv.
5 Koma tatambasulani dzanja lanu ndi kuwononga thupi lake, ndipo iyeyo adzakutukwanani ndithu pamaso panu.”
Dog udræk nu din Haand og rør ved hans Ben og hans Kød; hvad gælder det, om han ikke skal fornægte dig lige for dit Ansigt?
6 Yehova anati kwa Satana, “Chabwino, iye ali mʼmanja mwako; koma moyo wake usawuchotse.”
Og Herren sagde til Satan: Se, han være i din Haand; dog var hans Liv!
7 Choncho Satana anachoka pamaso pa Yehova napita kukazunza Yobu ndi zilonda zaululu pa thupi lake lonse.
Da for Satan ud fra Herrens Ansigt og slog Job med onde Bylder fra hans Fodsaal og indtil hans Isse.
8 Pamenepo Yobu anatenga phale ndi kumadzikanda nalo atakhala pa dzala la phulusa.
Og han tog sig et Potteskaar til at skrabe sig med, og han sad midt i Asken.
9 Mkazi wake anati kwa iye, “Kodi ukuwumirirabe kukhala wangwiro? Tukwana Mulungu kuti ufe!”
Og hans Hustru sagde til ham: Holder du endnu fast ved din Retsindighed? velsign Gud og dø!
10 Yobu anayankha kuti, “Ukuyankhula ngati mkazi wopusa. Kodi tidzalandira zokoma zokhazokha kwa Mulungu, osalandiranso zowawa?” Mu zonsezi, Yobu sanachimwe pa zimene anayankhula.
Men han sagde til hende: Du taler, ligesom en af de daarlige Kvinder taler; skulde vi alene tage imod det gode af Gud og ikke tage imod det onde? I alt dette syndede Job ikke med sine Læber.
11 Abwenzi atatu a Yobu, Elifazi wa ku Temani, Bilidadi wa ku Suki ndi Zofari wa ku Naama, atamva za tsoka lonse limene linamugwera iye, ananyamuka ku nyumba zawo nakumana malo amodzi mopangana kuti apite ndi kukamupepesa Yobu ndi kumutonthoza.
Og der Jobs tre Venner hørte al den Ulykke, som var kommen over ham, da kom de, hver fra sit Sted: Themaniten Elifas og Sukiten Bildad og Naamathiten Zofar, og de forenede sig med hverandre for at komme at vise ham Medynk og trøste ham.
12 Atamuona Yobuyo, iwo ali chapatalipo, sanathe kumuzindikira. Choncho anayamba kulira mokweza mawu ndipo anangʼamba mikanjo yawo ndi kuwaza fumbi pa mitu yawo.
Men der de opløftede deres Øjne langtfra, da kendte de ham ikke, og de opløftede deres Røst og græd, og de sønderrev hver sin Kappe, og de kastede Støv paa deres Hoveder op imod Himmelen.
13 Tsono anakhala naye pamodzi pansi kwa masiku asanu ndi awiri, usana ndi usiku omwe. Palibe ndi mmodzi yemwe anayankhula naye, chifukwa anazindikira kuti Yobu amavutika kwambiri.
Og de sade hos ham paa Jorden syv Dage og syv Nætter, og ingen talte et Ord til ham; thi de saa, at Pinen var saare stor.

< Yobu 2 >