< Yobu 2 >

1 Tsiku linanso pamene ana a Mulungu anabwera kudzadzionetsa pamaso pa Yehova, nayenso Satana anabwera nawo limodzi kudzadzionetsa pamaso pa Yehova.
I stalo se opět jednoho dne, že když přišli synové Boží, aby se postavili před Hospodinem, přišel také i Satan mezi ně, aby se postavil před Hospodinem.
2 Ndipo Yehova anati kwa Satana, “Kodi iwe ukuchokera kuti?” Satana anayankha Yehova kuti, “Ndakhala ndikungoyendayenda ndi kumangozungulira mʼdzikoli.”
Tedy řekl Hospodin Satanovi: Odkud jdeš? I odpověděl Satan Hospodinu, řka: Procházel jsem zemi, a obcházel jsem ji.
3 Pamenepo Yehova anati kwa Satana, “Kodi unalingalirapo za mtumiki wanga Yobu? Palibe wina pa dziko lapansi wofanana naye; ndi munthu wosalakwa ndi wolungama mtima, munthu amene amaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa. Ndipo iye akanalibe wangwiro, ngakhale iwe unandiwumiriza kuti ndikulole kuti umuvutitse popanda chifukwa.”
I řekl Hospodin Satanovi: Spatřil-lis služebníka mého Joba, že není jemu rovného na zemi, že jest muž sprostný a upřímý, bojící se Boha, a varující se zlého, a že po dnes trvá v upřímnosti své, ačkoli jsi ty mne popudil proti němu, abych jej hubil bez příčiny.
4 Satana anayankha kuti, “Iye ayesedwe mʼthupi mwake. Munthu angathe kupereka zonse ali nazo malingana iyeyo ali ndi moyo.
A odpovídaje Satan Hospodinu, řekl: Kůži za kůži, a všecko, což má člověk, dá za sebe samého.
5 Koma tatambasulani dzanja lanu ndi kuwononga thupi lake, ndipo iyeyo adzakutukwanani ndithu pamaso panu.”
Ale vztáhni nyní ruku svou, a dotkni se kostí jeho, a masa jeho, nebude-liť v oči zlořečiti tobě.
6 Yehova anati kwa Satana, “Chabwino, iye ali mʼmanja mwako; koma moyo wake usawuchotse.”
Tedy řekl Hospodin Satanovi: Aj, v moci tvé buď, a však zachovej ho při životu.
7 Choncho Satana anachoka pamaso pa Yehova napita kukazunza Yobu ndi zilonda zaululu pa thupi lake lonse.
Protož vyšed Satan od tváři Hospodinovy, ranil Joba nežitem nejhorším, od zpodku nohy jeho až do vrchu hlavy jeho,
8 Pamenepo Yobu anatenga phale ndi kumadzikanda nalo atakhala pa dzala la phulusa.
Tak že vzal střepinu, aby se jí drbal, usadiv se v popele.
9 Mkazi wake anati kwa iye, “Kodi ukuwumirirabe kukhala wangwiro? Tukwana Mulungu kuti ufe!”
I řekla jemu žena jeho: Ještě vždy trváš v své upřímnosti? Zlořeč Bohu a umři.
10 Yobu anayankha kuti, “Ukuyankhula ngati mkazi wopusa. Kodi tidzalandira zokoma zokhazokha kwa Mulungu, osalandiranso zowawa?” Mu zonsezi, Yobu sanachimwe pa zimene anayankhula.
Jížto řekl: Mluvíš, jako jedna z bláznivých mluvívá. Dobré-liž jen věci bráti budeme od Boha, zlých pak nebudeme přijímati? V tom ve všem nezhřešil Job rty svými.
11 Abwenzi atatu a Yobu, Elifazi wa ku Temani, Bilidadi wa ku Suki ndi Zofari wa ku Naama, atamva za tsoka lonse limene linamugwera iye, ananyamuka ku nyumba zawo nakumana malo amodzi mopangana kuti apite ndi kukamupepesa Yobu ndi kumutonthoza.
Když pak uslyšeli tři přátelé Jobovi o všem tom zlém, kteréž přišlo na něj, přišli jeden každý z místa svého: Elifaz Temanský, a Bildad Suchský a Zofar Naamatský, na tom zůstavše spolu, aby přijdouce k němu, politovali ho a těšili jej.
12 Atamuona Yobuyo, iwo ali chapatalipo, sanathe kumuzindikira. Choncho anayamba kulira mokweza mawu ndipo anangʼamba mikanjo yawo ndi kuwaza fumbi pa mitu yawo.
Kteříž pozdvihše očí svých zdaleka, nepoznali ho. Potom pozdvihše hlasu svého, plakali, a roztrhše jeden každý roucho své, házeli prachem nad hlavy své zhůru.
13 Tsono anakhala naye pamodzi pansi kwa masiku asanu ndi awiri, usana ndi usiku omwe. Palibe ndi mmodzi yemwe anayankhula naye, chifukwa anazindikira kuti Yobu amavutika kwambiri.
A seděli s ním na zemi sedm dní a sedm nocí, a žádný k němu nepromluvil slova; nebo viděli, že se velmi rozmohla bolest jeho.

< Yobu 2 >