< Yobu 19 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Na Hiob buae se,
2 “Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti, ndi kundilasa ndi mawu anuwo?
“Mobɛhyɛ me ɔyaw na mode nsɛm abubu me akosi da bɛn?
3 Inuyo mwandinyoza kwambiri; mwanditsutsa mopanda manyazi.
Mpɛn du ni a moasopa me; mo ani nwu sɛ motow hyɛ me so.
4 Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera, cholakwachotu nʼchanga.
Sɛ ɛyɛ nokware sɛ mafom ɔkwan a, me mfomso yɛ me nko ara asɛm.
5 Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga, ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,
Sɛ ampa sɛ mobɛma mo ho so asen me na mode mʼanimguase ayɛ adanse atia me a,
6 pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira ndipo wandizinga ukonde wake.
ɛno de munhu sɛ Onyankopɔn ayɛ me bɔne na ɔde ne tan atwa me ho ahyia.
7 “Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha; ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.
“Ɛwɔ mu, misu se, ‘Wɔafom me’ de, nanso obiara mmua me; meteɛ mu pɛ mmoa, nanso atɛntrenee biara nni hɔ.
8 Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa; waphimba njira zanga ndi mdima.
Wasiw me kwan enti mintumi nsen; ɔde sum aduru mʼakwan so.
9 Iye wandilanda ulemu wanga ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.
Wayi mʼanuonyam afi me so na watu mʼahenkyɛw afi me ti so.
10 Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu; Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.
Wasɛe me akwannuasa nyinaa so de awie me; watu mʼanidaso ase te sɛ dua.
11 Wandikwiyira ndipo akundiyesa mmodzi mwa adani ake.
Nʼabufuw huru tia me; na wakan me afra nʼatamfo mu.
12 Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu, akonzekera zodzalimbana nane ndipo azungulira nyumba yanga.
Nʼakofo ba anibere so; wosisi mpie de tia me na wotwa me ntamadan ho hyia.
13 “Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga; wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.
“Wayi me nuabarimanom afi me ho; na mʼamanifo atwe wɔn ho koraa.
14 Abale anga andithawa; abwenzi anga andiyiwala.
Mʼabusuafo kɔ; na me nnamfonom werɛ afi me.
15 Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo; ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.
Mʼahɔho ne me mmaawa bu me sɛ ɔhɔho; mete sɛ ɔnanani ma wɔn.
16 Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha, ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.
Mefrɛ me somfo, na ommua; mpo, metew mʼano srɛ no.
17 Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga; ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.
Me home bɔn me yere; me ho afono mʼankasa nuabarimanom.
18 Inde, ngakhale ana amandinyoza; akandiona amandinyodola.
Mpo, mmarimaa nkumaa bu me animtiaa; sɛ mipue a wodi me ho fɛw.
19 Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane; iwo amene ndinkawakonda andiwukira.
Me nnamfo ankasa nyinaa kyi me; mʼadɔfo asɔre atia me.
20 Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha; ndapulumuka lokumbakumba.
Maka were ne nnompe, nea mede aguan nkutoo ne me se akyi nam.
21 “Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni, pakuti dzanja la Mulungu landikantha.
“Munhu me mmɔbɔ, me nnamfonom, munhu mmɔbɔ, na Onyankopɔn nsa abɔ me.
22 Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu? Kodi simunatope nalo thupi langa?
Adɛn nti na motaa me sɛnea Onyankopɔn yɛ no? Na mommfa me honam yi saa ara?
23 “Aa, achikhala mawu anga analembedwa, achikhala analembedwa mʼbuku,
“Ao, sɛ anka wɔde me nsɛm bɛhyɛ nhoma mu, anka wɔbɛkyerɛw wɔ nhoma mmobɔwee so,
24 akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo, akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!
anka wɔde dade pɛe bɛkyerɛw wɔ sumpii so, anaa wobekuruakyerɛw wɔ ɔbotan so afebɔɔ!
25 Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo, ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.
Minim sɛ me dimafo te ase, na awiei no ɔbɛsɔre agyina asase so.
26 Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka, mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.
Na wɔasɛe me were awie no, mefi me were mu ahu Onyankopɔn.
27 Ine ndemwe ndidzamuona Iye ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi. Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!
Me ara mehu no mede mʼani, na ɛnyɛ obi foforo ani, behu no. Sɛnea me koma ho pere wɔ me mu!
28 “Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji, popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’
“Sɛ moka se, ‘Yɛbɛteetee no, efisɛ ɔhaw no fi ɔno ara a,’
29 Inu muyenera kuopa lupanga; pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga; zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”
ɛsɛ sɛ mo ankasa musuro afoa no na abufuw nam afoa so de asotwe bɛba, na mubehu sɛ atemmu wɔ hɔ.”

< Yobu 19 >