< Yobu 19 >
1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Eyüp şöyle yanıtladı:
2 “Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti, ndi kundilasa ndi mawu anuwo?
“Ne zamana dek beni üzecek, Sözlerinizle ezeceksiniz?
3 Inuyo mwandinyoza kwambiri; mwanditsutsa mopanda manyazi.
On kez oldu beni aşağılıyor, Hiç utanmadan saldırıyorsunuz.
4 Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera, cholakwachotu nʼchanga.
Yanlış yola sapmışsam, Bu benim suçum.
5 Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga, ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,
Kendinizi gerçekten benden üstün görüyor, Utancımı bana karşı kullanıyorsanız,
6 pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira ndipo wandizinga ukonde wake.
Bilin ki, Tanrı bana haksızlık yaptı, Beni ağıyla kuşattı.
7 “Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha; ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.
“İşte, ‘Zorbalık bu!’ diye haykırıyorum, ama yanıt yok, Yardım için bağırıyorum, ama adalet yok.
8 Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa; waphimba njira zanga ndi mdima.
Yoluma set çekti, geçemiyorum, Yollarımı karanlığa boğdu.
9 Iye wandilanda ulemu wanga ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.
Üzerimden onurumu soydu, Başımdaki tacı kaldırdı.
10 Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu; Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.
Her yandan yıktı beni, tükendim, Umudumu bir ağaç gibi kökünden söktü.
11 Wandikwiyira ndipo akundiyesa mmodzi mwa adani ake.
Öfkesi bana karşı alev alev yanıyor, Beni hasım sayıyor.
12 Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu, akonzekera zodzalimbana nane ndipo azungulira nyumba yanga.
Orduları üstüme üstüme geliyor, Bana karşı rampalar yapıyor, Çadırımın çevresinde ordugah kuruyorlar.
13 “Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga; wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.
“Kardeşlerimi benden uzaklaştırdı, Tanıdıklarım bana büsbütün yabancılaştı.
14 Abale anga andithawa; abwenzi anga andiyiwala.
Akrabalarım uğramaz oldu, Yakın dostlarım beni unuttu.
15 Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo; ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.
Evimdeki konuklarla hizmetçiler Beni yabancı sayıyor, Garip oldum gözlerinde.
16 Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha, ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.
Kölemi çağırıyorum, yanıtlamıyor, Dil döksem bile.
17 Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga; ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.
Soluğum karımı tiksindiriyor, Kardeşlerim benden iğreniyor.
18 Inde, ngakhale ana amandinyoza; akandiona amandinyodola.
Çocuklar bile beni küçümsüyor, Ayağa kalksam benimle eğleniyorlar.
19 Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane; iwo amene ndinkawakonda andiwukira.
Bütün yakın dostlarım benden iğreniyor, Sevdiklerim yüz çeviriyor.
20 Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha; ndapulumuka lokumbakumba.
Bir deri bir kemiğe döndüm, Ölümün eşiğine geldim.
21 “Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni, pakuti dzanja la Mulungu landikantha.
“Ey dostlarım, acıyın bana, siz acıyın, Çünkü Tanrı'nın eli vurdu bana.
22 Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu? Kodi simunatope nalo thupi langa?
Neden Tanrı gibi siz de beni kovalıyor, Etime doymuyorsunuz?
23 “Aa, achikhala mawu anga analembedwa, achikhala analembedwa mʼbuku,
“Keşke şimdi sözlerim yazılsa, Kitaba geçseydi,
24 akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo, akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!
Demir kalemle, kurşunla Sonsuza dek kalsın diye kayaya kazılsaydı!
25 Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo, ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.
Oysa ben kurtarıcımın yaşadığını, Sonunda yeryüzüne geleceğini biliyorum.
26 Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka, mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.
Derim yok olduktan sonra, Yeni bedenimle Tanrı'yı göreceğim.
27 Ine ndemwe ndidzamuona Iye ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi. Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!
O'nu kendim göreceğim, Kendi gözlerimle, başkası değil. Yüreğim bayılıyor bağrımda!
28 “Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji, popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’
Eğer, ‘Sıkıntının kökü onda olduğu için Onu kovalım’ diyorsanız,
29 Inu muyenera kuopa lupanga; pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga; zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”
Kılıçtan korkmalısınız, Çünkü kılıç cezası öfkeli olur, O zaman adaletin var olduğunu göreceksiniz.”