< Yobu 19 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
پس ایوب در جواب گفت:۱
2 “Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti, ndi kundilasa ndi mawu anuwo?
«تا به کی جان مرا می‌رنجانید؟ و مرا به سخنان خود فرسوده می‌سازید؟۲
3 Inuyo mwandinyoza kwambiri; mwanditsutsa mopanda manyazi.
این ده مرتبه است که مرا مذمت نمودید، و خجالت نمی کشید که با من سختی می‌کنید؟۳
4 Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera, cholakwachotu nʼchanga.
و اگر فی الحقیقه خطا کرده‌ام، خطای من نزد من می‌ماند.۴
5 Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga, ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,
اگر فی الواقع بر من تکبر نمایید و عار مرا بر من اثبات کنید،۵
6 pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira ndipo wandizinga ukonde wake.
پس بدانید که خدا دعوی مرا منحرف ساخته، و به دام خود مرا احاطه نموده است.۶
7 “Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha; ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.
اینک از ظلم، تضرع می‌نمایم و مستجاب نمی شوم و استغاثه می‌کنم و دادرسی نیست.۷
8 Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa; waphimba njira zanga ndi mdima.
طریق مرا حصارنموده است که از آن نمی توانم گذشت و برراههای من تاریکی را گذارده است.۸
9 Iye wandilanda ulemu wanga ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.
جلال مرا ازمن کنده است و تاج را از سر من برداشته،۹
10 Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu; Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.
مرا ازهر طرف خراب نموده، پس هلاک شدم. و مثل درخت، ریشه امید مرا کنده است.۱۰
11 Wandikwiyira ndipo akundiyesa mmodzi mwa adani ake.
غضب خودرا بر من افروخته، و مرا یکی از دشمنان خودشمرده است.۱۱
12 Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu, akonzekera zodzalimbana nane ndipo azungulira nyumba yanga.
فوجهای او با هم می‌آیند و راه خود را بر من بلند می‌کنند و به اطراف خیمه من اردو می‌زنند.۱۲
13 “Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga; wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.
«برادرانم را از نزد من دور کرده است وآشنایانم از من بالکل بیگانه شده‌اند.۱۳
14 Abale anga andithawa; abwenzi anga andiyiwala.
خویشانم مرا ترک نموده و آشنایانم مرا فراموش کرده‌اند.۱۴
15 Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo; ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.
نزیلان خانه‌ام و کنیزانم مرا غریب می‌شمارند، و در نظر ایشان بیگانه شده‌ام.۱۵
16 Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha, ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.
غلام خود راصدا می‌کنم و مرا جواب نمی دهد، اگر‌چه او را به دهان خود التماس بکنم.۱۶
17 Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga; ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.
نفس من نزد زنم مکروه شده است و تضرع من نزد اولاد رحم مادرم.۱۷
18 Inde, ngakhale ana amandinyoza; akandiona amandinyodola.
بچه های کوچک نیز مرا حقیرمی شمارند و چون برمی خیزم به ضد من حرف می‌زنند.۱۸
19 Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane; iwo amene ndinkawakonda andiwukira.
همه اهل مشورتم از من نفرت می‌نمایند، و کسانی را که دوست می‌داشتم از من برگشته‌اند.۱۹
20 Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha; ndapulumuka lokumbakumba.
استخوانم به پوست و گوشتم چسبیده است، و با پوست دندانهای خودخلاصی یافته‌ام.۲۰
21 “Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni, pakuti dzanja la Mulungu landikantha.
بر من ترحم کنید! ترحم کنیدشما‌ای دوستانم! زیرا دست خدا مرا لمس نموده است.۲۱
22 Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu? Kodi simunatope nalo thupi langa?
چرا مثل خدا بر من جفا می‌کنید وازگوشت من سیر نمی شوید.۲۲
23 “Aa, achikhala mawu anga analembedwa, achikhala analembedwa mʼbuku,
کاش که سخنانم الان نوشته می‌شد! کاش که در کتابی ثبت می‌گردید،۲۳
24 akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo, akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!
و با قلم آهنین و سرب بر صخره‌ای تا به ابد کنده می‌شد!۲۴
25 Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo, ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.
و من می‌دانم که ولی من زنده است، و در ایام آخر، بر زمین خواهدبرخاست.۲۵
26 Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka, mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.
و بعد از آنکه این پوست من تلف شود، بدون جسدم نیز خدا را خواهم دید.۲۶
27 Ine ndemwe ndidzamuona Iye ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi. Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!
ومن او را برای خود خواهم دید. و چشمان من بر اوخواهد نگریست و نه چشم دیگری. اگر‌چه گرده هایم در اندرونم تلف شده باشد.۲۷
28 “Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji, popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’
اگربگویید چگونه بر او جفا نماییم و حال آنگاه اصل امر در من یافت می‌شود.۲۸
29 Inu muyenera kuopa lupanga; pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga; zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”
پس از شمشیربترسید، زیرا که سزاهای شمشیر غضبناک است، تا دانسته باشید که داوری خواهد بود.»۲۹

< Yobu 19 >