< Yobu 19 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Wasephendula uJobe wathi:
2 “Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti, ndi kundilasa ndi mawu anuwo?
Koze kube nini lihlupha umphefumulo wami, lingiphahlaza ngamazwi?
3 Inuyo mwandinyoza kwambiri; mwanditsutsa mopanda manyazi.
Lezizikhathi ezilitshumi lingithela ngehlazo; kalilanhloni, lingiphatha kubi.
4 Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera, cholakwachotu nʼchanga.
Uba-ke kuliqiniso ukuthi ngiduhile, ukuduha kwami kuzahlala lami.
5 Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga, ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,
Uba isibili lizikhukhumeza phezu kwami, liphikisane lami ngehlazo lami,
6 pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira ndipo wandizinga ukonde wake.
yazini-ke ukuthi nguNkulunkulu ongihlanekeleyo, wangigombolozela ngembule lakhe.
7 “Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha; ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.
Khangela, ngiyamemeza ngithi: Okubi! Kodwa kangiphendulwa. Ngicela usizo, kodwa akulasahlulelo.
8 Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa; waphimba njira zanga ndi mdima.
Uyivalile indlela yami ngomduli ukuze ngingedluli, wamisa umnyama emikhondweni yami.
9 Iye wandilanda ulemu wanga ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.
Ungihlubule udumo lwami, wasusa umqhele wekhanda lami.
10 Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu; Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.
Ungibhidlizile inhlangothi zonke, sengihambile, ulisiphule ithemba lami njengesihlahla.
11 Wandikwiyira ndipo akundiyesa mmodzi mwa adani ake.
Ulumathisile ulaka lwakhe kimi, ungibale njengezitha zakhe kuye.
12 Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu, akonzekera zodzalimbana nane ndipo azungulira nyumba yanga.
Amabutho akhe afika kanyekanye, abuthelela indlela yawo emelene lami, amisa inkamba agombolozela ithente lami.
13 “Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga; wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.
Ubeke abafowethu khatshana lami, labangaziyo isibili sebengabemzini kimi.
14 Abale anga andithawa; abwenzi anga andiyiwala.
Izihlobo zami zinyamalele, labazana lami bangikhohliwe.
15 Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo; ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.
Abahlala endlini yami lencekukazi zami bangibala njengowezizwe; ngingumfokazi emehlweni abo.
16 Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha, ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.
Ngabiza inceku yami, kodwa kayiphendulanga; ngayincenga ngomlomo wami.
17 Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga; ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.
Umoya wami uyenyanyeka kumkami, sengiyisinengiso kumadodana esizalo sami.
18 Inde, ngakhale ana amandinyoza; akandiona amandinyodola.
Labantwana abancinyane bayangidelela; ngasukuma, basebekhuluma bemelene lami.
19 Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane; iwo amene ndinkawakonda andiwukira.
Bonke abantu besifuba sami banengwa yimi, labo ebengibathanda sebengiphendukele.
20 Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha; ndapulumuka lokumbakumba.
Ithambo lami linamathelana lesikhumba sami lenyama yami, njalo ngiphephe ngesikhumba samazinyo ami.
21 “Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni, pakuti dzanja la Mulungu landikantha.
Ngihawukelani, ngihawukelani, lina bangane bami; ngoba isandla sikaNkulunkulu singithintile.
22 Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu? Kodi simunatope nalo thupi langa?
Lingizingelelani njengoNkulunkulu, lingeneliswa yinyama yami?
23 “Aa, achikhala mawu anga analembedwa, achikhala analembedwa mʼbuku,
Kungathi ngabe khathesi amazwi ami abhaliwe! Kungathi ngabe acindezelwe egwalweni!
24 akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo, akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!
Ngabe abazwe ngepheni yensimbi langomnuso edwaleni kuze kube nininini!
25 Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo, ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.
Ngoba mina ngiyazi ukuthi umhlengi wami uyaphila, lekupheleni uzakuma emhlabathini.
26 Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka, mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.
Lapho sekutshabalalise lokhu emva kwesikhumba sami, kanti enyameni yami ngizambona uNkulunkulu,
27 Ine ndemwe ndidzamuona Iye ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi. Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!
mina engizazibonela yena, lamehlo ami azabona, hatshi omunye. Izinso zami seziphelile ngaphakathi kwami.
28 “Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji, popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’
Kodwa lithi: Kungani simzingela? Ngoba impande yendaba itholakala kimi.
29 Inu muyenera kuopa lupanga; pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga; zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”
Lina yesabeni inkemba, ngoba ulaka luletha izijeziso zenkemba, ukuze lazi ukuthi sikhona isahlulelo.

< Yobu 19 >