< Yobu 19 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Bet Ījabs atbildēja un sacīja:
2 “Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti, ndi kundilasa ndi mawu anuwo?
Cik ilgi jūs manu dvēseli bēdināsiet un mani mocīsiet ar vārdiem?
3 Inuyo mwandinyoza kwambiri; mwanditsutsa mopanda manyazi.
Jūs gan desmitkārt mani likuši kaunā un nekaunaties mani tā nomākt.
4 Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera, cholakwachotu nʼchanga.
Un ja es tiešām esmu maldījies, tad tā maldīšanās ir mana.
5 Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga, ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,
Vai tad jums tiešām tā bija lielīties pret mani un pierādīt manu kaunu?
6 pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira ndipo wandizinga ukonde wake.
Ņemiet jel vērā, kā Dievs mani lauzis un mani apvaldzinājis ar Savu tīklu.
7 “Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha; ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.
Redzi, es brēcu par varas darbu, bet man neatbild; es kliedzu pēc palīga, bet tiesas nav.
8 Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa; waphimba njira zanga ndi mdima.
Manam ceļam Viņš licis šķēršļus, ka netieku uz priekšu, un uz manām tekām Viņš licis tumsību.
9 Iye wandilanda ulemu wanga ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.
Manu godu Viņš man novilcis un atņēmis manas galvas kroni.
10 Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu; Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.
Viņš mani nopostījis visapkārt, ka eju bojā, un manu cerību Viņš izsakņojis kā koku.
11 Wandikwiyira ndipo akundiyesa mmodzi mwa adani ake.
Viņš iededzinājis Savu bardzību pret mani un mani tur kā Savu ienaidnieku.
12 Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu, akonzekera zodzalimbana nane ndipo azungulira nyumba yanga.
Viņa kara spēki sanākuši kopā un pret mani taisījuši savu ceļu un apmetuši lēģeri ap manu dzīvokli.
13 “Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga; wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.
Manus brāļus viņš atšķīris tālu no manis, un mani draugi man palikuši visai sveši.
14 Abale anga andithawa; abwenzi anga andiyiwala.
Mani tuvinieki atstājās, un mani draugi mani aizmirst.
15 Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo; ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.
Mana saime un manas kalpones tur mani par svešinieku, un es esmu kā svešs viņu acīs.
16 Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha, ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.
Es saucu savu kalpu, bet tas neatbild, tas man mīļi jālūdzās ar savu muti.
17 Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga; ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.
Mana dvaša riebj manai sievai, un mana smaka manas mātes bērniem.
18 Inde, ngakhale ana amandinyoza; akandiona amandinyodola.
Pat puikas mani nicina; kad es ceļos, tad tie man runā pretim.
19 Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane; iwo amene ndinkawakonda andiwukira.
Visi mani uzticamie draugi mani tur par negantību, un ko es mīlējis, tie ir griezušies pret mani.
20 Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha; ndapulumuka lokumbakumba.
Mani kauli līp pie manas ādas un pie manas miesas, un maniem zobiem āda vien atliek.
21 “Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni, pakuti dzanja la Mulungu landikantha.
Apžēlojaties par mani, apžēlojaties par mani, mani draugi! Jo Dieva roka mani aizskārusi.
22 Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu? Kodi simunatope nalo thupi langa?
Kāpēc jūs mani vajājat, kā tas stiprais Dievs, un no manas miesas nevarat pieēsties?
23 “Aa, achikhala mawu anga analembedwa, achikhala analembedwa mʼbuku,
Ak kaut mani vārdi taptu sarakstīti, ak kaut tie taptu iezīmēti grāmatā!
24 akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo, akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!
Kaut tie ar dzelzs kaltu un svinu par mūžīgu piemiņu taptu iecirsti akmenī.
25 Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo, ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.
Bet es zinu, ka mans Pestītājs dzīvs, un pēcgalā Viņš celsies pār pīšļiem.
26 Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka, mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.
Un kad mana āda, kas tā sasista, vairs nebūs, tad vaļā no savas miesas es skatīšu Dievu.
27 Ine ndemwe ndidzamuona Iye ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi. Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!
Tiešām, es Viņu sev skatīšu, un manas acis Viņu redzēs, un nebūs svešs. - Mana sirds iekš manis ilgojās.
28 “Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji, popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’
Kad jūs sakāt: Kā mēs to vajāsim? Un ka tā vaina pie manis atrasta:
29 Inu muyenera kuopa lupanga; pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga; zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”
Tad bīstaties no zobena; jo zobens ir tā bardzība par noziegumiem, lai jūs atzīstat, ka ir sodība.

< Yobu 19 >