< Yobu 19 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
respondens autem Iob dixit
2 “Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti, ndi kundilasa ndi mawu anuwo?
usquequo adfligitis animam meam et adteritis me sermonibus
3 Inuyo mwandinyoza kwambiri; mwanditsutsa mopanda manyazi.
en decies confunditis me et non erubescitis opprimentes me
4 Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera, cholakwachotu nʼchanga.
nempe et si ignoravi mecum erit ignorantia mea
5 Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga, ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,
at vos contra me erigimini et arguitis me obprobriis meis
6 pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira ndipo wandizinga ukonde wake.
saltim nunc intellegite quia Deus non aequo iudicio adflixerit me et flagellis suis me cinxerit
7 “Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha; ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.
ecce clamabo vim patiens et nemo audiet vociferabor et non est qui iudicet
8 Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa; waphimba njira zanga ndi mdima.
semitam meam circumsepsit et transire non possum et in calle meo tenebras posuit
9 Iye wandilanda ulemu wanga ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.
spoliavit me gloria mea et abstulit coronam de capite meo
10 Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu; Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.
destruxit me undique et pereo et quasi evulsae arbori abstulit spem meam
11 Wandikwiyira ndipo akundiyesa mmodzi mwa adani ake.
iratus est contra me furor eius et sic me habuit quasi hostem suum
12 Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu, akonzekera zodzalimbana nane ndipo azungulira nyumba yanga.
simul venerunt latrones eius et fecerunt sibi viam per me et obsederunt in gyro tabernaculum meum
13 “Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga; wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.
fratres meos longe fecit a me et noti mei quasi alieni recesserunt a me
14 Abale anga andithawa; abwenzi anga andiyiwala.
dereliquerunt me propinqui mei et qui me noverant obliti sunt mei
15 Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo; ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.
inquilini domus meae et ancillae meae sicut alienum habuerunt me et quasi peregrinus fui in oculis eorum
16 Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha, ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.
servum meum vocavi et non respondit ore proprio deprecabar illum
17 Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga; ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.
halitum meum exhorruit uxor mea et orabam filios uteri mei
18 Inde, ngakhale ana amandinyoza; akandiona amandinyodola.
stulti quoque despiciebant me et cum ab eis recessissem detrahebant mihi
19 Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane; iwo amene ndinkawakonda andiwukira.
abominati sunt me quondam consiliarii mei et quem maxime diligebam aversatus est me
20 Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha; ndapulumuka lokumbakumba.
pelli meae consumptis carnibus adhesit os meum et derelicta sunt tantummodo labia circa dentes meos
21 “Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni, pakuti dzanja la Mulungu landikantha.
miseremini mei miseremini mei saltim vos amici mei quia manus Domini tetigit me
22 Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu? Kodi simunatope nalo thupi langa?
quare persequimini me sicut Deus et carnibus meis saturamini
23 “Aa, achikhala mawu anga analembedwa, achikhala analembedwa mʼbuku,
quis mihi tribuat ut scribantur sermones mei quis mihi det ut exarentur in libro
24 akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo, akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!
stilo ferreo et plumbi lammina vel certe sculpantur in silice
25 Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo, ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.
scio enim quod redemptor meus vivat et in novissimo de terra surrecturus sim
26 Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka, mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.
et rursum circumdabor pelle mea et in carne mea videbo Deum
27 Ine ndemwe ndidzamuona Iye ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi. Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!
quem visurus sum ego ipse et oculi mei conspecturi sunt et non alius reposita est haec spes mea in sinu meo
28 “Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji, popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’
quare ergo nunc dicitis persequamur eum et radicem verbi inveniamus contra eum
29 Inu muyenera kuopa lupanga; pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga; zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”
fugite ergo a facie gladii quoniam ultor iniquitatum gladius est et scitote esse iudicium

< Yobu 19 >