< Yobu 19 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Giobbe allora rispose:
2 “Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti, ndi kundilasa ndi mawu anuwo?
Fino a quando mi tormenterete e mi opprimerete con le vostre parole?
3 Inuyo mwandinyoza kwambiri; mwanditsutsa mopanda manyazi.
Son dieci volte che mi insultate e mi maltrattate senza pudore.
4 Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera, cholakwachotu nʼchanga.
E' poi vero che io abbia mancato e che persista nel mio errore?
5 Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga, ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,
Non è forse vero che credete di vincere contro di me, rinfacciandomi la mia abiezione?
6 pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira ndipo wandizinga ukonde wake.
Sappiate dunque che Dio mi ha piegato e mi ha avviluppato nella sua rete.
7 “Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha; ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.
Ecco, grido contro la violenza, ma non ho risposta, chiedo aiuto, ma non c'è giustizia!
8 Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa; waphimba njira zanga ndi mdima.
Mi ha sbarrato la strada perché non passi e sul mio sentiero ha disteso le tenebre.
9 Iye wandilanda ulemu wanga ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.
Mi ha spogliato della mia gloria e mi ha tolto dal capo la corona.
10 Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu; Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.
Mi ha disfatto da ogni parte e io sparisco, mi ha strappato, come un albero, la speranza.
11 Wandikwiyira ndipo akundiyesa mmodzi mwa adani ake.
Ha acceso contro di me la sua ira e mi considera come suo nemico.
12 Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu, akonzekera zodzalimbana nane ndipo azungulira nyumba yanga.
Insieme sono accorse le sue schiere e si sono spianata la strada contro di me; hanno posto l'assedio intorno alla mia tenda.
13 “Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga; wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.
I miei fratelli si sono allontanati da me, persino gli amici mi si sono fatti stranieri.
14 Abale anga andithawa; abwenzi anga andiyiwala.
Scomparsi sono vicini e conoscenti, mi hanno dimenticato gli ospiti di casa;
15 Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo; ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.
da estraneo mi trattano le mie ancelle, un forestiero sono ai loro occhi.
16 Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha, ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.
Chiamo il mio servo ed egli non risponde, devo supplicarlo con la mia bocca.
17 Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga; ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.
Il mio fiato è ripugnante per mia moglie e faccio schifo ai figli di mia madre.
18 Inde, ngakhale ana amandinyoza; akandiona amandinyodola.
Anche i monelli hanno ribrezzo di me: se tento d'alzarmi, mi danno la baia.
19 Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane; iwo amene ndinkawakonda andiwukira.
Mi hanno in orrore tutti i miei confidenti: quelli che amavo si rivoltano contro di me.
20 Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha; ndapulumuka lokumbakumba.
Alla pelle si attaccano le mie ossa e non è salva che la pelle dei miei denti.
21 “Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni, pakuti dzanja la Mulungu landikantha.
Pietà, pietà di me, almeno voi miei amici, perché la mano di Dio mi ha percosso!
22 Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu? Kodi simunatope nalo thupi langa?
Perché vi accanite contro di me, come Dio, e non siete mai sazi della mia carne?
23 “Aa, achikhala mawu anga analembedwa, achikhala analembedwa mʼbuku,
Oh, se le mie parole si scrivessero, se si fissassero in un libro,
24 akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo, akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!
fossero impresse con stilo di ferro sul piombo, per sempre s'incidessero sulla roccia!
25 Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo, ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.
Io lo so che il mio Vendicatore è vivo e che, ultimo, si ergerà sulla polvere!
26 Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka, mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.
Dopo che questa mia pelle sarà distrutta, senza la mia carne, vedrò Dio.
27 Ine ndemwe ndidzamuona Iye ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi. Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!
Io lo vedrò, io stesso, e i miei occhi lo contempleranno non da straniero. Le mie viscere si consumano dentro di me.
28 “Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji, popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’
Poiché dite: «Come lo perseguitiamo noi, se la radice del suo danno è in lui?»,
29 Inu muyenera kuopa lupanga; pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga; zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”
temete per voi la spada, poiché punitrice d'iniquità è la spada, affinchè sappiate che c'è un giudice.

< Yobu 19 >