< Yobu 19 >
1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Alors Job prit la parole, et dit:
2 “Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti, ndi kundilasa ndi mawu anuwo?
Jusques à quand affligerez-vous mon âme, et m'accablerez-vous de paroles?
3 Inuyo mwandinyoza kwambiri; mwanditsutsa mopanda manyazi.
Voilà déjà dix fois que vous m'outragez: vous n'avez pas honte de me maltraiter?
4 Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera, cholakwachotu nʼchanga.
Vraiment si j'ai failli, ma faute demeure avec moi.
5 Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga, ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,
Si vraiment vous vous élevez contre moi, si vous me reprochez l'opprobre où je me trouve,
6 pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira ndipo wandizinga ukonde wake.
Sachez donc que c'est Dieu qui m'a fait tort, et qui a tendu ses filets autour de moi.
7 “Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha; ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.
Voici, je crie à la violence, et on ne me répond pas; je crie au secours, et il n'y a point de justice!
8 Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa; waphimba njira zanga ndi mdima.
Il a fermé mon chemin, et je ne puis passer; il a mis des ténèbres sur mes sentiers.
9 Iye wandilanda ulemu wanga ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.
Il m'a dépouillé de ma gloire; il a ôté la couronne de ma tête.
10 Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu; Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.
Il m'a détruit de tous côtés, et je m'en vais; il a arraché, comme un arbre, mon espérance.
11 Wandikwiyira ndipo akundiyesa mmodzi mwa adani ake.
Il a allumé sa colère contre moi, et il m'a tenu pour l'un de ses ennemis.
12 Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu, akonzekera zodzalimbana nane ndipo azungulira nyumba yanga.
Ses troupes sont venues en-semble; elles ont dressé contre moi leurs chaussées, et se sont campées autour de ma tente.
13 “Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga; wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.
Il a éloigné de moi mes frères, et ceux qui me connaissaient se sont écartés comme des étrangers;
14 Abale anga andithawa; abwenzi anga andiyiwala.
Mes proches m'ont abandonné, et mes connaissances m'ont oublié.
15 Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo; ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.
Les hôtes de ma maison et mes servantes m'ont traité comme un étranger; je suis devenu un inconnu pour eux.
16 Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha, ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.
J'ai appelé mon serviteur, il ne m'a pas répondu; de ma propre bouche, j'ai dû le supplier.
17 Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga; ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.
Mon haleine est insupportable à ma femme, et ma prière aux fils de ma mère.
18 Inde, ngakhale ana amandinyoza; akandiona amandinyodola.
Les petits enfants eux-mêmes me méprisent: si je veux me lever, ils parlent contre moi.
19 Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane; iwo amene ndinkawakonda andiwukira.
Tous mes intimes m'ont en abomination, et ceux que j'aimais se sont tournés contre moi.
20 Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha; ndapulumuka lokumbakumba.
Mes os se sont attachés à ma peau et à ma chair, et je me suis échappé avec la peau de mes dents.
21 “Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni, pakuti dzanja la Mulungu landikantha.
Ayez pitié de moi, ayez pitié de moi, vous, mes amis! Car la main de Dieu m'a frappé.
22 Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu? Kodi simunatope nalo thupi langa?
Pourquoi me persécutez-vous comme Dieu, et ne pouvez-vous vous rassasier de ma chair?
23 “Aa, achikhala mawu anga analembedwa, achikhala analembedwa mʼbuku,
Oh! je voudrais que mes paroles fussent écrites quelque part! Je voudrais qu'elles fussent inscrites dans un livre;
24 akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo, akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!
Qu'avec un burin de fer et avec du plomb, elles fussent gravées sur le roc, pour toujours!
25 Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo, ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.
Pour moi, je sais que mon Rédempteur est vivant, qu'à la fin il se lèvera sur la terre,
26 Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka, mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.
Et qu'après cette peau qui se détruit, et hors de ma chair, je verrai Dieu;
27 Ine ndemwe ndidzamuona Iye ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi. Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!
Moi, je le verrai, à moi propice; mes yeux le verront, et non un autre. Mes reins se consument en mon sein!
28 “Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji, popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’
Si vous dites: Comment le poursuivrons-nous, et trouverons-nous en lui la cause de son malheur?
29 Inu muyenera kuopa lupanga; pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga; zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”
Craignez l'épée pour vous-mêmes, car la fureur est un crime digne de l'épée, afin que vous sachiez qu'il y a un jugement.