< Yobu 19 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
And Job answereth and saith: —
2 “Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti, ndi kundilasa ndi mawu anuwo?
Till when do ye afflict my soul, And bruise me with words?
3 Inuyo mwandinyoza kwambiri; mwanditsutsa mopanda manyazi.
These ten times ye put me to shame, ye blush not. Ye make yourselves strange to me —
4 Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera, cholakwachotu nʼchanga.
And also — truly, I have erred, With me doth my error remain.
5 Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga, ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,
If, truly, over me ye magnify yourselves, And decide against me my reproach;
6 pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira ndipo wandizinga ukonde wake.
Know now, that God turned me upside down, And His net against me hath set round,
7 “Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha; ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.
Lo, I cry out — violence, and am not answered, I cry aloud, and there is no judgment.
8 Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa; waphimba njira zanga ndi mdima.
My way He hedged up, and I pass not over, And on my paths darkness He placeth.
9 Iye wandilanda ulemu wanga ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.
Mine honour from off me He hath stripped, And He turneth the crown from my head.
10 Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu; Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.
He breaketh me down round about, and I go, And removeth like a tree my hope.
11 Wandikwiyira ndipo akundiyesa mmodzi mwa adani ake.
And He kindleth against me His anger, And reckoneth me to Him as His adversaries.
12 Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu, akonzekera zodzalimbana nane ndipo azungulira nyumba yanga.
Come in do His troops together, And they raise up against me their way, And encamp round about my tent.
13 “Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga; wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.
My brethren from me He hath put far off, And mine acquaintances surely Have been estranged from me.
14 Abale anga andithawa; abwenzi anga andiyiwala.
Ceased have my neighbours And my familiar friends have forgotten me,
15 Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo; ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.
Sojourners of my house and my maids, For a stranger reckon me: An alien I have been in their eyes.
16 Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha, ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.
To my servant I have called, And he doth not answer, With my mouth I make supplication to him.
17 Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga; ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.
My spirit is strange to my wife, And my favours to the sons of my [mother's] womb.
18 Inde, ngakhale ana amandinyoza; akandiona amandinyodola.
Also sucklings have despised me, I rise, and they speak against me.
19 Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane; iwo amene ndinkawakonda andiwukira.
Abominate me do all the men of my counsel, And those I have loved, Have been turned against me.
20 Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha; ndapulumuka lokumbakumba.
To my skin and to my flesh Cleaved hath my bone, And I deliver myself with the skin of my teeth.
21 “Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni, pakuti dzanja la Mulungu landikantha.
Pity me, pity me, ye my friends, For the hand of God hath stricken against me.
22 Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu? Kodi simunatope nalo thupi langa?
Why do you pursue me as God? And with my flesh are not satisfied?
23 “Aa, achikhala mawu anga analembedwa, achikhala analembedwa mʼbuku,
Who doth grant now, That my words may be written? Who doth grant that in a book they may be graven?
24 akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo, akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!
With a pen of iron and lead — For ever in a rock they may be hewn.
25 Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo, ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.
That — I have known my Redeemer, The Living and the Last, For the dust he doth rise.
26 Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka, mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.
And after my skin hath compassed this [body], Then from my flesh I see God:
27 Ine ndemwe ndidzamuona Iye ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi. Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!
Whom I — I see on my side, And mine eyes have beheld, and not a stranger, Consumed have been my reins in my bosom.
28 “Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji, popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’
But ye say, 'Why do we pursue after him?' And the root of the matter hath been found in me.
29 Inu muyenera kuopa lupanga; pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga; zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”
Be ye afraid because of the sword, For furious [are] the punishments of the sword, That ye may know that [there is] a judgment.

< Yobu 19 >