< Yobu 19 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Forsothe Joob answeride, and seide, Hou long turmente ye my soule,
2 “Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti, ndi kundilasa ndi mawu anuwo?
and al to-breken me with wordis?
3 Inuyo mwandinyoza kwambiri; mwanditsutsa mopanda manyazi.
Lo! ten sithis ye schenden me, and ye ben not aschamed, oppressynge me.
4 Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera, cholakwachotu nʼchanga.
Forsothe and if Y `koude not, myn vnkynnyng schal be with me.
5 Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga, ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,
And ye ben reisid ayens me, and repreuen me with my schenschipis.
6 pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira ndipo wandizinga ukonde wake.
Nameli now vndurstonde ye, that God hath turmentid me not bi euene doom, and hath cumpassid me with hise betyngis.
7 “Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha; ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.
Lo! Y suffrynge violence schal crye, and no man schal here; Y schal crye loude, and `noon is that demeth.
8 Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa; waphimba njira zanga ndi mdima.
He bisette aboute my path, and Y may not go; and he settide derknessis in my weie.
9 Iye wandilanda ulemu wanga ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.
He hath spuylid me of my glorye, and hath take awey the coroun fro myn heed.
10 Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu; Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.
He hath distried me on ech side, and Y perischide; and he hath take awei myn hope, as fro a tre pullid vp bi the roote.
11 Wandikwiyira ndipo akundiyesa mmodzi mwa adani ake.
His stronge veniaunce was wrooth ayens me; and he hadde me so as his enemye.
12 Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu, akonzekera zodzalimbana nane ndipo azungulira nyumba yanga.
Hise theues camen togidere, and `maden to hem a wei bi me; and bisegiden my tabernacle in cumpas.
13 “Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga; wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.
He made fer my britheren fro me; and my knowun as aliens yeden awei fro me.
14 Abale anga andithawa; abwenzi anga andiyiwala.
My neiyboris forsoken me; and thei that knewen me han foryete me.
15 Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo; ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.
The tenauntis of myn hows, and myn handmaydis hadden me as a straunger; and Y was as a pilgrym bifor her iyen.
16 Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha, ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.
Y clepide my seruaunt, and he answeride not to me; with myn owne mouth Y preiede hym.
17 Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga; ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.
My wijf wlatide my breeth; and Y preiede the sones of my wombe.
18 Inde, ngakhale ana amandinyoza; akandiona amandinyodola.
Also foolis dispisiden me; and whanne Y was goon awei fro hem, thei bacbitiden me.
19 Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane; iwo amene ndinkawakonda andiwukira.
Thei, that weren my counselouris sum tyme, hadden abhomynacioun of me; and he, whom Y louede moost, was aduersarie to me.
20 Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha; ndapulumuka lokumbakumba.
Whanne fleischis weren wastid, my boon cleuyde to my skyn; and `oneli lippis ben left aboute my teeth.
21 “Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni, pakuti dzanja la Mulungu landikantha.
Haue ye merci on me, haue ye merci on me, nameli, ye my frendis; for the hond of the Lord hath touchid me.
22 Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu? Kodi simunatope nalo thupi langa?
Whi pursuen ye me, as God pursueth; and ben fillid with my fleischis?
23 “Aa, achikhala mawu anga analembedwa, achikhala analembedwa mʼbuku,
Who yyueth to me, that my wordis be writun? Who yyueth to me,
24 akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo, akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!
that tho be writun in a book with an yrun poyntil, ethir with a plate of leed; ethir with a chisel be grauun in a flynt?
25 Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo, ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.
For Y woot, that myn ayenbiere lyueth, and in the laste dai Y schal rise fro the erthe;
26 Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka, mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.
and eft Y schal be cumpassid with my skyn, and in my fleisch Y schal se God, my sauyour.
27 Ine ndemwe ndidzamuona Iye ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi. Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!
Whom Y my silf schal se, and myn iyen schulen biholde, and not an other man. This myn hope is kept in my bosum.
28 “Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji, popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’
Whi therfor seien ye now, Pursue we hym, and fynde we the roote of a word ayens hym?
29 Inu muyenera kuopa lupanga; pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga; zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”
Therfor fle ye fro the face of the swerd; for the swerd is the vengere of wickidnessis, and wite ye, that doom schal be.

< Yobu 19 >