< Yobu 19 >
1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Then Job answered and said,
2 “Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti, ndi kundilasa ndi mawu anuwo?
How long will ye vex my soul, and break me in pieces with words?
3 Inuyo mwandinyoza kwambiri; mwanditsutsa mopanda manyazi.
These ten times have ye reproached me: ye are not ashamed [that] ye make yourselves strange to me.
4 Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera, cholakwachotu nʼchanga.
And be it indeed [that] I have erred, my error remaineth with myself.
5 Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga, ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,
If indeed ye will magnify [yourselves] against me, and plead against me my reproach:
6 pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira ndipo wandizinga ukonde wake.
Know now that God hath overthrown me, and hath encompassed me with his net.
7 “Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha; ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.
Behold, I cry out of wrong, but I am not heard: I cry aloud, but [there is] no judgment.
8 Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa; waphimba njira zanga ndi mdima.
He hath fenced up my way that I cannot pass, and he hath set darkness in my paths.
9 Iye wandilanda ulemu wanga ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.
He hath stripped me of my glory, and taken the crown [from] my head.
10 Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu; Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.
He hath destroyed me on every side, and I am gone: and my hope hath he removed like a tree.
11 Wandikwiyira ndipo akundiyesa mmodzi mwa adani ake.
He hath also kindled his wrath against me, and he counteth me to him as [one of] his enemies.
12 Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu, akonzekera zodzalimbana nane ndipo azungulira nyumba yanga.
His troops come together, and raise up their way against me, and encamp around my tabernacle.
13 “Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga; wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.
He hath put my brethren far from me, and my acquaintance are verily estranged from me.
14 Abale anga andithawa; abwenzi anga andiyiwala.
My kinsmen have failed, and my familiar friends have forgotten me.
15 Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo; ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.
They that dwell in my house, and my maids, count me for a stranger: I am an alien in their sight.
16 Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha, ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.
I called my servant, and he gave [me] no answer; I entreated him with my mouth.
17 Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga; ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.
My breath is strange to my wife, though I entreated for the children's [sake] of my own body.
18 Inde, ngakhale ana amandinyoza; akandiona amandinyodola.
Yes, young children despised me; I arose, and they spoke against me.
19 Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane; iwo amene ndinkawakonda andiwukira.
All my intimate friends abhorred me: and they whom I loved are turned against me.
20 Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha; ndapulumuka lokumbakumba.
My bone cleaveth to my skin and to my flesh, and I have escaped with the skin of my teeth.
21 “Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni, pakuti dzanja la Mulungu landikantha.
Have pity upon me, have pity upon me, O ye my friends; for the hand of God hath touched me.
22 Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu? Kodi simunatope nalo thupi langa?
Why do ye persecute me as God, and are not satisfied with my flesh?
23 “Aa, achikhala mawu anga analembedwa, achikhala analembedwa mʼbuku,
Oh that my words were now written! oh that they were printed in a book!
24 akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo, akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!
That they were graven with an iron pen in lead, in the rock for ever!
25 Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo, ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.
For I know [that] my redeemer liveth, and [that] he will stand at the latter [day] upon the earth:
26 Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka, mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.
And [though] after my skin [worms] destroy this [body], yet in my flesh shall I see God:
27 Ine ndemwe ndidzamuona Iye ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi. Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!
Whom I shall see for myself, and my eyes shall behold, and not another; [though] my reins be consumed within me.
28 “Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji, popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’
But ye would say, Why persecute we him, seeing the root of the matter is found in me?
29 Inu muyenera kuopa lupanga; pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga; zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”
Be ye afraid of the sword: for wrath [bringeth] the punishments of the sword, that ye may know [there] is a judgment.