< Yobu 19 >
1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Job replied,
2 “Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti, ndi kundilasa ndi mawu anuwo?
“How long will you go on tormenting me? How long will you go on crushing me with words?
3 Inuyo mwandinyoza kwambiri; mwanditsutsa mopanda manyazi.
Ten times already you have humiliated me. Aren't you ashamed for treating me so badly?
4 Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera, cholakwachotu nʼchanga.
Even if I did sin, that's my problem, and has nothing to do with you.
5 Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga, ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,
You think you're so much better than me, and you use my degradation against me.
6 pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira ndipo wandizinga ukonde wake.
But you should realize that it's God who has wronged me, he has trapped me in his net.
7 “Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha; ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.
Even though I cry for help, I get no answer; even though I shout my objections, I get no justice.
8 Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa; waphimba njira zanga ndi mdima.
God has walled me in so I can't escape; he has plunged my path into darkness.
9 Iye wandilanda ulemu wanga ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.
He has stripped my honor from me; he has taken away my reputation.
10 Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu; Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.
He tears me down from all sides until I am finished; he has destroyed my hope like a tree that is uprooted.
11 Wandikwiyira ndipo akundiyesa mmodzi mwa adani ake.
His anger burns against me; he treats me as one of his enemies.
12 Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu, akonzekera zodzalimbana nane ndipo azungulira nyumba yanga.
God's troops assemble to attack me. They build ramparts against me. They encircle and besiege my home.
13 “Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga; wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.
He has driven my brothers far away from me; all my former friends are estranged from me.
14 Abale anga andithawa; abwenzi anga andiyiwala.
My relatives have abandoned me; my close friends have forgotten me.
15 Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo; ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.
My house guests and my maidservants treat me as a stranger—to them I have become a foreigner.
16 Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha, ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.
I call my servant, but he doesn't reply. I have to beg him!
17 Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga; ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.
I am repulsive to my wife, and I am loathsome to my own brothers.
18 Inde, ngakhale ana amandinyoza; akandiona amandinyodola.
Even young children despise me; when I stand up they ridicule me.
19 Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane; iwo amene ndinkawakonda andiwukira.
All my closest friends despise me, and those I loved have turned on me.
20 Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha; ndapulumuka lokumbakumba.
I've been reduced to skin and bones and I survive by the skin of my teeth.
21 “Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni, pakuti dzanja la Mulungu landikantha.
Have pity on me, my friends, have pity on me, because God has struck me down!
22 Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu? Kodi simunatope nalo thupi langa?
Why are you persecuting me like God does? Aren't you satisfied with getting your pound of flesh?
23 “Aa, achikhala mawu anga analembedwa, achikhala analembedwa mʼbuku,
I wish my words could be written down, recorded in a book,
24 akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo, akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!
or engraved with an iron pen and molten lead in the rock forever.
25 Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo, ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.
I know my Redeemer is alive, and that he shall finally take the stand for me on the earth.
26 Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka, mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.
Even though my skin is destroyed, in my body I shall see God.
27 Ine ndemwe ndidzamuona Iye ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi. Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!
I myself will see him—with my own eyes, and not those of someone else! The thought overcomes me!
28 “Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji, popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’
You say to yourselves, ‘How can we make him suffer so he can see he is the source of his problems?’
29 Inu muyenera kuopa lupanga; pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga; zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”
You yourselves should fear being punished by God, for you know anger brings God's punishment that accompanies judgment.”