< Yobu 19 >
1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
But Job answered by saying:
2 “Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti, ndi kundilasa ndi mawu anuwo?
How long will you afflict my soul and wear me down with words?
3 Inuyo mwandinyoza kwambiri; mwanditsutsa mopanda manyazi.
So, ten times you confound me and are not ashamed to oppress me.
4 Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera, cholakwachotu nʼchanga.
Now, of course, if I have been ignorant, my ignorance will be with me.
5 Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga, ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,
But you have risen up against me, and you accuse me to my disgrace.
6 pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira ndipo wandizinga ukonde wake.
At least now you should understand that God has not afflicted me with a balanced judgment, though he has encompassed me with his scourges.
7 “Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha; ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.
Behold, I will cry out, enduring violence, and no one will hear. I will announce loudly, but there is no one who may judge.
8 Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa; waphimba njira zanga ndi mdima.
He has hemmed in my path, and I cannot pass; he has added darkness to my difficult path.
9 Iye wandilanda ulemu wanga ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.
He has plundered me of my glory, and he has stolen the crown from my head.
10 Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu; Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.
He has destroyed me on every side, and I am lost, and, like an uprooted tree, he has taken away my hope.
11 Wandikwiyira ndipo akundiyesa mmodzi mwa adani ake.
His fury has raged against me, and in this way he has treated me like his enemy.
12 Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu, akonzekera zodzalimbana nane ndipo azungulira nyumba yanga.
His troops have gathered together, and they have made their way to me, and they have besieged my tabernacle all around.
13 “Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga; wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.
He has put my brothers far from me, and my friends have withdrawn from me like strangers.
14 Abale anga andithawa; abwenzi anga andiyiwala.
My kinsmen have forsaken me, and those who knew me, have forgotten me.
15 Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo; ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.
The inhabitants of my house and my maidservants treat me just as if I were a stranger, and I have been like a sojourner in their eyes.
16 Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha, ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.
I called my servant, and he did not respond; I pleaded with him with my own mouth.
17 Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga; ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.
My wife has shuddered at my breath, and I have begged the sons of my loins.
18 Inde, ngakhale ana amandinyoza; akandiona amandinyodola.
Even the foolish have looked down on me, and, when I withdrew from them, they spoke ill of me.
19 Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane; iwo amene ndinkawakonda andiwukira.
Those who were sometimes my counselors, treat me like an abomination; and he whom I valued the most has turned against me.
20 Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha; ndapulumuka lokumbakumba.
Since my flesh has been consumed, my bone adheres to my skin, and only my lips have been left around my teeth.
21 “Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni, pakuti dzanja la Mulungu landikantha.
Have mercy on me, have compassion on me, at least you my friends, because the hand of the Lord has touched me.
22 Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu? Kodi simunatope nalo thupi langa?
Why do you pursue me just as God does, and satiate yourselves with my flesh?
23 “Aa, achikhala mawu anga analembedwa, achikhala analembedwa mʼbuku,
Who will grant to me that my words may be written down? Who will grant to me that they may be inscribed in a book,
24 akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo, akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!
with an iron pen and a plate of lead, or else be carved in stone?
25 Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo, ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.
For I know that my Redeemer lives, and on the last day I will rise out of the earth.
26 Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka, mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.
And I will be enveloped again with my skin, and in my flesh I will see my God.
27 Ine ndemwe ndidzamuona Iye ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi. Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!
It is he whom I myself will see, and he whom my eyes will behold, and no other. This, my hope, has taken rest in my bosom.
28 “Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji, popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’
Why then do you now say: “Let us pursue him, and let us find a basis to speak against him?”
29 Inu muyenera kuopa lupanga; pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga; zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”
So then, flee from the face of the sword, for the sword is the avenger of iniquities; but know this: there is to be a judgment.