< Yobu 19 >
1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Så tog Job til Orde og svarede:
2 “Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti, ndi kundilasa ndi mawu anuwo?
"Hvor længe vil I krænke min Sjæl og slå mig sønder med Ord?
3 Inuyo mwandinyoza kwambiri; mwanditsutsa mopanda manyazi.
I håner mig nu for tiende Gang, mishandler mig uden Skam.
4 Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera, cholakwachotu nʼchanga.
Har jeg da virkelig fejlet, hænger der Fejl ved mig?
5 Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga, ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,
Eller gør I jer store imod mig og revser mig ved at smæde?
6 pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira ndipo wandizinga ukonde wake.
Så vid da, at Gud har bøjet min Ret, omspændt mig med sit Net.
7 “Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha; ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.
Se, jeg skriger: Vold! men får ikke Svar, råber om Hjælp, der er ingen Ret.
8 Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa; waphimba njira zanga ndi mdima.
Han spærred min Vej, jeg kom ikke frem, han hylled mine Stier i Mørke;
9 Iye wandilanda ulemu wanga ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.
han klædte mig af for min Ære, berøved mit Hoved Kronen,
10 Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu; Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.
brød mig ned overalt, så jeg må bort, oprykked mit Håb som Træet;
11 Wandikwiyira ndipo akundiyesa mmodzi mwa adani ake.
hans Vrede blussede mod mig, han regner mig for sin Fjende;
12 Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu, akonzekera zodzalimbana nane ndipo azungulira nyumba yanga.
samlede rykker hans Flokke frem og bryder sig Vej imod mig, de lejrer sig om mit Telt.
13 “Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga; wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.
Mine Brødre har fjernet sig fra mig, Venner er fremmede for mig,
14 Abale anga andithawa; abwenzi anga andiyiwala.
mine nærmeste og Hendinge holder sig fra mig, de, der er i mit Hus, har glemt mig;
15 Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo; ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.
mine Piger regner mig for en fremmed, vildfremmed er jeg i deres Øjne;
16 Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha, ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.
ej svarer min Træl, når jeg kalder, jeg må trygle ham med min Mund;
17 Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga; ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.
ved min Ånde væmmes min Hustru, mine egne Brødre er jeg en Stank;
18 Inde, ngakhale ana amandinyoza; akandiona amandinyodola.
selv Drenge agter mig ringe, når jeg reljser mig, taler de mod mig;
19 Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane; iwo amene ndinkawakonda andiwukira.
Standsfælleræmmes til Hobe ved mig, de, jeg elskede, vender sig mod mig.
20 Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha; ndapulumuka lokumbakumba.
Benene hænger fast ved min Hud, med Kødet i Tænderne slap jeg bort.
21 “Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni, pakuti dzanja la Mulungu landikantha.
Nåde, mine Venner, Nåde, thi Guds Hånd har rørt mig!
22 Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu? Kodi simunatope nalo thupi langa?
Hvi forfølger og I mig som Gud og mættes ej af mit Kød?
23 “Aa, achikhala mawu anga analembedwa, achikhala analembedwa mʼbuku,
Ak, gid mine Ord blev skrevet op, blev tegnet op i en Bog,
24 akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo, akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!
med Griffel af Jern, med Bly indristet i Hlippen for evigt!
25 Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo, ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.
Men jeg ved, at min Løser lever, over Støvet vil en Forsvarer stå frem.
26 Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka, mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.
Når min sønderslidte Hud er borte, skal jeg ud fra mit Kød skue Gud,
27 Ine ndemwe ndidzamuona Iye ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi. Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!
hvem jeg skal se på min Side; ham skal mine Øjne se, ingen fremmed! Mine Nyrer forgår i mit Indre!
28 “Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji, popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’
Når I siger: "Hor vi skal forfølge ham, Sagens Rod vil vi udfinde hos ham!"
29 Inu muyenera kuopa lupanga; pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga; zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”
så tag jer i Vare for Sværdet; thi Vrede rammer de lovløse, at I skal kende, der kommer en Dom!